< 1 Akorinto 12 >

1 Tsopano abale anga okondedwa, sindikufuna mukhale osadziwa za mphatso za Mzimu.
Or, en ce qui concerne les choses spirituelles, frères, je ne veux pas que vous soyez ignorants.
2 Inu mukudziwa kuti pamene munali akunja, ankakusocheretsani mʼnjira zosiyanasiyana ndi kukukokerani ku mafano osayankhula.
Vous savez que, lorsque vous étiez païens, vous vous laissiez entraîner vers ces idoles muettes, quelle que soit la manière dont vous vous laissiez entraîner.
3 Nʼchifukwa chake ndikuwuzani kuti palibe munthu amene ali ndi Mzimu wa Mulungu angayankhule kuti, “Yesu atembereredwe,” ndiponso palibe munthu anganene kuti “Yesu ndi Ambuye,” popanda kutsogozedwa ndi Mzimu Woyera.
C'est pourquoi je vous fais connaître que nul, parlant par l'Esprit de Dieu, ne dit: « Jésus est maudit. » Personne ne peut dire: « Jésus est Seigneur », si ce n'est par le Saint-Esprit.
4 Pali mphatso zosiyanasiyana, koma Mzimu yemweyo.
Il y a plusieurs sortes de dons, mais un seul et même Esprit.
5 Pali mautumiki osiyanasiyana koma Ambuye yemweyo.
Il y a diverses sortes de services, et le même Seigneur.
6 Pali magwiridwe antchito osiyanasiyana, koma Mulungu yemweyo amagwira ntchito monsemo mwa anthu onse.
Il y a diverses sortes d'œuvres, mais le même Dieu qui opère toutes choses en tous.
7 Tsono Mzimu amapereka mphatso kwa aliyense kuti ipindulire onse.
Mais à chacun est donnée la manifestation de l'Esprit pour le profit de tous.
8 Mzimu amapereka kwa munthu wina mawu anzeru, Mzimu yemweyonso amapereka kwa wina mawu achidziwitso.
En effet, à l'un est donnée par l'Esprit la parole de sagesse, à un autre la parole de connaissance selon le même Esprit,
9 Kwa wina, Mzimu yemweyo amapereka chikhulupiriro, kwa wina mphatso zamachiritso, Mzimu yemweyo.
à un autre la foi par le même Esprit, à un autre le don des guérisons par le même Esprit,
10 Kwa wina mphamvu zochita zodabwitsa, kwa wina mawu a uneneri, kwa wina mphatso yozindikira mizimu, kwa wina malilime osiyanasiyana, ndiponso kwa wina kutanthauzira malilimewo.
à un autre l'action des miracles, à un autre la prophétie, à un autre le discernement des esprits, à un autre la diversité des langues, à un autre l'interprétation des langues.
11 Zonsezi ndi ntchito za Mzimu mmodzi yemweyo, ndipo amapereka kwa munthu aliyense monga momwe Mzimuyo wafunira.
Mais c'est un seul et même Esprit qui produit tout cela, distribuant à chacun séparément ce qu'il veut.
12 Thupi ndi limodzi, ngakhale kuti lapangidwa ndi ziwalo zambiri. Ndipo ngakhale ziwalo zake zonse ndi zambiri, zimapanga thupi limodzi. Momwemonso ndi mmene alili Khristu.
Car, comme le corps est un et a plusieurs membres, et que tous les membres du corps, étant nombreux, ne forment qu'un seul corps, ainsi en est-il de Christ.
13 Pakuti tonse tinabatizidwa ndi Mzimu mmodzi mʼthupi limodzi. Myuda kapena Mgriki, kapolo kapena mfulu tonse tinapatsidwa kuti timwe Mzimu mmodzi yemweyo.
Car c'est dans un seul Esprit que nous avons tous été baptisés pour former un seul corps, Juifs ou Grecs, esclaves ou libres, et que nous avons tous été abreuvés dans un seul Esprit.
14 Tsopano thupi silinapangidwe ndi chiwalo chimodzi koma ndi ziwalo zambiri.
Car le corps n'est pas un seul membre, mais plusieurs.
15 Ngati phazi litanena kuti, “Pakuti sindine dzanja, sindine chiwalo cha thupi.” Chifukwa chimenechi sichingachititse phazi kuti lisakhale chiwalo cha thupi.
Si le pied dit: « Je ne suis pas la main, je ne fais pas partie du corps », il ne fait donc pas partie du corps.
16 Ndipo ngati khutu litanena kuti, “Pakuti sindine diso, sindine chiwalo cha thupi.” Chifukwa chimenechi sichingachititse khutu kuti lisakhale chiwalo cha thupi.
Si l'oreille disait: « Parce que je ne suis pas l'œil, je ne fais pas partie du corps », elle ne ferait donc pas partie du corps.
17 Kodi thupi lonse likanakhala diso, tikanamamva bwanji? Nanga thupi lonse likanakhala khutu, tikanamanunkhiza bwanji?
Si le corps tout entier était un œil, où serait l'ouïe? Si tout le corps était une ouïe, où serait l'odorat?
18 Koma zoona nʼzakuti, Mulungu anayika ziwalo mʼthupi, chilichonse monga momwe Iye anafunira.
Mais maintenant, Dieu a placé les membres, chacun d'eux, dans le corps, comme il l'a voulu.
19 Nanga zonse zikanakhala chiwalo chimodzi, ndiye thupi likanakhala lotani?
S'ils étaient tous un seul membre, où serait le corps?
20 Mmene zililimu, pali ziwalo zambiri koma thupi ndi limodzi lokha.
Mais maintenant, ils sont plusieurs membres, mais un seul corps.
21 Diso silingawuze dzanja kuti, “Iwe sindikukufuna!” Ndipo mutu sungawuze phazi kuti “Iwe sindikukufuna!”
L'œil ne peut pas dire à la main: « Je n'ai pas besoin de toi », ni la tête aux pieds: « Je n'ai pas besoin de toi. »
22 Mʼmalo mwake, ziwalo zathupi zimene zimaoneka ngati zofowoka ndizo zili zofunikira kwambiri,
Non, bien plutôt, les membres du corps qui semblent plus faibles sont nécessaires.
23 ndipo ziwalo zathupi zimene timaziyesa zopanda ulemu, ndizo timazilemekeza kwambiri. Ndipo ziwalo zosaoneka bwino ndizo zimalandira ulemu wapadera.
Les parties du corps qui nous paraissent moins honorables, nous les honorons plus abondamment; et nos parties non visibles ont plus de pudeur,
24 Koma ziwalo zooneka bwino, nʼkosafunika kuti tizisamalire mwapadera. Mulungu polumikiza ziwalo zathupi, anapereka ulemu wopambana kwa ziwalo zimene zimafunadi ulemuwo
tandis que nos parties visibles n'en ont pas besoin. Mais Dieu a composé le corps ensemble, en donnant plus d'honneur à la partie inférieure,
25 kuti pasakhale kugawikana mʼthupi koma kuti ziwalo zonse zisamalirane.
afin qu'il n'y ait pas de division dans le corps, mais que les membres aient le même soin les uns des autres.
26 Ngati chiwalo chimodzi chikumva kuwawa, ziwalo zonse zimamvanso kuwawa. Ngati chiwalo chimodzi chilandira ulemu, ziwalo zonse zimakondwera nawo.
Si un membre souffre, tous les membres souffrent avec lui. Quand un membre est honoré, tous les membres se réjouissent avec lui.
27 Tsopano inu ndinu thupi la Khristu, ndipo aliyense wa inu ndi chiwalo cha thupilo.
Or, vous êtes le corps du Christ, et ses membres individuellement.
28 Ndipo Mulungu mu mpingo anayika poyamba atumwi, kachiwiri aneneri, kachitatu aphunzitsi, kenaka ochita zozizwitsa, ena a mphatso zamachiritso, ena a mphatso yothandiza anzawo, ena a mphatso yotsogolera ndiponso ena a mphatso ya malilime.
Dieu a établi certains dans l'assemblée: premièrement des apôtres, deuxièmement des prophètes, troisièmement des docteurs, puis des thaumaturges, puis des dons de guérison, d'assistance, de gouvernement et de langues diverses.
29 Kodi onse ndi atumwi? Kodi onse ndi aneneri? Kodi onse ndi aphunzitsi? Kodi onse amachita zozizwitsa?
Tous sont-ils apôtres? Sont-ils tous prophètes? Sont-ils tous des enseignants? Sont-ils tous des thaumaturges?
30 Kodi onse ali ndi mphatso zamachiritso? Kodi onse amayankhula malilime? Kodi onse amatanthauzira malilime?
Ont-ils tous des dons de guérison? Parlent-ils tous en diverses langues? Tous interprètent-ils?
31 Koma funitsitsani mphatso zopambana. Tsopano ndikuonetsani njira yopambana kwambiri.
Mais désirez ardemment les meilleurs dons. D'ailleurs, je vous montre une voie excellente.

< 1 Akorinto 12 >