< 1 Akorinto 1 >

1 Paulo, woyitanidwa mwachifuniro cha Mulungu kuti akhale mtumwi wa Khristu Yesu ndi mʼbale wathu Sositene.
Paul, appelé à être apôtre de Jésus-Christ par la volonté de Dieu, et notre frère Sosthène,
2 Kupita ku mpingo wa Mulungu ku Korinto, kwa oyeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi oyitanidwa kukhala opatulika ndiponso kwa onse amene amapemphera mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu mʼdziko lonse lapansi, amene ndi Ambuye wawo ndi wathunso.
à l'assemblée de Dieu qui est à Corinthe, à ceux qui sont sanctifiés en Jésus-Christ, appelés saints, avec tous ceux qui invoquent le nom de notre Seigneur Jésus-Christ, en tout lieu, chez eux et chez nous:
3 Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
Grâce et paix à vous, de la part de Dieu notre Père et du Seigneur Jésus-Christ.
4 Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu.
Je rends toujours grâces à mon Dieu à votre sujet, pour la grâce de Dieu qui vous a été donnée en Jésus-Christ,
5 Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse,
afin que vous soyez enrichis en tout par lui, en toute parole et en toute connaissance,
6 chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu.
comme le témoignage de Christ a été confirmé en vous,
7 Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe.
afin que vous ne soyez en retard d'aucun don, dans l'attente de la révélation de notre Seigneur Jésus-Christ,
8 Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu.
qui vous confirmera aussi jusqu'à la fin, irréprochables au jour de notre Seigneur Jésus-Christ.
9 Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.
Dieu est fidèle, celui par qui vous avez été appelés à la communion de son Fils, Jésus-Christ notre Seigneur.
10 Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo.
Or, je vous prie, frères, par le nom de notre Seigneur Jésus-Christ, de parler tous de la même chose, et qu'il n'y ait pas de divisions parmi vous, mais que vous soyez perfectionnés ensemble dans le même esprit et dans le même jugement.
11 Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu.
Car il m'a été rapporté à votre sujet, mes frères, par ceux de la maison de Chloé, qu'il y a des disputes parmi vous.
12 Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”
Or, je veux dire que chacun de vous dit: « Je suis Paul », « Je suis Apollos », « Je suis Céphas », et « Je suis le Christ ».
13 Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo?
Le Christ est-il divisé? Paul a-t-il été crucifié pour vous? Ou bien avez-vous été baptisé au nom de Paul?
14 Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo,
Je rends grâces à Dieu de ce que je n'ai baptisé aucun de vous, excepté Crispus et Gaïus,
15 mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa.
afin que personne ne puisse dire que je vous ai baptisés en mon propre nom.
16 (Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense).
(J'ai aussi baptisé la maison de Stéphanas; en dehors d'eux, je ne sais pas si j'en ai baptisé d'autres).
17 Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.
Car ce n'est pas pour baptiser que Christ m'a envoyé, mais pour annoncer la Bonne Nouvelle, sans sagesse de mots, afin que la croix de Christ ne soit pas annulée.
18 Pakuti uthenga wa mtanda ndi chopusa kwa iwo amene akuwonongeka, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa uthengawu ndi mphamvu ya Mulungu.
Car la parole de la croix est une folie pour ceux qui meurent, mais pour nous qui sommes sauvés, elle est une puissance de Dieu.
19 Pakuti kwalembedwa kuti, “Ine ndidzawononga nzeru za anthu anzeru; luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
Car il est écrit, « Je détruirai la sagesse des sages. Je réduirai à néant le discernement de ceux qui savent discerner. »
20 Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? (aiōn g165)
Où est le sage? Où est le scribe? Où est le discoureur de ce siècle? Dieu n'a-t-il pas rendu insensée la sagesse de ce monde? (aiōn g165)
21 Tsono poti mwa nzeru za Mulungu dziko lapansi mu nzeru zake silinamudziwe Iye, Mulungu amakondweretsedwa kuti kudzera mu chopusa cha zomwe zinalalikidwa apulumutse iwo amene akhulupirira.
En effet, puisque, dans la sagesse de Dieu, le monde n'a pas connu Dieu, Dieu a voulu, par la folie de la prédication, sauver ceux qui croient.
22 Ayuda amafuna zizindikiro zodabwitsa ndipo Agriki amafunafuna nzeru,
Car les Juifs demandent des signes, les Grecs cherchent la sagesse,
23 koma ife timalalikira Khristu wopachikidwa. Chitsa chokhumudwitsa kwa Ayuda ndi chopusa kwa a mitundu ina.
mais nous, nous prêchons Christ crucifié, pierre d'achoppement pour les Juifs et folie pour les Grecs,
24 Koma kwa iwo amene Mulungu anawayitana, Ayuda ndi Agriki omwe, Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndi nzeru za Mulungu.
mais pour ceux qui sont appelés, Juifs et Grecs, Christ est la puissance de Dieu et la sagesse de Dieu,
25 Pakuti za Mulungu zooneka ngati zopusa, ndi za nzeru kuposa nzeru za munthu, ndipo za Mulungu zooneka ngati zofowoka, zili ndi mphamvu kuposa mphamvu za munthu.
car la folie de Dieu est plus sage que les hommes, et la faiblesse de Dieu est plus forte que les hommes.
26 Abale taganizirani mmene munalili musanayitanidwe. Si ambiri a inu munali a nzeru, si ambiri a inu munali a mphamvu zamakopedwe. Si ambiri a inu munali obadwa pa ulemerero.
Car vous voyez votre vocation, frères, qu'il n'y a pas beaucoup de sages selon la chair, ni beaucoup de puissants, ni beaucoup de nobles;
27 Koma Mulungu anasankha zinthu zopusa za dziko lapansi kuti achititse manyazi anzeru. Mulungu anasankha zinthu zofowoka za dziko lapansi kuti achititse manyazi amphamvu.
mais Dieu a choisi les choses insensées du monde pour confondre les sages. Dieu a choisi les choses faibles du monde, pour couvrir de honte les choses fortes.
28 Anasankha zinthu zapansipansi ndi zopeputsidwa za dziko la pansi lino, zinthu zimene kulibe, kuti asukulutse zimene zilipo,
Dieu a choisi les choses humbles du monde, les choses méprisées, les choses qui n'existent pas, afin de réduire à néant les choses qui existent,
29 kuti munthu asanyade pamaso pa Mulungu.
pour que nulle chair ne se glorifie devant Dieu.
30 Nʼchifukwa cha Iye kuti inu muli mwa Khristu Yesu, amene wakhala nzeru ya kwa Mulungu, kwa ife, kunena kuti kulungama kwathu, chiyero ndi chipulumutso.
C'est à cause de lui que vous êtes en Jésus-Christ, qui a été fait pour nous sagesse de Dieu, justice, sanctification et rédemption,
31 Choncho poti zinalembedwa kuti, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
afin que, selon qu'il est écrit: « Que celui qui se glorifie se glorifie dans le Seigneur. »

< 1 Akorinto 1 >