< 2 Rois 18 >

1 En la troisième année du règne d'Osée, en Israël, Ezéchias, fils d'Achaz, devint roi de Juda.
Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
2 Il avait vingt-cinq ans quand il monta sur le trône, et il régna vingt- neuf ans à Jérusalem; sa mère se nommait Abu, fille de Zacharie.
Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
3 Et il fit ce qui est droit aux yeux du Seigneur, se conformant à tout ce qu'avait fait David, son aïeul.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
4 Ce fut lui qui détruisit les hauts lieux, qui abattit les colonnes, qui arracha les bois sacrés, et le serpent d'airain qu'avait fait Moïse; car, jusqu'à ces jours-là, les enfants d'Israël l'avaient encensé; Ezéchias lui donna le nom de Neesthan.
Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
5 En Dieu seul il mit son espérance, et après lui il n'y eut point en Juda de roi qui lui ressemblât, et il n'y en avait pas eu parmi ceux qui l'avaient précédé.
Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
6 Il s'attacha au Seigneur, et il ne cessa pas de le suivre; il observa tous les commandements qu'il avait donnés à Moïse.
Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
7 Et le Seigneur était avec lui, et il montra de la sagesse en toutes ses entreprises; il se révolta contre le roi des Assyriens, et il ne lui resta pas asservi.
Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
8 Ce fut lui qui frappa les Philistins jusqu'à Gaza et sa banlieue, depuis les tours des guetteurs jusqu'aux cités fortifiées.
Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
9 En la quatrième année du règne d'Ezéchias (la septième année du règne d'Osée, en Israël), Salmanasar, roi des Assyriens, ayant marché contre Samarie, l'assiégea.
Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
10 Et il la prit au bout de trois ans, en la huitième année du règne d'Ezéchias (la neuvième du règne d'Osée, celle où tomba Samarie).
Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
11 Puis, le roi des Assyriens transporta ses habitants en Haba et en Habor, sur le fleuve Gozan, et sur les montagnes des Mèdes;
Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
12 Parce que les Samaritains n'avaient point obéi à la voix du Seigneur, qu'ils avaient violé son alliance, qu'ils n'avaient ni écouté, ni pratiqué ce qu'il avait prescrit à son serviteur Moïse.
Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
13 En la quatorzième année du règne d'Ezéchias, Sennachérib, roi des Assyriens, vint assiéger les villes fortes de Juda, et il les prit.
Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
14 Alors, le roi Ezéchias envoya des messagers au roi des Assyriens à Lachis, disant: J'ai failli, éloigne-toi de moi; ce dont tu me chargeras, je le porterai. Et le roi des Assyriens chargea Ezéchias d'une taxe de trois cents talents d'argent et trois cents talents d'or.
Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
15 Et le roi de Juda donna tout l'argent qui se trouva dans le temple et dans les trésors de son palais.
Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
16 En ce temps-là, Ezéchias ôta l'or des portes du temple et les lames d'or dont il avait lui-même revêtu les colonnes, et il les donna au roi des Assyriens.
Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
17 Et le roi des Assyriens envoya de Lachis, au roi Ezéchias, Tharthan, Rhaphis et Rhabsacès, accompagnés d'une forte armée; ils arrivèrent devant Jérusalem, et s'arrêtèrent à l'aqueduc de la piscine supérieure qui est sur le chemin du Champ du Foulon.
Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
18 De là, ils appelèrent à grands cris Ezéchias; aussitôt Eliacim, fils d'Helcias, l'économe; Sobna le scribe, et Joas, fils de Saphat, l'archiviste, vinrent les trouver.
Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
19 Et Rhabsacès leur dit: Dites à Ezéchias: Voici ce que dit le grand roi, le roi des Assyriens: Quel est l'appui en qui tu t'es confié?
Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
20 Tu as dit (mais seulement des lèvres): Mon conseil, mon armée, inclinent pour la guerre; maintenant donc, en qui t'es-tu confié, pour te révolter contre nous?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
21 Voyons, n'as-tu point foi en ce roseau brisé qu'on appelle l'Égypte? Il entrera dans la main de quiconque s'appuiera sur lui, et il la percera. Voilà comment est le Pharaon d'Égypte pour tous ceux qui se fient en lui.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
22 Mais, tu m'as dit: Nous nous confions en Dieu le Seigneur. Or, ce Dieu n'est-il pas le même dont Ézéchias a détruit, sur les hauts lieux, les autels, quand il a donné cet ordre à Jérusalem et à Juda: Vous adorerez, devant cet autel seul, dans Jérusalem?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
23 Eh bien! combats aujourd'hui mon maître le roi des Assyriens, et je te donnerai deux mille chevaux, si tu peux te donner toi-même deux mille cavaliers.
“‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
24 Comment donc feras-tu reculer le moindre des chefs qui servent mon maître? Et tu mets ta confiance en l'Égypte, en ses chars, en ses chevaux!
Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
25 Est-ce que nous sommes venus détruire cette terre sans le Seigneur? Le Seigneur m'a dit: Marche sur cette terre, et détruis-la.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
26 Et Eliacim, fils d'Helcias, Sobna et Joas dirent à Rhabsacès: Parle syrien à tes serviteurs, car nous l'entendons; ne nous parle pas en langue judaïque. Pourquoi parles-tu pour être ouï du peuple qui est sur les remparts?
Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
27 Mais Rhabsacès répondit: Est-ce que mon maître m'a envoyé dire ces paroles à ton maître et à toi? Ne sont-elles pas pour les hommes qui se tiennent sur les remparts, et qui sont réduits comme vous à manger leurs excréments et à boire leur urine?
Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
28 Et Rbabsacès, se redressant, éleva la voix, et dit en langue judaïque: Écoutez les paroles du grand roi des Assyriens;
Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
29 Voici ce que dit le roi: Qu'Ezéchias ne vous excite point par ses discours, car il ne pourra vous arracher de mes mains.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
30 Qu'Ézéchias ne vous fasse point espérer au Seigneur, disant: Le Seigneur nous délivrera; il ne livrera point sa ville au roi des Assyriens.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
31 N'écoutez point Ezéchias; car voici ce que dit le roi des Assyriens: Cherchez auprès de moi votre bénédiction; venez à moi, et chacun boira le vin de sa vigne, chacun mangera les fruits de son figuier, chacun boira l'eau de sa citerne,
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
32 Jusqu'à ce que je revienne pour vous transporter en une terre comme la vôtre, en une terre de blé et de vignes, terre de pain et de vin, terre d'huile et de miel; et vous vivrez et vous ne mourrez point. N'écoutez point Ezéchias; car il vous trompe, quand il dit: Le Seigneur vous délivrera.
mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
33 Les dieux des nations qui tour à tour sont tombées dans les mains du roi, les ont-ils délivrées?
Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
34 Où est le dieu d'Emath et d'Arphad? Où est le dieu de Sepharvaïm, d'Ana et d'Abe? Ont-ils délivré Samarie de mes mains?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
35 Quel est donc celui des dieux, de toutes les nations, qui ait délivré sa terre de mes mains? Le Seigneur délivrera-t-il Jérusalem de mes mains?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
36 Et le peuple resta muet; personne ne répondit à ce discours; car le roi l'avait ainsi ordonné, disant: Ne lui répondez pas.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
37 Et l'économe Eliacim, fils d'Helcias, le scribe Sobna et l'archiviste Joas, fils de Saphat, rentrèrent auprès d'Ezéchias après avoir déchiré leurs vêtements; ils lui rapportèrent les paroles de Rhabsacès.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.

< 2 Rois 18 >