< Aefeso 2 >
1 Kunena za inu, kale munali akufa chifukwa cha zolakwa zanu ndi machimo anu,
And you were once dead in your sins and offenses,
2 mmene inu munkakhalamo pamene munkatsatira njira za dziko lapansi ndi za ulamuliro waufumu wa mlengalenga, mzimu umene ukugwira ntchito tsopano mwa amene samvera. (aiōn )
in which you walked in times past, according to the age of this world, according to the prince of the power of this sky, the spirit who now works in the sons of distrust. (aiōn )
3 Nthawi ina tonsefe tinalinso ndi moyo wonga wawo, tinkachitanso zilizonse zimene matupi ndi maganizo athu ankafuna. Mwachibadwa chathu, tinali oyenera chilango monga anthu ena onse.
And we too were all conversant in these things, in times past, by the desires of our flesh, acting according to the will of the flesh and according to our own thoughts. And so we were, by nature, sons of wrath, even like the others.
4 Koma chifukwa cha chikondi chake chachikulu pa ife, Mulungu amene ndi olemera mʼchifundo,
Yet still, God, who is rich in mercy, for the sake of his exceedingly great charity with which he loved us,
5 anatipanga kukhala amoyo ndi Khristu ngakhale pamene ife tinali akufa mu zolakwa zathu. Koma tinapulumutsidwa mwachisomo.
even when we were dead in our sins, has enlivened us together in Christ, by whose grace you have been saved.
6 Ndipo Mulungu anatiukitsa pamodzi ndi Khristu ndi kutikhazika pamodzi ndi Iye mmwamba mwa Khristu Yesu,
And he has raised us up together, and he has caused us to sit down together in the heavens, in Christ Jesus,
7 ndi cholinga chakuti mʼnthawi imene ikubwera, Iyeyo adzaonetse chuma choposa cha chisomo chake, choonetsedwa mwa kukoma mtima kwake kwa ife mwa Khristu Yesu. (aiōn )
so that he may display, in the ages soon to arrive, the abundant wealth of his grace, by his goodness toward us in Christ Jesus. (aiōn )
8 Pakuti mwapulumutsidwa mwachisomo, kudzera mʼchikhulupiriro ndipo izi sizochokera mwa inu eni, koma ndi mphatso ya Mulungu,
For by grace, you have been saved through faith. And this is not of yourselves, for it is a gift of God.
9 osati ndi ntchito, kuti wina aliyense asadzitamandire.
And this is not of works, so that no one may glory.
10 Pakuti ndife ntchito ya Mulungu, olengedwa mwa Khristu Yesu kuti tichite ntchito zabwino, zimene Mulungu anazikonzeratu kale kuti tizichite.
For we are his handiwork, created in Christ Jesus for the good works which God has prepared and in which we should walk.
11 Chifukwa chake kumbukirani kuti poyamba inu amene munali anthu a mitundu ina mwachibadwa ndipo munkatchedwa “osachita mdulidwe” ndi amene amadzitcha okha “a mdulidwe” (zimene zinachitika mʼthupi ndi manja a anthu).
Because of this, be mindful that, in times past, you were Gentiles in the flesh, and that you were called uncircumcised by those who are called circumcised in the flesh, something done by man,
12 Kumbukirani kuti nthawi imene inu munali wopanda Khristu, simunkawerengedwa ngati nzika za Israeli ndipo munali alendo pa pangano la lonjezo, wopanda chiyembekezo ndi opanda Mulungu mʼdziko lapansi.
and that you were, in that time, without Christ, being foreign to the way of life of Israel, being visitors to the testament, having no hope of the promise, and being without God in this world.
13 Koma tsopano mwa Khristu Yesu, inu amene nthawi ina munali kutali, mwabweretsedwa pafupi kudzera mʼmagazi a Khristu.
But now, in Christ Jesus, you, who were in times past far away, have been brought near by the blood of Christ.
14 Pakuti Iye mwini ndiye mtendere wathu, amene anachita kuti awiri akhale mmodzi ndipo anagumula chotchinga, khoma la udani lotilekanitsa,
For he is our peace. He made the two into one, by dissolving the intermediate wall of separation, of opposition, by his flesh,
15 pothetsa mʼthupi lake lamulo pamodzi ndi zolamulira zake ndi malangizo. Cholinga chake chinali chakuti alenge mwa Iye mwini, munthu mmodzi watsopano kuchokera kwa abwino, motero nʼkupanga mtendere,
emptying the law of commandments by decree, so that he might join these two, in himself, into one new man, making peace
16 ndi kuyanjanitsa onse awiriwa mʼthupi lake kwa Mulungu, kudzera pa mtanda, umene Iye anaphapo udani wawo.
and reconciling both to God, in one body, through the cross, destroying this opposition in himself.
17 Iye anabwera ndipo analalikira mtendere kwa inu amene munali kutali ndi mtendere ndiponso kwa iwonso amene anali pafupi.
And upon arriving, he evangelized peace to you who were far away, and peace to those who were near.
18 Pakuti mwa Iye, ife tonse titha kufika kwa Atate mwa Mzimu mmodzi.
For by him, we both have access, in the one Spirit, to the Father.
19 Kotero kuti, inu sindinunso alendo ndi adani, koma nzika pamodzi ndi anthu a Mulungu ndiponso a mʼbanja la Mulungu.
Now, therefore, you are no longer visitors and new arrivals. Instead, you are citizens among the saints in the household of God,
20 Ndinu okhazikika pa maziko a atumwi ndi a aneneri, pamodzi ndi Khristu Yesu mwini ngati mwala wa pa ngodya.
having been built upon the foundation of the Apostles and of the Prophets, with Jesus Christ himself as the preeminent cornerstone.
21 Mwa Iyeyo, nyumba yonse yalumikizidwa pamodzi ndipo yakwezedwa kukhala Nyumba yoyera mwa Ambuye.
In him, all that has been built is framed together, rising up into a holy temple in the Lord.
22 Ndipo mwa Iye, inunso mukamangidwa pamodzi ndi ena onse kukhala nyumba yokhalamo imene Mulungu amakhala mwa Mzimu wake.
In him, you also have been built together into a habitation of God in the Spirit.