< Agalatiya 6 >

1 Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe.
And, brothers, if a man has been overtaken by any offense, you who are spiritual should instruct someone like this with a spirit of leniency, considering that you yourselves might also be tempted.
2 Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu.
Carry one another’s burdens, and so shall you fulfill the law of Christ.
3 Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha.
For if anyone considers himself to be something, though he may be nothing, he deceives himself.
4 Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake,
So let each one prove his own work. And in this way, he shall have glory in himself only, and not in another.
5 pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.
For each one shall carry his own burden.
6 Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.
And let him who is being taught the Word discuss it with him who is teaching it to him, in every good way.
7 Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa.
Do not choose to wander astray. God is not to be ridiculed. For whatever a man will have sown, that also shall he reap.
8 Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. (aiōnios g166)
For whoever sows in his flesh, from the flesh he shall also reap corruption. But whoever sows in the Spirit, from the Spirit he shall reap eternal life. (aiōnios g166)
9 Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa.
And so, let us not be deficient in doing good. For in due time, we shall reap without fail.
10 Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.
Therefore, while we have time, we should do good works toward everyone, and most of all toward those who are of the household of the faith.
11 Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.
Consider what kind of letters I have written to you with my own hand.
12 Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu.
For as many of you as they desire to please in the flesh, they compel to be circumcised, but only so that they might not suffer the persecution of the cross of Christ.
13 Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo.
And yet, neither do they themselves, who are circumcised, keep the law. Instead, they want you to be circumcised, so that they may glory in your flesh.
14 Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi.
But far be it from me to glory, except in the cross of our Lord Jesus Christ, through whom the world is crucified to me, and I to the world.
15 Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano.
For in Christ Jesus, neither circumcision nor uncircumcision prevails in any way, but instead there is a new creature.
16 Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.
And whoever follows this rule: may peace and mercy be upon them, and upon the Israel of God.
17 Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
Concerning other matters, let no one trouble me. For I carry the stigmata of the Lord Jesus in my body.
18 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.
May the grace of our Lord Jesus Christ be with your spirit, brothers. Amen.

< Agalatiya 6 >