< Agalatiya 1 >

1 Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
Paul, apôtre, non de la part des hommes et par les hommes, mais par Jésus-Christ et Dieu le Père, qui l'a ressuscité des morts,
2 pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
et tous les frères qui sont avec moi, aux assemblées de la Galatie.
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
Que la grâce et la paix vous soient données par Dieu le Père et par notre Seigneur Jésus-Christ,
4 Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn g165)
qui s'est livré lui-même pour nos péchés, afin de nous délivrer du présent siècle mauvais, selon la volonté de notre Dieu et Père, (aiōn g165)
5 Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
à qui soit la gloire aux siècles des siècles. Amen. (aiōn g165)
6 Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
Je m'étonne que vous abandonniez si vite celui qui vous a appelés dans la grâce de Christ pour une autre « bonne nouvelle »,
7 umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
mais il n'y a pas d'autre « bonne nouvelle ». Seulement, il y a des gens qui vous troublent et qui veulent pervertir la Bonne Nouvelle du Christ.
8 Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
Mais si nous-mêmes, ou un ange du ciel, vous annonçons une autre « bonne nouvelle » que celle que nous vous avons annoncée, qu'il soit maudit.
9 Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
Ce que nous avons déjà dit, je le répète maintenant: si quelqu'un vous annonce une autre « bonne nouvelle » que celle que vous avez reçue, qu'il soit maudit.
10 Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
Car est-ce que je cherche maintenant la faveur des hommes, ou celle de Dieu? Ou bien est-ce que je cherche à plaire aux hommes? Car si je cherchais encore à plaire aux hommes, je ne serais pas un serviteur du Christ.
11 Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
Mais je vous fais savoir, frères, au sujet de la Bonne Nouvelle qui a été prêchée par moi, qu'elle n'est pas selon l'homme.
12 Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
Car je ne l'ai pas reçue d'un homme, et on ne me l'a pas enseignée, mais elle m'est venue par révélation de Jésus-Christ.
13 Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
Car vous avez appris comment j'ai vécu autrefois dans la religion des Juifs, et comment j'ai persécuté l'assemblée de Dieu et l'ai ravagée.
14 Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
J'étais plus avancé dans la religion juive que beaucoup de mes compatriotes de mon âge, étant plus zélé pour les traditions de mes pères.
15 Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
Mais lorsque Dieu, qui m'a séparé du sein de ma mère et m'a appelé par sa grâce, eut le bon plaisir
16 kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
de révéler son Fils en moi, afin que je l'annonce parmi les païens, je ne me suis pas immédiatement entretenu avec la chair et le sang,
17 Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
et je ne suis pas monté à Jérusalem auprès de ceux qui ont été apôtres avant moi, mais je suis parti en Arabie. Puis je suis retourné à Damas.
18 Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
Puis, au bout de trois ans, je montai à Jérusalem pour visiter Pierre, et je restai avec lui quinze jours.
19 Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
Mais des autres apôtres, je n'ai vu que Jacques, le frère du Seigneur.
20 Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
Or, pour ce qui est des choses que je vous écris, voici que, devant Dieu, je ne mens pas.
21 Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
Puis je suis arrivé dans les régions de Syrie et de Cilicie.
22 Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
J'étais encore inconnu de visage aux assemblées de Judée qui étaient en Christ,
23 Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
mais elles entendaient seulement dire: « Celui qui nous persécutait autrefois prêche maintenant la foi qu'il s'efforçait autrefois de détruire. »
24 Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.
Ils ont donc glorifié Dieu en moi.

< Agalatiya 1 >