< 2 Akorinto 1 >

1 Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, pamodzi ndi mʼbale wathu Timoteyo, Kulembera mpingo wa Mulungu mu Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse mu Akaya monse.
Paul, apôtre de Jésus-Christ, selon la volonté de Dieu, et Timothée, notre frère, à l'assemblée de Dieu qui est à Corinthe, avec tous les saints qui sont dans toute l'Achaïe.
2 Mukhale ndi chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
Grâce et paix à vous, de la part de Dieu notre Père et du Seigneur Jésus-Christ.
3 Alemekezeke Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, Atate achifundo chonse, Mulungu wachitonthozo chonse.
Béni soit le Dieu et Père de notre Seigneur Jésus-Christ, le Père des miséricordes et Dieu de toute consolation,
4 Iye amatitonthoza ife mʼmavuto athu onse, kuti ifenso tithe kutonthoza amene ali pavuto lililonse ndi chitonthozo chimene ife tilandira kwa Mulungu.
qui nous console dans toute notre affliction, afin que nous puissions consoler ceux qui sont dans quelque affliction, par la consolation dont nous sommes nous-mêmes consolés par Dieu.
5 Pakuti monga momwe tili mʼmasautso pamodzi ndi Khristu, momwemonso Khristu amatitonthoza kwambiri.
En effet, comme les souffrances de Christ nous abondent, de même notre consolation abonde aussi par Christ.
6 Ngati ife tikusautsidwa, nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe ndi kupulumutsidwa. Ngati ife tikutonthozedwa nʼchifukwa choti inu mutonthozedwe, ndi chitonthozo chimene chimabweretsa mwa inu kupirira kosawiringula pa zosautsa zomwe timasauka nazo ife.
Mais si nous sommes affligés, c'est pour votre consolation et votre salut. Si nous sommes consolés, c'est pour votre consolation, qui produit en vous la patience dans les mêmes souffrances que nous.
7 Ndipo chiyembekezo chathu pa inu nʼcholimba chifukwa tikudziwa kuti monga momwe mumamva zowawa pamodzi nafe, momwemonso mumatonthozedwa nafe pamodzi.
Notre espérance pour vous est inébranlable, sachant que, puisque vous avez part aux souffrances, vous avez aussi part à la consolation.
8 Abale, sitikufuna kuti mukhale osadziwa za masautso amene tinakumana nawo mʼchigawo cha Asiya. Tinapanikizidwa koopsa kuposa muyeso woti nʼkutha kupirira, mwakuti sitinkadziwa kuti nʼkukhalabe ndi moyo.
Nous ne voulons pas, en effet, vous laisser dans l'ignorance, frères, de l'épreuve qui nous est arrivée en Asie: nous avons été accablés au-delà de nos forces, au point de désespérer même de la vie.
9 Zoonadi, tinamva mʼmitima mwathu chilango cha imfa. Koma izi zimachitika kuti tisangodzidalira mwa ife tokha koma Mulungu yemwe amaukitsa akufa.
Oui, nous avons eu nous-mêmes la sentence de mort au-dedans de nous-mêmes, afin que nous ne nous confiions pas en nous-mêmes, mais en Dieu qui ressuscite les morts,
10 Mulungu watilanditsa ku zoopsa zotere za imfa, ndipo adzatilanditsanso. Ife tayika chiyembekezo chathu pa Iyeyo kuti adzapitiriza kutilanditsabe.
qui nous a délivrés d'une si grande mort, et qui délivre, lui en qui nous avons mis notre espérance qu'il nous délivrera encore,
11 Mutithandize potipempherera. Pamenepo ambiri adzathokoza mʼmalo mwathu, chifukwa cha chisomo chake poyankha mapemphero a anthu ambiri.
vous aussi, vous vous associez en notre faveur par vos supplications, afin que, pour le don qui nous a été fait par l'intermédiaire de plusieurs, des remerciements soient rendus par plusieurs personnes en votre faveur.
12 Tsono chonyadira chathu nʼchakuti, chikumbumtima chathu chimatitsimikizira kuti timakhala bwino mʼdziko lapansi, makamaka pa ubale wathu ndi inu. Takhala moona mtima ndi oyera mtima. Sitinachite chomwechi mwa nzeru ya dziko lapansi koma monga mwa chisomo cha Mulungu.
Car notre vantardise, c'est ceci: le témoignage de notre conscience que, dans la sainteté et la sincérité de Dieu, non dans la sagesse charnelle, mais dans la grâce de Dieu, nous nous sommes conduits dans le monde, et plus abondamment envers vous.
13 Pakuti sitikukulemberani zoti simungawerenge kapena kumvetsetsa.
Car nous ne vous écrivons rien d'autre que ce que vous lisez ou même reconnaissez, et j'espère que vous reconnaîtrez jusqu'au bout -
14 Monga mwamva pangʼono chabe, ndikuyembekeza kuti mudzamvetsa kwenikweni, kuti mutha kutinyadira monga ife tidzakunyadirani, pa tsiku la Ambuye Yesu.
comme vous nous avez aussi reconnus en partie - que nous sommes votre vantardise, comme vous êtes aussi la nôtre, au jour de notre Seigneur Jésus.
15 Popeza ndinatsimikiza mtima za ichi, nʼchifukwa chake ndinafuna kuti poyamba, ndidzakuchezereni kuti mupindule pawiri.
Dans cette confiance, j'étais résolu à venir d'abord chez toi, afin que tu en retires un second avantage,
16 Ndinafuna kuti ndidzakuchezereni pa ulendo wanga wopita ku Makedoniya ndi kudzakuonaninso pochokera ku Makedoniyako kuti inu mudzandithandize pa ulendo wanga wopita ku Yudeya.
à passer par toi en Macédoine, et de nouveau de Macédoine à venir chez toi, et à être envoyé par toi en voyage en Judée.
17 Kodi pamene ndinkakonzekera zimenezi, mukuganiza kuti ndinkachita mwachibwana? Kapena kuti ndinkaganiza ngati mwa dziko lapansi; kuti ndikhoza kumanena kuti, “Inde, Inde,” nthawi yomweyo nʼkumatinso “Ayi, Ayi?”
Quand j'ai conçu ces projets, ai-je fait preuve d'inconstance? Ou bien les choses que je projette, les projette-je selon la chair, pour qu'il y ait chez moi des « oui, oui » et des « non, non »?
18 Koma zoona monga Mulungu ali wokhulupirika, uthenga wathu kwa inu siwakuti, “Inde” nʼkutinso “Ayi.”
Mais comme Dieu est fidèle, notre parole à votre égard n'a pas été « Oui et non ».
19 Pakuti Yesu Khristu mwana wa Mulungu amene ine, Silivano ndi Timoteyo tinamulalikira pakati panu sali “Inde” yemweyonso “Ayi.” Koma nthawi zonse mwa Iye muli “Inde.”
Car le Fils de Dieu, Jésus-Christ, que nous avons prêché parmi vous, moi, Silvain et Timothée, n'était pas « oui et non », mais en lui c'est « oui ».
20 Pakuti ngakhale malonjezo a Mulungu atachuluka chotani, onsewo ndi “Inde” mwa Khristu. Kotero kuti mwa Iye, ife timati “Ameni” kuchitira Mulungu ulemu.
En effet, quel que soit le nombre des promesses de Dieu, le « oui » est en lui. C'est pourquoi aussi par lui est l' « Amen », à la gloire de Dieu par nous.
21 Tsono ndi Mulungu amene anachititsa kuti inu ndi ife tiyime molimba mwa Khristu. Anatidzoza ife,
Or, celui qui nous a établis avec vous en Christ et nous a oints, c'est Dieu,
22 nayikanso Mzimu wake mʼmitima mwathu kutitsimikizira za mʼtsogolo.
qui nous a aussi scellés et nous a donné l'acompte de l'Esprit dans nos cœurs.
23 Mulungu ndi mboni yanga kuti sindinabwererenso ku Korinto kuno kuti ndisakumvetseni chisoni.
Mais j'appelle Dieu en témoignage de mon âme, que, pour vous épargner, je ne suis pas venu à Corinthe.
24 Sikuti ife tikufuna kukhala olamulira chikhulupiriro chanu, koma timagwira nanu ntchito pamodzi kuti mukhale achimwemwe, chifukwa ndinu okhazikika kwambiri mʼchikhulupiriro.
Nous ne contrôlons pas votre foi, mais nous sommes compagnons de travail avec vous pour votre joie. Car vous tenez ferme dans la foi.

< 2 Akorinto 1 >