< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
Життя моє стало бридке́ для моєї душі... Нехай наріка́ння своє я на се́бе пущу́, нехай говорю́ я в гірко́ті своєї душі!
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
Скажу Богові я: Не осу́джуй мене́! Повідо́м же мене, чого став Ти зо мною на прю?
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
Чи це добре Тобі, що Ти гно́биш мене́, що пого́рджуєш тво́ривом рук Своїх, а раду безбожних осві́тлюєш?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
Хіба маєш Ти очі тілесні? Чи Ти бачиш так само, як бачить люди́на люди́ну?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Хіба Твої дні — як дні лю́дські, чи лі́та Твої — як дні мужа,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
що шукаєш провини моєї й виві́дуєш гріх мій,
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
хоч ві́даєш Ти, що я не беззако́нник, та нема, хто б мене врятува́в від Твоєї руки?
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Твої руки створили мене і вчинили мене́, потім Ти обернувся — і гу́биш мене.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Пам'ятай, що мов глину мене оброби́в Ти, — і в порох мене оберта́єш.
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Чи не ллєш мене, мов молоко, і не згусти́в Ти мене, мов на сир?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Ти шкірою й тілом мене зодяга́єш, і сплів Ти мене із костей та із жил.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Життя й милість пода́в Ти мені, а опіка Твоя стерегла мого духа.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
А оце заховав Ти у серці Своє́му, — я знаю, що є воно в Тебе:
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
якщо я грішу́, Ти мене стереже́ш, та з провини моєї мене не очи́щуєш.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
Якщо я провиню́ся, то горе мені! А якщо я невинний, не смію підня́ти свою голову, си́тий стидо́м та напо́єний горем своїм!
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
А коли піднесе́ться вона, то Ти ловиш мене, як той лев, і зно́ву предивно зо мною пово́дишся:
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
поно́влюєш свідків Своїх проти мене, помно́жуєш гнів Свій на мене, ві́йсько за ві́йськом на мене Ти шлеш.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
І на́що з утро́би Ти вивів мене? Я був би помер, — і жодні́сіньке око мене не побачило б,
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
як нібито не існував був би я, перейшов би з утроби до гро́бу.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Отож, дні мої нечисле́нні, — перестань же, й від мене вступи́сь, і нехай не турбу́юся я бодай тро́хи,
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
поки я не піду́ — й не верну́ся! — до кра́ю темно́ти та смертної тіні,
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
до те́много кра́ю, як мо́рок, до тьмя́ного краю, в якому поря́дків нема, і де світло, як те́мрява“.

< Yobu 10 >