< 1 Akorinto 5 >

1 Mbiri yamveka kuti pakati panu pakuchitika chigololo. Ndipo chigololo cha mtunduwu ngakhale pakati pa akunja sichingapezeke; munthu akumagonana ndi mkazi wa abambo ake.
On rapporte en effet qu'il y a parmi vous une immoralité sexuelle, et une immoralité sexuelle telle qu'on ne la nomme même pas chez les païens, que l'on a la femme de son père.
2 Ndipo inu mukudzitukumulabe. Kodi simukanayenera kudzazidwa ndi chisoni ndipo mukanamuchotsa pa chiyanjano chanu munthu wochita zimenezi?
Vous êtes arrogants, et vous n'avez pas plutôt porté le deuil, afin que celui qui a commis cette action soit retiré du milieu de vous.
3 Ngakhale sindili nanu mʼthupi, ndili nanu mu mzimu. Ndipo ineyo ndapereka kale chiweruzo pa munthu amene amachita zotere, ngati kuti ndili komweko.
En effet, moi, absent de corps mais présent d'esprit, j'ai déjà jugé, comme si j'étais présent, celui qui a commis cette action.
4 Mukasonkhana mu dzina la Ambuye athu Yesu, ine ndili nanu mu mzimu, ndipo mphamvu ya Ambuye athu Yesu ili pomwepo,
Au nom de notre Seigneur Jésus-Christ, lorsque vous serez réunis avec mon esprit par la puissance de notre Seigneur Jésus-Christ,
5 mumupereke munthuyu kwa Satana, kuti chikhalidwe chake cha uchimo chiwonongedwe ndikuti mzimu wake udzapulumuke pa tsiku la Ambuye.
vous livrerez un tel individu à Satan pour la destruction de la chair, afin que l'esprit soit sauvé au jour du Seigneur Jésus.
6 Kudziwa kwanu si kwabwino. Kodi simukudziwa kuti yisiti wochepa amafufumitsa mphumphu yaufa wonse wa tirigu?
Votre vantardise n'est pas bonne. Ne savez-vous pas qu'un peu de levure fait lever toute la masse?
7 Chotsani yisiti wakale kuti mukhale ndi mphumphu yopanda yisiti, monga inu muli. Pakuti Khristu, Mwana Wankhosa wa Paska wathu, anaperekedwa nsembe.
Débarrassez-vous du vieux levain, afin que vous soyez une pâte nouvelle, comme vous êtes sans levain. En effet, le Christ, notre Pâque, a été sacrifié à notre place.
8 Choncho, tiyeni tisunge chikondwererochi, osati ndi yisiti wakale, wowononga ndi woyipa, koma ndi buledi wopanda yisiti, buledi woona mtima ndi choonadi.
Célébrons donc la fête, non pas avec du vieux levain, ni avec un levain de malice et de méchanceté, mais avec les pains sans levain de la sincérité et de la vérité.
9 Ndakulemberani mʼkalata yanga kuti musayanjane nawo anthu achigololo.
Je vous ai écrit dans ma lettre de ne pas fréquenter les pécheurs sexuels;
10 Pamenepatu sindikutanthauzatu anthu a dziko lapansi lino amene ndi achigololo, kapena aumbombo, kapena opeza ndalama mwachinyengo, kapena opembedza mafano. Kukanatero mukanangochoka mʼdziko lapansi lino.
mais pas du tout avec les pécheurs sexuels de ce monde, ni avec les cupides et les extorqueurs, ni avec les idolâtres, car alors il vous faudrait quitter le monde.
11 Koma tsopano ndikukulemberani kuti musayanjane ndi aliyense amene adzitcha mʼbale koma ndi wachigololo, kapena waumbombo, kapena wopembedza mafano, kapena wonamizira anzake, woledzera kapena wopeza ndalama mwachinyengo. Munthu wotere ngakhale kudya, osadya naye pamodzi.
Or, je vous ai écrit de ne pas vous associer à quelqu'un qu'on appelle frère et qui est un pécheur sexuel, ou un cupide, ou un idolâtre, ou un calomniateur, ou un ivrogne, ou un extorqueur. Ne mangez même pas avec une telle personne.
12 Kodi ndipindulanji kuti ndiweruze anthu amene si a mu mpingo? Kodi simuyenera kuweruza iwo amene ali mu mpingo?
En effet, qu'ai-je à voir avec le fait de juger aussi ceux qui sont dehors? Ne jugez-vous pas ceux qui sont au dedans?
13 Mulungu adzaweruza akunja. “Chotsani woyipayo pakati panu.”
Mais c'est Dieu qui juge ceux du dehors. « Éliminez le méchant du milieu de vous-mêmes. »

< 1 Akorinto 5 >