< Yohani 7 >
1 Pambele uYesu atakaluta mufikaaja ifya mu kighavo ikya Galilaya, naakalondagha kuluta kukighavo ikya Yudea, u'wakuva aVayahudi vakalondagha kukum'buda.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 Unsiki ughwa kikulukulu kya Vayahudi ikya fyeve, ghulyale piipi kufika.
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 Avanuuna va Yesu vakam'buula uYesu vakati, “Lino uvuuke apa, ulute kukighavo ikya Yudea kuuti avavingilili vaako vafyaghe ifidegho fyako fino ghuvomba.
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 Umuunhu juno ilonda kukagulika, naivomba imbombo saake kuvusyefu, lino ulwakuva ghuvomba isi sooni, ghuhufie kuvaanhu vooni.”
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 Avanuuna valyajovile enendiiki, ulwakuva voope navalyamwitiike.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 Pe uYesu akavavuula akati, “Unsiki ghwango ghukyale pifika, looli umue ndepoonu muluta amasiki ghooni.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 Avaanhu ava mu iisi muno navangavakalalile umue, looli vikung'halalila une, ulwakuva nikuvaavuula kuuti, sino vivoomba mbiivi.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 Umue lutaghi kukikulukulu ikio; une naniluta ulwakuvaunsiki ghwango ghukyale pifika.
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 U Yesu ye ajovile aghuo akajigha mu kighavo ikya Galilaya.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 Neke avanuuna ye valutile ku kikulukulu, ghwope u Yesu akaluta, neke akaluta kisyefu, kisila kuhufia kuvaanhu. Kukikulukulu ukuo,
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 aVayahudi vakava vikumulonda u Yesu viposia kuvaanhu vitii, “Alikuughi?”
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 Avaanhu vinga mulipugha lila. Vakava vikujovasia, vamo vitii, “Umuunhu ujuo nnofu.” Avange vitii, “Ndali, umuunhu ujuo isofia avaanhu.”
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 Neke nakwealyale umuunhu juno alyale ijova imhola saake pa vuvalafu, ulwakuva vakoghopagha aVayahudi.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 Pakate pa fighono ifya kikulukulu u Yesu akingila mu luviika ulwa nyumba inyimike ija kufunyila, akatengula kuvulanisia avaanhu.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 Avayahudi vakava videgha vitii, “Umuunhu uju akaghwile ndaani isi, kisila kwimba?
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 Pe pano U Yesu akavamula akati, “Imbulanisio soni nivulanisia na sango, looli sihumile kwa juno asung'hile.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 Umuunhu juno ilonda kuvomba isa vughane vusa Nguluve, ikagula kuuti imbulanisio isi sihumile Nguluve, nambe kuuti nijova muvutavulilua vwango juune.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 Umuunhu juno ijova muvutavulilya vwake jujuo, ilonda avaanhu vamug'hiniaghe. Neke umuunhu juno ilonda vamughiniaghe juno ansunghile, ujuo ijova isa kyang'haani, naijova isa vudesi.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 U Moose naalyavapeliile umue indaghilo? Neke nakwalemambe jumo pakate palyumue juno ivingilila indaghilo isio. Lino kiki milonda pikumbuda?”
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 Avaantu mu lipugha lila vakamwamula vakati, “Uli ni lipepo uve. Ghwe veeni juno ilonda pikukubuda?”
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 U Yesu akavamula akati, “Une nikavombile ikidegho kimo, umue mweni mukakenyemuka.
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 U Moose alyalaghiile kuvomba ikivungo ikya kudumula ingola ija kidiimi avaana viinu. Ululaghilo uluo nalulyahumile kwa Moose, looli lulyahumile kuvakuulu viinu. Umue muvomba uluo nambe nambe kive kighono kya Sabati.
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 Lino nave lukwitikisivua umwana kuvombelua ikivungo ikio mukighono ikya Sabati kuuti muleke kudeenya ululaghilo ulwa Moose, kiki mukung'halalila une. Kukunsosia umuunhu mu kighono ikya Sabati?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Mulekaghe kuhiga umuunhu mulwa kulola pamaaso, looli muhighaghe mu vwakyang'haani.
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Avaanhu vamonga ava mu likaaja ilya Yelusalemu vakava viposania vitii, Asi, umuunhu uju naghwe juno avalongosi va Vayahudi vilonda kukumbuda?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 Lolagha ijova pa vuvalafu, neke avene naijova kimonga! Pamo aveene avolongosi vitii umuunhu uju lweli ghwe Kilisite!
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 Ukilisite iliiva ikwisa nakwale nambe muunhu juno ilikagula kuno ihumila! Umuunhu uju kuno ihumatukagwile.
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 U Yesu ye ajhighe ivulanisia mu luviika ulwa nyumba inyimike ija kufunyila, akajova fiijo akati, “Lweli umue mweni mung'haghwile une, kange mukaghwile kuno nihuma. Nambe mwiti mukagwile uluo,
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 une nanilisile mu vutavulilua vwango, ulwene juno asung'hile une ghwa kyang'haani, umue namunkagwile.
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 Une ninkagwile ulwakuva nihumile kwa mwene, kange ghwe juno asung'hile. Pepano vakava vilonda kukunkola, neke nakwealyale umuunhu juno akaghela kukunkola, ulwakuva unsiki ghwake ughwa kukolua ghulyakyale kufika.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 Avaanhu vinga mu lipugha lila vakamwitika. Vakava vijova viiti, “Iliiva ikwisa uKiliste ilivomba ifidegho kukila fino avombile uju?”
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 Avafalisayi vakapulika ilipugha lya vaanhu vipwepa vwimila imhola sa Yesu, pe avavaha va vatekesi na Vafalisayi vakasuung'ha avasikali kuuti vankole.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 Pepano uYesu ajajova akati, “Niiva numue unsiki n'debe vuvule, neke pambele nigomoka kwa juno asun'ghile.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 Mulikundoonda, neke namulikunyaagha, kange kuno niliiva, umue namungafike.”
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 Pe aVayahudi vakava viposania viiti, “Umuunhu uju iluta kuughi kuno usue natunga mwaghe? Asi, iluya ku vano Vapalasiine vano nkate mu vaYunani na kukuvavulanisia avaYunani?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 Asi, kwe kuti kiki pano iiti, 'Mulikundonda, neke namulikunyaagha, kange kuno niliiva umue namungafike?”
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 Ikighono ikya vusililo ikya kikulukulu kya fyeve, kino kilyale kighono kivaha, uYesu akiima akajova fiijo akati, “Umuunhu nave ali ni kyumilua, iise kulyune anyue.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 Umuunhu juno ikunyitika une, iiva ndavule ghijova amalembe amimike kuuti, isaasa isa malenga amanya vwumi sidwivuka mu mwojo ghwake.
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 Alyajovile uluo mu mhola ija mhepo uMwimike, juno avaanhu vano vikumwitika vilikumwupila pambele, unsiki ughuo, uNguluve alyakyale kukunsuung'ha umhepo ghwake, ulwakuva alyakyale kuhufia kuvaanu uvuvaha vwa Yesu.
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 Avaanhu vamonga mu lipugha lila ye vapuliike amasio aghuo, vakati, “Kyang'haani, umuunhu uju m'bili.”
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 Vamonga vakati, “Umuunhu uju ghwe Kilisite.” Neke avange vakati, “Ndali, uKilisite ndepoonu ihuma ku Galilaya?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 Asi amalembe amimike naghiiti uKilisite ilihuma mu kikolo ikya ntwa u Daudi ku kikaaja ikya Bethelehemu, kikaaja kino alyale ikukukala untwa uDaudi?
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 Pepano avaanhu vakalekeng'hana vivimila uYesu.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 Avaanu vamonga mu lipugha lila vakava vilonda kuku nkola, neke nakwealyale umuunhu juno akaghela kuku nkola.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 Avasikali vala vakagomoka ku vavaha va vatekesi na kuVafalisayi, kisila kunkola uYesu. Avavaha vala vakavaposia vakati, “Kiki namunkolile na kukumuleeta?”
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 Avasikali vala vakamula vakati, “Naaghelile kuhumila umuunhu juno ijova ndavule umuunhu jula.
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 Avafalisayi vakavaposia vakati, “Kwekuti najumue musyangilue?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Asi ghwe veeni mu valongosi viitu nambe mu Vafalisayi juno amwitiike?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 Ulwene avanu avuo avuo navasikagwile indaghilo sa moose, avuo vaghunilue.”
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 Pepano uNikodemu (umo mu valongosi va Vafalisayi, juno ikighono kimonga alyalutile kwa Yesu pakilo), akavaposia akati,
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 “Asi indaghilo siitu sikwitikisia kukumhigha umuunhu kisila kumpulikisia na kukusitang'hania sino avombile?”
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 Aveene vakamwamula vakati, “Neke najuuve uhumile ku Galilaya? Londagha muMalembe amimike pekyaghukagula kuuti nakwale umbili juno ahumile ku Galilaya.”
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.