< 1 Chroniques 19 >

1 Et Naas, roi des fils d'Ammon, mourut, et Anan (Annon), son fils, régna à sa place.
Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Et David dit: Je serai miséricordieux envers Anan, fils de Naas, de même que son père a été miséricordieux pour moi. En conséquence, il envoya des serviteurs pour le consoler au sujet de son père, et les serviteurs de David allèrent en la terre des fils d'Ammon, auprès d'Anan, pour le consoler.
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
3 Mais, les princes des fils d'Ammon dirent à Anan: Est-ce pour glorifier devant toi ton père que David envoie ces consolateurs? N'est-ce point plutôt pour s'informer de ta ville et pour là reconnaître que ses serviteurs sont venus près de toi?
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Anan saisit donc les serviteurs de David; il leur rasa la barbe; il coupa leurs manteaux, depuis le milieu du corps jusqu'aux pieds; puis, il les chassa.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
5 On vint dire à David ce qui leur était arrivé, et il envoya des gens à leur rencontre; car ils étaient cruellement déshonorés, et il leur dit: Demeurez à Jéricho jusqu'à ce que votre barbe ait repoussé; puis, alors vous reviendrez.
Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Les fils d'Ammon, voyant que le peuple d'Israël se tenait pour outragé, Anan et les fils d'Ammon envoyèrent mille talents d'argent pour enrôler des chars et des cavaliers dans la Syrie de Mésopotamie, dans la Syrie Maacha et à Sobal.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
7 Ils enrôlèrent ainsi pour eux trente-deux mille chars, et le roi de Maacha avec tout son peuple. Ces auxiliaires vinrent, et ils campèrent vis-à-vis Médaba. Cependant, les fils d'Ammon, sortant de leurs villes, se rassemblèrent, et ils s'ébranlèrent pour combattre.
Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
8 David l'apprit, et il mit en mouvement Joab avec toute l'armée des hommes vaillants.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
9 Et les fils d'Ammon sortirent, et ils se rangèrent en bataille près des portes de la ville, et les rois leurs alliés campèrent, chacun de son côté, dans la campagne.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
10 Joab reconnut qu'il aurait à livrer bataille devant son front et sur ses derrières; il rangea donc en face des Syriens les plus vaillants des jeunes fils d'Israël.
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
11 Et il confia à son frère Abessa le reste de l'armée, qui se déploya devant les fils d'Ammon.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
12 Et il dit à son frère: Si le Syrien l'emporte sur moi, tu viendras à mon aide, et si les fils d'Ammon te font plier, j'irai te secourir.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
13 Sois fort, agis en homme, pour l'amour de notre peuple et pour les villes de notre Dieu; que le Seigneur ensuite fasse à sa volonté.
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
14 Et Joab avec sa troupe tomba sur les Syriens; et ceux-ci s'enfuirent devant lui.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
15 Quand les fils d'Ammon virent que les Syriens fuyaient, ils s'enfuirent eux-mêmes devant Abessa; et ils s'enfermèrent dans leur ville, et Joab revint à Jérusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
16 Et le Syrien, voyant qu'Israël l'avait mis en fuite, envoya des messagers qui levèrent toute la Syrie des rives du Jourdain, et à sa tête Sophath (Sobac), général en chef de l'armée d'Adraazar.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
17 On en instruisit David; il réunit tout Israël, passa le Jourdain, les atteignit et les aborda de front; aussitôt la bataille s'engagea.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
18 Les Syriens s'enfuirent devant Israël; David leur tua sept mille hommes montés sur des chars, et quarante mille piétons; Sophath, le général en chef, périt.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
19 Et tous les serviteurs d'Adraazar, voyant qu'ils avaient échoué devant Israël, traitèrent avec David, et ils lui furent asservis. Quant au Syrien, il ne voulut plus secourir les fils d'Ammon.
Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< 1 Chroniques 19 >