< До галатів 1 >
1 Павло, апостол, [покликаний] не людьми і не людиною, а Ісусом Христом і Богом Отцем, Який воскресив Його з мертвих,
Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
2 разом з усіма братами. Церквам Галатії.
pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
3 Благодать вам і мир від Бога, нашого Отця, і від Господа Ісуса Христа,
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
4 [Який, ] віддавши Самого Себе за наші гріхи, визволив нас від нинішнього злого віку згідно з волею Бога й Отця нашого, (aiōn )
Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn )
5 Якому слава навіки-віків! Амінь. (aiōn )
Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
6 Я здивований, що ви так швидко відвертаєтеся від Того, Хто покликав вас благодаттю Христа, заради іншої «доброї звістки».
Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
7 Насправді іншої немає, але існують деякі [люди], які бентежать вас і намагаються змінити Добру Звістку Христа.
umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
8 Але навіть якщо хтось із нас або ангел із неба буде проповідувати вам добру звістку, відмінну від тієї, яку ми вам проповідували, то нехай буде проклятий!
Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
9 Ми говорили вже раніше, і я ще раз повторюю: якщо хтось проповідує вам іншу добру звістку, а не ту, що ви прийняли, то нехай буде проклятий!
Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
10 Чиє схвалення я намагаюся завоювати: людей чи Бога? Хіба я намагаюся догодити людям? Якби я намагався догодити людям, я б не був рабом Христа.
Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
11 Я хочу, щоб ви, брати, знали, що Добра Звістка, яку я проповідував, не від людей.
Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
12 Бо я отримав і вивчив її не від якоїсь людини, але через одкровення Ісуса Христа.
Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
13 Ви чули про мій попередній спосіб життя в юдействі, як я завзято переслідував Церкву Божу й намагався її зруйнувати.
Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
14 В юдействі я перевершив багатьох моїх однолітків зі свого народу і був надзвичайно ревним до звичаїв моїх предків.
Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
15 Але коли Бог, Який обрав мене ще до мого народження, покликав мене через Свою благодать, уподобав
Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
16 відкрити мені Свого Сина, щоб я проповідував Його Добру Звістку серед язичників, тоді я не пішов відразу радитися з кимось із людей,
kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
17 не ходив також і до Єрусалима, до тих, що були апостолами до мене, але пішов в Аравію і знову повернувся в Дамаск.
Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
18 Потім, через три роки, я вирушив до Єрусалима, щоб познайомитися з Кифою, і пробув із ним п’ятнадцять днів.
Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
19 Інших же апостолів я не бачив, окрім Якова, брата Господнього.
Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
20 Я пишу вам і запевняю перед Богом, що не обманюю.
Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
21 Після того я пішов до земель Сирії та Килікії.
Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
22 Церкви Юдеї, що в Христі, мене особисто не знали.
Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
23 Вони лише чули, що той, хто раніше їх переслідував, зараз проповідує віру, яку колись намагався знищити,
Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
24 і прославляли Бога за мене.
Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.