< Yobu 10 >

1 “Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
U A uluhua ko'u naau i kuu ola ana; E waiho iho au i kuu ulono ana ia'u iho; E olelo aku au maloko o ka ehaeha o kuu naau.
2 Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
E i aku au i ke Akua, Mai hoohewa mai oe ia'u; E hoike mai oe i ka mea au e hakaka mai nei me au.
3 Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
He mea maikai anei ia oe, e hookaumaha, A e hoowahawaha i ka hana a kou lima, A e hoomalamalama ae maluna o ka manao o ka poe hewa?
4 Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
O ko ke kino mau maka anei kou? Ua ike anei oe e like me ka ike ana a ke kanaka?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
Ua like anei kou mau la me na la o ke kanaka? Ua like anei kou mau makahiki me na la o ke kanaka,
6 kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
I ninau mai ai oe i kuu hala, A imi mai ai hoi i ko'u hewa?
7 ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
Ma kou ike aohe o'u hewa; Aohe mea nana e hoopakele mai kou lima aku.
8 “Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
Ua hana kou mau lima ia'u, A ua hoopaa mai oe ia'u a puni; Aka, ke luku mai nei oe ia'u.
9 Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
Ke noi aku nei au ia oe e hoomanao, Ua hana mai oe ia'u, e like me ka lepo; A e hoihoi anei oe ia'u i ka lepo?
10 Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
Aole anei oe i ninini iho ia'u me he waiu la, A i hoopaakiki mai hoi ia'u, me he waiupaa la?
11 Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
Ua uhi mai oe ia'u i ka ili a me ka io, A ua hoopaa mai oe ia'u i na iwi a me na olona.
12 Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
Ua hana mai oe iloko i ke ola a me ka pomaikai, A ua malama mai kou kiai ana i kuu uhane.
13 “Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
O keia mau mea kau i huna'i iloko o kou naau: Ua ike no wau, aia no me oe keia mea.
14 Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
Ina e hana hewa au, alaila hoomanao mai no oe ia'u, Aole oe e kela mai ia'u, mai ko'u hewa aku.
15 Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
Ina ua hewa au, auwe hoi wau; Ina ua pono au, aole wau e hookiekie i ko'u poo. Ua piha au i ka hilahila; A ua ike au i kuu poino;
16 Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
Ina e hookiekieia auanei ia, Ke hoohalua nei oe ia'u, me he liona la: A hoike hou mai oe ia oe iho he mana maluna o'u.
17 Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
Ke hoala hou nei oe i kou mau hoike ku e ia'u, A ke hoonui nei i kou inaina ia'u; A ke hoomahuahua mau nei na puali kaua ia'u.
18 “Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
No ke aha la hoi oe i lawe mai ai ia'u, mai ka opu mai: Ina ua make au ilaila, A ua ike ole ka maka ia'u!
19 Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
Ina ua like au me he mea ola ole la, Ina ua laweia'ku au mai ka opu aku, a ka luakupapau.
20 Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
Aole anei he uuku ko'u mau la? U'oki pela, a e waiho ia'u, i oluolu iki iho ai au,
21 ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
Mamua o kuu hele ana'ku i kahi aole au e hoi hou mai, I ka aina pouli, a me ka malu make;
22 ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”
He aina poeleele e like me ka pouli; He malu make, aohe mea i hooponoponoia, A o ka malamalama, ua like ia me ka pouli.

< Yobu 10 >