< Ісая 27 >
1 У той день наві́дає Господь Своїм тверди́м, і дужим та сильним мече́м левіята́на, змія прудко́го, і левіята́на, змія звивко́го, і драко́на, що в морі, заб'є.
Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
2 У той день заспівайте про нього, про виноградник прина́дний:
Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
3 Я Господь, його Сто́рож, щохвилі його Я напо́юю; щоб хто не наві́дав його, стережу́ його вдень та вночі,
Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
4 Я гніву не маю. Хто Мені дасть терни́ну й будя́ччя, — на бій Я піду́ проти них, і спалю́ їх усіх!
Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
5 Хіба буде держа́тися міцно Мого він за́хисту, щоб мир учини́ти зо Мною, зо Мною щоб мир учини́ти!
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
6 Яків у майбу́тньому пу́стить корі́ння, розцвіте́ться Ізра́їль і пу́п'янки пу́стить, і поверхню вселенної пло́дом напо́внять.
Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
7 Чи Він ура́зив його, як ура́зив того, хто бив був його? Чи він був забитий, як забиті були його вби́вники?
Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
8 Ти вигнав його, відіслав його й су́дишся з ним, вигнав його Своїм по́дувом сильним у день схі́днього вітру.
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
9 Тому вина Якова буде оку́плена цим, а це плід увесь: усу́нення з нього гріха́, коли він учинить каміння все же́ртівника побитим, немов грудки́ крейди, і не стоятимуть більше Аста́рти, і стовпи́ на честь сонця.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
10 Бо місто укрі́плене буде само́тнє, мешка́ння покинене та позоста́влене, мов би пустиня, — там па́стися буде теля, і там буде лежати воно, та пони́щить галу́зки його.
Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 Коли ви́сохнуть ві́ття його, то пола́мане буде, — жінки при́йдуть і спалять його. А що це нерозумний наро́д, тому милосердя до нього Творе́ць його мати не буде, і не буде ласка́вий до нього Створи́тесь його́.
Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
12 І станеться в день той, плоди́ помоло́тить Господь від бігу ріки до потоку єгипетського, а ви по одно́му позби́рані будете, сино́ве Ізраїля!
Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
13 I станеться в день той, і буде засу́рмлено в велику сурму́, і при́йдуть, хто гинув у кра́ї асирійському, і вигна́нці до кра́ю єгипетського, і будуть вони на святій горі в Єрусалимі вклонятися Господе́ві.
Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.