< Ездра 4 >
1 І почули Юдині та Веніяминові вороги́, що вигна́нці будують храма Господе́ві, Богові Ізраїля.
Adani a Yuda ndi Benjamini anamva kuti anthu obwera ku ukapolo aja akumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli.
2 І прийшли вони до Зорова́веля та до голів ба́тьківських родів, та й сказали їм: І ми бу́демо будува́ти з вами, бо ми зверта́ємось, як ви, до вашого Бога, і ми прино́симо Йому жертви від днів Есар-Хаддона, царя асирійського, що привів нас сюди“.
Tsono anapita kwa Zerubabeli ndi kwa atsogoleri a mabanja awo ndi kunena kuti, “Mutilole kuti tikuthandizeni kumangaku chifukwa ife timapembedza Mulungu wanu monga momwe mumachitira inu, ndipo takhala tikupereka nsembe kwa Iye kuyambira nthawi ya Esrahadoni, mfumu ya ku Asiriya, amene anabwera nafe kuno.”
3 І сказав їм Зоровавель і Ісус, та решта голів батьківських родів Ізраїлевих: „Не вам і нам разом будувати храм для Бога! Самі бо ми бу́демо будувати для Господа, Бога Ізраїлевого, як наказа́в нам цар Кір, цар перський“.
Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”
4 І став народ тієї землі осла́блювати руки Юдиного наро́ду та страха́ти їх при будува́нні.
Tsono anthu a mʼdzikomo anayamba kuchititsa ulesi anthu a ku Yuda, ndi kuwachititsa mantha kuti aleke ntchito yomangayo.
5 І підку́плювали вони проти них дора́дників царськи́х, щоб залама́ти їхній за́дум, по всі дні Кіра, царя перського, й аж до царюва́ння Да́рія, царя перського.
Analemba alangizi ena kuti alepheretse cholinga chawo pa ntchitoyo pa nthawi yonse ya Koresi, mfumu ya ku Perisiya, ndiponso mpaka pamene Dariyo mfumu ya ku Perisiya ankalamulira dzikolo.
6 А за царя Ахашвероша, на поча́тку його царюва́ння, написали вони оска́рження на ме́шканців Юдеї та Єрусалиму.
Mfumu Ahasiwero atangoyamba kulamulira dzikolo, adani aja analemba kalata yoneneza anthu a Yuda ndi Yerusalemu.
7 А за днів Артаксеркса написав Бішлам, Мітредат, Товеїл та решта товаришів його до Артаксеркса, царя перського. А лист був написаний по-араме́йськи, а перекладений по-перськи.
Ndiponso mʼnthawi ya Aritasasita mfumu ya Perisiya, Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli ndi anzawo ena analemba kalata inanso kwa Aritasasita. Kalatayo inalembedwa mʼChiaramu ndipo ankatanthauzira poyiwerenga.
8 Начальник Рехум та писар Шімай написали одно́го листа проти Єрусалиму до царя Артаксеркса отак.
Rehumu mkulu wankhondo ndi Simisai mlembi, nawonso analemba kalata yawo yoneneza anthu a ku Yerusalemu kwa mfumu Aritasasita. Anayilemba motere:
9 Тоді начальник Рехум та писар Шімшай та решта товариші́в його, судді й урядники, писарчуки, писарі, аркев'я́ни, вавило́няни, шушаня́ни, цебто еламі́ти,
Kalata yochokera kwa Rehumu, mkulu wa gulu lankhondo, mlembi Simisai ndi anzawo awa: oweruza, nduna, akuluakulu ena, anthu a ku Peresiya, Ereki, Babuloni, Susa mʼdziko la Elamu,
10 та решта наро́дів, яких повиганяв Аснаппар, великий та славний, й осадив їх у місті Самарії та в решті Заріччя.
ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.
11 Оце ві́дпис листа, що послали до нього: „До царя Артаксеркса твої раби, люди Зарі́ччя. І ось
Mawu a mʼkalata ya kwa Aritasasita anali awa: Kwa mfumu Aritasasita: Kuchokera kwa atumiki anu, anthu a kutsidya kwa Yufurate:
12 щоб було відо́ме цареві, що Юдеї, які вийшли від тебе до нас, прибули́ до Єрусалиму. Вони будують місто бунтівни́че та шкідли́ве, і вдоскона́люють мури, а підва́лини поліпши́ли.
Amfumu tati mudziwe kuti Ayuda amene anabwera kuno kuchokera kwanuko apita ku Yerusalemu ndipo akumanganso mzinda wa anthu owukira ndi oyipa uja. Akumaliza makoma ake ndipo akukonzanso maziko.
13 А тепер щоб було відо́ме цареві, що коли тільки це місто буде збудо́ване, а мури закі́нчаться, вони не будуть давати ані дани́ни, ані пода́тку, ані мита, а це буде шкодити царсько́му прибу́ткові.
Kuwonjeza apo amfumu mudziwe kuti ngati amalize kumanganso mzindawu ndi kukonzanso makoma ake, adzaleka kukhoma msonkho, kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko kapena msonkho wina uliwonse, ndipo chuma cha thumba la ufumu chidzachepa.
14 І ото, беручи́ на увагу, що сіль царського пала́цу — сіль наша, а царськи́й сором не випадає нам бачити, тому ми посилаємо й завідомля́ємо царя,
Popeza tsono ife timadya nawo kwa mfumu sitiyenera tizingoonerera zinthu zochititsa mfumu manyazi. Nʼchifukwa chake tikutumiza uthenga kwa inu a mfumu kuti mudziwe zonse.
15 щоб пошукали в книзі споминів батьків твоїх, і ти зна́йдеш у книзі споминів, і знатимеш, що місто це — місто бунтівни́че та шкідли́ве царям та окру́гам, і що в ньому підійма́ли бунт від праві́ку, чому́ місто це було зруйно́ване.
Choncho pachitike kafukufuku mʼbuku la mbiri yakale ya makolo anu. Mʼbuku la mbiri zakale mudzapezamo ndi kuwerenga kuti mzinda umenewu ndi waupandu, wosautsa mafumu ndi nduna zamʼmadera zomwe. Kuyambira kale wakhala ukuwukira ulamuliro uliwonse. Nʼchifukwa chake mzinda umenewu anawuwononga.
16 Ми сповіщаємо царя, що коли тільки місто це буде добудо́ване, а мури закі́нчаться, то через те не бу́де тобі частки в Зарі́ччі“.
Tsono tikukudziwitsani amfumu kuti ngati mzinda umenewu umangidwanso ndi makoma ake nʼkutsirizidwanso ndiye kuti inu simudzalamuliranso chigawo cha patsidya pa Yufurate.
17 Цар послав відповідь: „Начальникові Рехумові, і писареві Шімшаєві, та решті їхніх товаришів, що сидять у Самарії, і решта Заріччя: Мир вам! А тепер, —
Mfumu inatumiza yankho ili: Mkulu wa gulu lankhondo Rehumu, mlembi Simisai ndi anzanu onse amene akukhala ku Samariya ndi mʼzigawo zina zonse za Patsidya pa Yufurate. Landirani moni.
18 лист, якого ви послали до нас, вира́зно прочи́таний передо мною.
Kalata imene munatumiza ija yawerengedwa bwino lomwe pamaso panga.
19 І був ви́даний від мене нака́з, і шукали та й знайшли, що місто це з да́вніх-даве́н підійма́лося на царів, і повста́ння та бунт робилися в ньо́му.
Ine nditalamula kuti afufuze nkhaniyi kwapezekadi kuti mzinda umenewu uli ndi mbiri yowukira mafumu ndi kuti zaupandu ndi zowukira zinkachitikadi mʼmenemo.
20 І могу́тні царі були́ над Єрусалимом, і панували в усьо́му Зарі́ччі, а дани́на, пода́ток та мито давалися їм.
Mafumu amphamvu akhala akulamulira Yerusalemu ndi chigawo chonse cha Patsidya pa Yufurate. Iwo ankalandira msonkho ndi kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko pa kanthu kena kalikonse.
21 А тепер видайте нака́за, щоб спини́лися ці люди, а місто це не будува́лося, поки від мене не буде ви́даний новий нака́з.
Tsopano inu khazikitsani lamulo kuti anthu amenewo asiye ntchitoyo, asamangenso mzindawo mpaka ine nditalamula
22 І будьте бе́режні, щоб через це не зробити по́милки. На́що рости́ме зло на шкоду царям?“
Musachedwe kuchita zimenezi. Kodi ine ndingalole bwanji kuti zowononga zotere zikule ndi kupweteka ine mfumu?
23 Тоді, як тільки був прочи́таний ві́дпис листа царя Артаксеркса перед Рехумом і писарем Шімшаєм та їхніми товариша́ми, пішли вони поспішно до Єрусалиму, і спини́ли роботу їх зброєю та насиллям!
Kalata ya mfumu Aritasasitayi itangowerengedwa pamaso pa Rehumu ndi Simisai mlembi uja, ndi anzawo onse, iwo anapita msangamsanga ku Yerusalemu kukawaletsa Ayuda aja mwamphamvu kuti asapitirire ntchito yawo.
24 Тим спинилася робота Божого дому, що в Єрусалимі, і спини́лася вона аж до другого року царюва́ння Дарія, царя перського...
Motero ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu inayimitsidwa mpaka chaka cha chiwiri cha ulamuliro wa Dariyo mfumu ya ku Perisiya.