< Aroma 1 >

1 Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
Paul, serviteur de Jésus-Christ, appelé à être apôtre, mis à part pour la Bonne Nouvelle de Dieu,
2 umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
qu'il a promise auparavant par ses prophètes dans les saintes Écritures,
3 Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
concernant son Fils, né de la postérité de David selon la chair,
4 Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
déclaré Fils de Dieu avec puissance selon l'Esprit de sainteté, par la résurrection des morts, Jésus-Christ notre Seigneur,
5 ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
par lequel nous avons reçu la grâce et l'apostolat pour l'obéissance de la foi parmi toutes les nations, à cause de son nom;
6 Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
parmi lesquels vous êtes aussi appelés à appartenir à Jésus-Christ;
7 Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
à tous ceux qui sont à Rome, bien-aimés de Dieu, appelés à être saints: Grâce et paix à vous, de la part de Dieu notre Père et du Seigneur Jésus-Christ.
8 Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
D'abord, je rends grâce à mon Dieu par Jésus-Christ pour vous tous, de ce que votre foi est proclamée dans le monde entier.
9 Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
Car Dieu m'est témoin, lui que je sers en esprit dans la Bonne Nouvelle de son Fils, combien sans cesse je fais mention de vous dans mes prières,
10 Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
en demandant si, d'une manière ou d'une autre, la volonté de Dieu me permet enfin d'aller vers vous.
11 Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
Car je désire ardemment vous voir, afin de vous communiquer quelque don spirituel, pour que vous soyez affermis;
12 ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
c'est-à-dire que je sois encouragé en vous, chacun de nous par la foi de l'autre, la vôtre et la mienne.
13 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
Or, je ne veux pas que vous ignoriez, frères, que j'ai souvent projeté de venir chez vous (et que j'en ai été empêché jusqu'ici), afin de porter du fruit parmi vous aussi, comme parmi le reste des païens.
14 Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
J'ai une dette envers les Grecs et les étrangers, envers les sages et les insensés.
15 Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
Ainsi, autant qu'il est en moi, je suis impatient d'annoncer la Bonne Nouvelle à vous aussi qui êtes à Rome.
16 Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
En effet, je n'ai pas honte de la Bonne Nouvelle du Christ, car elle est la puissance de Dieu pour le salut de quiconque croit, du Juif d'abord, et aussi du Grec.
17 Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
Car en elle est révélée la justice de Dieu, de foi à foi. Comme il est écrit: « Le juste vivra par la foi. »
18 Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
Car la colère de Dieu se révèle du ciel contre toute impiété et toute injustice des hommes qui suppriment la vérité dans l'injustice,
19 Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
parce que ce qui est connu de Dieu est révélé en eux, car Dieu le leur a révélé.
20 Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios g126)
Car les choses invisibles de Dieu, depuis la création du monde, se voient clairement, étant perçues par les choses faites, même sa puissance éternelle et sa divinité, afin qu'ils soient sans excuse. (aïdios g126)
21 Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
Parce que, connaissant Dieu, ils ne l'ont pas glorifié comme Dieu, et n'ont pas rendu grâces, mais ils sont devenus vains dans leurs raisonnements, et leur cœur insensé s'est obscurci.
22 Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
Se prétendant sages, ils sont devenus fous,
23 Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
et ils ont échangé la gloire du Dieu incorruptible contre l'image de l'homme corruptible, des oiseaux, des quadrupèdes et des reptiles.
24 Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
C'est pourquoi Dieu les a livrés à l'impureté dans les convoitises de leur cœur, afin que leur corps soit déshonoré au milieu d'eux.
25 Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
Ils ont changé la vérité de Dieu en mensonge, et ils ont adoré et servi la créature plutôt que le Créateur, qui est béni éternellement. Amen. (aiōn g165)
26 Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
C'est pourquoi Dieu les a livrés à des passions infâmes. Car leurs femmes ont changé la fonction naturelle en ce qui est contre nature.
27 Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
De même, les hommes, abandonnant la fonction naturelle de la femme, se sont enflammés dans leur convoitise les uns envers les autres, les hommes faisant ce qui est inconvenant avec les hommes, et recevant en eux-mêmes la peine due à leur erreur.
28 Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
De même qu'ils ont refusé d'avoir Dieu dans leur connaissance, Dieu les a livrés à un esprit réprouvé, pour qu'ils fassent ce qui ne convient pas;
29 Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
étant remplis de toute iniquité, d'immoralité sexuelle, de méchanceté, de cupidité, de malice; pleins d'envie, de meurtres, de querelles, de tromperies, de mauvaises habitudes, calomniateurs en secret,
30 osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
médisants, odieux à Dieu, insolents, arrogants, fanfarons, inventeurs de malheurs, désobéissants à leurs parents,
31 alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
sans intelligence, violateurs d'alliance, sans affection naturelle, impitoyables, sans miséricorde,
32 Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.
qui, connaissant le décret de Dieu, selon lequel ceux qui pratiquent de telles choses méritent la mort, non seulement agissent de même, mais encore approuvent ceux qui les pratiquent.

< Aroma 1 >