< Nehemiya 13 >
1 Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
Того дня читане було з Мойсеєвої книги вголос наро́ду, і було зна́йдене написане в ній, що Аммоні́тянин та Моаві́тянин не вві́йде до Божої громади, і так бу́де аж навіки,
2 Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
бо вони не стріли були Ізраїлевих синів хлібом та водою, і найняли́ були на нього Валаама прокля́сти його, та Бог наш обернув те прокляття на благослове́ння.
3 Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
І сталося, як почули вони Зако́н, то відділили від Ізраїля все чуже.
4 Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
А перед тим священик Ел'яшів, призна́чений до комори дому нашого Бога, близьки́й Товійїн,
5 Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
то зробив йому велику комору, а туди давали колись жертву хлі́бну, ла́дан, і по́суд, і десятину збіжжя, молоде вино та оливу, призначені за́повіддю для Левитів, і співаків, і придве́рних, і священичі прине́сення.
6 Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
А за ввесь цей час не був я в Єрусалимі, бо в тридцять другому році Артаксе́ркса, царя вавилонського, я прийшов був до царя, та по певному ча́сі ви́просився я від царя.
7 ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
І прийшов я до Єрусалиму, і розглянувся в тому злі, що зробив Єл'яшів Товійї, ро́блячи йому комору на подві́р'ях Божого дому.
8 Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
І було мені дуже зле, й я всі домашні Товійїні речі повикида́в геть із комори.
9 Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
І я сказав, і очи́стили комори, а я вернув туди по́суд Божого дому, хлі́бну жертву та ла́дан.
10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
І дові́дався я, що левитські ча́стки не давалися, а вони повтікали кожен на поле своє, ті Левити та співаки́, що робили свою працю.
11 Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
І докоряв я заступникам та й сказав: „Чого опу́щений дім Божий?“І зібрав я їх, і поставив їх на їхніх місця́х.
12 Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
І вся Юдея прино́сила десятину збіжжя, і молодого вина, і оливи до скарбни́ць.
13 Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
І настанови́в я над скарбни́цями священика Шелемію й книжника Садока та Педаю з Левитів, а на їхню руку — Ханана, сина Заккура, сина Маттаніїного, бо вони були уважа́ні за вірних. І на них покладено — діли́ти частки для їхніх братів.
14 Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
Пам'ятай же мене, Боже, за це, і не зітри́ моїх добродійств, які я зробив у Божому домі та в сторо́жах!
15 Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
Тими днями бачив я в Юдеї таких, що топта́ли в суботу чави́ла, і носи́ли снопи́, і нав'ю́чували на ослів вино, виноград, і фіґі, і всілякий тяга́р, і ве́зли до Єрусалиму суботнього дня. І я при свідках остеріг їх того дня, коли вони продавали живність.
16 Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
А тиряни ме́шкали в ньому, і постача́ли рибу й усе на про́даж, і продавали в суботу Юдиним синам та в Єрусалимі.
17 Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
I докоряв я Юдиним шляхе́тним та й сказав їм: „Що́ це за річ, яку ви робите, і безчестите суботній день?
18 Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
Чи ж не так робили ваші батьки, а наш Бог спровадив усе це зло на нас та на це місто? А ви побі́льшуєте жар гніву на Ізраїля зневажа́нням суботи“.
19 Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
І бувало, як падала вечерова тінь на єрусалимські брами перед суботою, то я наказував, — і були зами́кувані брами. І звелів я, щоб не відчиняли їх, а тільки аж по суботі. А біля брам я поставив слуг своїх, — щоб тяга́р не входив суботнього дня!
20 Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
І ночували крамарі́ та продавці всього продажного раз і два поза Єрусалимом.
21 Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
І остеріг я їх при свідках та й сказав їм: „Чого ви ночуєте навпроти муру? Якщо ви повто́рите це, я простягну́ руку на вас!“Від того ча́су вони не прихо́дили в суботу.
22 Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
І сказав я Левитам, щоб вони очи́стилися й прихо́дили стерегти брами, щоб освятити суботній день. Також це запам'ятай мені, Боже мій, і змилуйся надо мною за великістю милости Твоєї!
23 Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
Тими днями бачив я також юдеїв, що брали собі за жіно́к ашдо́дянок, аммоні́тянок, моаві́тянок.
24 Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
А їхні сини говорили наполовину по-ашдо́дському, і не вміли говорити по-юдейському, а говорили мовою того чи того наро́ду.
25 Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
І докоряв я їм, і проклинав їх, і бив декого з них, і рвав їм волосся, і заприсягав їх Богом, ка́жучи: „Не давайте ваших дочо́к їхнім синам, і не беріть їхніх дочо́к для ваших синів та для вас.
26 Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
Чи ж не цим згрішив був Соломон, Ізраїлів цар, — а між багатьма́ наро́дами не було такого царя, як він, і був уподо́баний Богові своєму, і Бог настанови́в його царем над усім Ізраїлем, — і його ввели́ в гріх ті чужі жінки́?
27 Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
І тому́ чи ж чуте було́ таке, щоб чинити все це велике лихо на спроневі́рення проти нашого Бога, щоб брати чужих жіно́к?“
28 Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
А один із синів Йояди, сина Ел'яшіва, великого священика, був зятем хоронянина Санваллата, — і я вигнав його від себе!
29 Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
Запам'ята́й же їм, Боже мій, за спля́млення свяще́нства та заповіту свяще́ничого та леви́тського!
30 Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
І очистив я їх від усього чужого, і встановив че́рги для священиків та для Левитів, кожного в службі їх,
31 Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.
і для пожертви дров в озна́чених часа́х, і для первопло́дів. Запам'ятай же мене, Боже мій, на добро́!“