< Aefeso 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu. Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:
Paul, an Apostle of Jesus Christ through the will of God, to all the saints who are at Ephesus and to the faithful in Christ Jesus.
2 Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
Grace and peace to you from God the Father, and from the Lord Jesus Christ.
3 Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu.
Blessed be the God and Father of our Lord Jesus Christ, who has blessed us with every spiritual blessing in the heavens, in Christ,
4 Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,
just as he chose us in him before the foundation of the world, so that we would be holy and immaculate in his sight, in charity.
5 Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.
He has predestined us to adoption as sons, through Jesus Christ, in himself, according to the purpose of his will,
6 Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.
for the praise of the glory of his grace, with which he has gifted us in his beloved Son.
7 Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu
In him, we have redemption through his blood: the remission of sins in accord with the riches of his grace,
8 chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso,
which is superabundant in us, with all wisdom and prudence.
9 Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake.
So does he make known to us the mystery of his will, which he has set forth in Christ, in a manner well-pleasing to him,
10 Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
in the dispensation of the fullness of time, so as to renew in Christ everything that exists through him in heaven and on earth.
11 Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake,
In him, we too are called to our portion, having been predestined in accord with the plan of the One who accomplishes all things by the counsel of his will.
12 nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake.
So may we be, to the praise of his glory, we who have hoped beforehand in Christ.
13 Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza.
In him, you also, after you heard and believed the Word of truth, which is the Gospel of your salvation, were sealed with the Holy Spirit of the Promise.
14 Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
He is the pledge of our inheritance, unto the acquisition of redemption, to the praise of his glory.
15 Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse,
Because of this, and hearing of your faith that is in the Lord Jesus, and of your love toward all the saints,
16 ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.
I have not ceased giving thanks for you, calling you to mind in my prayers,
17 Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
so that the God of our Lord Jesus Christ, the Father of glory, may give a spirit of wisdom and of revelation to you, in knowledge of him.
18 Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
May the eyes of your heart be illuminated, so that you may know what is the hope of his calling, and the wealth of the glory of his inheritance with the saints,
19 Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
and the preeminent magnitude of his virtue toward us, toward we who believe in accord with the work of his powerful virtue,
20 imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba.
which he wrought in Christ, raising him from the dead and establishing him at his right hand in the heavens,
21 Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn g165)
above every principality and power and virtue and dominion, and above every name that is given, not only in this age, but even in the future age. (aiōn g165)
22 Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo,
And he has subjected all things under his feet, and he has made him the head over the entire Church,
23 umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.
which is his body and which is the fullness of him who accomplishes everything in everyone.

< Aefeso 1 >