< Imbombo 1 >

1 Ikitabu ikyapakaliikyapakali nilyakilembile, Theofilo, nikajova soni sino alyasitenguile uYesu kuvomba na kuvulanisia,
Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
2 kudughila ikighono kino umwene alyapelilue kukianya. Uulu luliale yeluhumile ululaghilo kuhumila kw Mhepo mwimike kuvavulanesivua vano alyavasaluile.
mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
3 Ye sikilile imumuko sa Vene, umwene alyavonike kuvanave mwuumi kange na sising'ilisio nyinga sikoleleuagha. Mufighono fijigho fine alihufisiealihufisie kuvene, napikwolelela vumila isa vatwa va Nguluve
Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
4 Panorama akatang'anagha navope, pe akavalaghilagha kuti navangavukaghe mhu Yerusalemu, loli vaghulilaghe ulyalufingo lwa Nata, lino, alyatile, “Mulyapulike kuhuma kuliune
Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
5 kuti uYohanauYohana aliofuighe ulyofugho lwa malenga, loli umue mkwofughuagha nhu Mhepo mwimike mofighono fififii fidebe.”
Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
6 Pano ye vakong'anile palikimo valyamposisie, “Mutwa, kwekuti ku uulu ghilikuvagomokesia avanhu va Israeli uvutwa?”
Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7 Umwene akavavula akaati, “nalunoghile kuliumue kukagula amasiki Ghana uNata afumbilue kuvatavulilua va mwene jujuo.”
Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
8 Loli mukupila ingufu, unsiki ghuno ilikwisa kuliumue uMhepo umwimike; umue muliva volesi vango kuoni muYerusalem name muYahudi mwoni ni Samaria na kuvusililokuvusililo vwa iisi.”
Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9 U Mutwa Yesu yamalile kujova isi, avenue yevilola kukyanya, umwene akanyanyulivua kukianya, ilifunde likakupikila valeke kumuagha name Mason ghavanave.
Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10 Pano vakalolagha kukyanya nhuvusyukue yeiluta, nakalingi, avanhu vavili valyiima pakati name Kati pavanave vafwalile amanda amavalafu.
Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
11 Vakati, “Umue me vanhu va mugalilaya, lwakiiki mwimile apa mulola kukyanya?” U Yesu uju Juno atoghile kukyanya iligomoka lulalula ndavule mumbwene iluta kukyanya.
Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
12 Pepano vakagomoka kuhuma kukidunda kya mizeituni, kind kilipipi nii Yerusalem, ulughendo ulwa kighono ikya sabati.
Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
13 Ye vafikilevafikile vakaluta kugholofa kuno vakikalagha. Vope veva Ptro, Yohana, Yakobo, Andrea, Filipino, Thomas, Batholomayo, Matayo, Yakobo, Mwana wa Afayo, Simon Zelote, nhu Yuda Mwana wa Yakobo.
Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
14 Voni vakakolana aka huana munhu jumbo, ningufu vakaghendelela ni nyifunyo. Palikimo na vope pevaliale avakimama, Maliamu ung'ina ghwa Yesu na valumbu va mwene.
Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15 Mufighono fila uPetro akima pakate nakate navanyalukolo avanhu kilundo kimo night fijigho fivili, akati,
Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
16 Vanyalukolo, lulyanoghile Kati amalembe ghakwilanilaghe pano pakali uMhepo mwimike akajovelagha muloomo ghwa Daudi ulwakuling'ana nhu Yuda, alyamendime kuvala vano valya n'kolile uYesu.
Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
17 Ulwakuva umwene alyale njiitu alyiupile ikighelelo kya mwene mumboo jiitu iiji.”
Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18 (lino umunhu uju alyaghulile ikivanja kind aliipile nhuvuhosi vwa mwene apuo pe akaghwisagha akalongosiagha umutu, umbili ghukadendemuka namaleme ghakakung'ika niiki ghakava pavugholofu.
(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
19 Voni vanovakakilagha muYerusalemu valyasipulike soni isi, pe ikivanja ikio pevakakipela kunjovele javanave “Akelidama”ughu ghwe “mughunda ghwa Dana.”)
Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20 “Mukitabu kya Zaburi lilembilue, 'ghuula umughunda ghuake ghuva wa kuhama kwejeje name jumonga nangikalaghe Pala;' name, 'Tavulile umunhu ujunge atole inafasi jamwene ijavulongosi.'
Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21 Uluo lwakyang'ani, lino, jumbo umughosi vakavingilisaniagha pano uMutwa Yesu alyahumile napikwingila muliusue,
Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
22 kutengulila kulwofugho lwa Yohana kufika ikighono Kira kinda akatolwagha kukyanya, anoghile piva mwolesi ghwa lusyiuko palikimopalikimo nusue.
kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23 “Vakavavika pavulongolo avaghosi vaviili, Yusufu Juno akatambulivugha Balinaba, junoghuope akatambulivagha Yusto nhu Maria.
Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
24 Avene vakifunyagha vakatisagha, “Uve, Mutwa, ghwejuno ukagwile amojo gha vanhu voni, tuvikiile pavugholofu ghwe Venice muvanhu avaviili Juno usaluile.
Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
25 Uwakuhala imbombo ija vwomolia jino akajile uYuda Juno akahokile ghwejuno ahaliile papa mwene.”
kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
26 Vakavatovela ikuura vavuo, ni kura jikamughwila Mathia wejuno akavalilua palikimo na vasung'wa kijigho najumo.
Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

< Imbombo 1 >