< 2 до коринтян 13 >
1 Оце втретє йду до вас. «Нехай кожне слово підтвердиться устами двох або трьох свідків».
Uwu ndi ulendo wachitatu ndikubwera kudzakuyenderani. “Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.”
2 Як я попереджав, коли був у вас удруге, так і зараз, коли відсутній, попереджаю тих, що раніше згрішили, і всіх інших: якщо прийду знову, то нікого не щадитиму.
Ndinakuchenjezani kale pamene ndinali nanu ulendo wachiwiri uja. Tsopano ndikubwereza ndisanafike. Ndikabweranso sindidzachitira chifundo amene anachimwa poyamba paja kapena wina aliyense amene anachimwa,
3 Адже ви шукаєте доказу того, що через мене говорить Христос. Він не безсилий, але сильний у вас,
popeza mufuna chitsimikizo chakuti Khristu akuyankhula kudzera mwa ine. Iye siwofowoka pofuna kuchita nanu koma ndi wamphamvu pakati panu.
4 бо хоч Він і був розіп’ятий у слабкості, проте живе завдяки Божій силі. Адже і ми слабкі в Ньому, але завдяки Божій силі будемо жити з Ним для вас.
Pofuna kutsimikizira, anapachikidwa ali wofowoka koma ali ndi moyo mwamphamvu ya Mulungu. Chomwechonso, ife ndife ofowoka mwa Iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi naye ndi mphamvu ya Mulungu, potumikira pakati panu.
5 Перевіряйте самих себе, чи ви у вірі; випробовуйте себе. Хіба ви не знаєте, що Ісус Христос [живе] у вас? Звичайно, якщо ви пройшли це випробування.
Tadzisanthulani nokha kuti muone ngati muli mʼchikhulupiriro; dziyeseni nokha. Kodi simuzindikira kuti Khristu Yesu ali mwa inu, ngati si choncho mwalephera mayesowa?
6 А щодо нас, сподіваюся, ви зрозумієте, що ми пройшли це випробування.
Ndipo ndikhulupirira kuti mudzazindikira kuti ife sitinalephere mayesowo.
7 Тепер ми молимося Богові, щоб ви не чинили ніякого зла. Не для того, щоб здавалося, ніби ми пройшли випробування. Робіть добро, навіть тоді, коли здаватиметься, що ми не пройшли його.
Tsopano tikupemphera kwa Mulungu kuti musadzachite kanthu kena kalikonse kolakwa. Osati chifukwa choti anthu aone kuti ife tapambana mayesowo koma kuti mudzachite zokhoza ngakhale anthu atamationa ngati olephera.
8 Адже ми нічого не можемо робити проти істини, а лише заради істини.
Pakuti sitingachite chilichonse chotsutsana ndi choonadi, koma chokhacho chovomerezana ndi choonadi.
9 Ми радіємо, коли ми слабкі, а ви сильні. За це й молимося – за ваше вдосконалення.
Ife timasangalala kuti pamene tafowoka, inu muli amphamvu; ndipo pemphero lathu ndi lakuti mukhale angwiro.
10 Тому я й пишу вам це, поки мене з вами немає, щоб, коли буду з вами, мені не довелося бути суворим, використовуючи владу, яку дав мені Господь, щоб зміцнювати, а не руйнувати.
Nʼchifukwa chake ndimalemba zinthu zoterezi pamene ndili kutali, kuti ndikabwera ndisadzagwiritse ntchito ulamuliro wanga mokalipa, uwu ndi ulamuliro umene Ambuye anandipatsa kuti ndikukuzeni inu osati kukuwonongani.
11 І наостанок, брати, [заохочую вас: ] радійте, виправляйте одне одного, підбадьорюйте одне одного, будьте однодумні, живіть у мирі – і Бог любові й миру буде з вами!
Potsiriza abale, ndikuti tsalani bwino. Yesetsani kukhala angwiro, mvetsetsani pempho langa, khalani a mtima umodzi, khalani mwamtendere. Ndipo Mulungu wachikondi ndi mtendere adzakhala nanu.
12 Вітайте одне одного святим поцілунком!
Lonjeranani ndi mpsopsono wachiyero.
13 Усі святі вітають вас!
Anthu onse a Mulungu akupereka moni.
14 [Нехай] благодать Господа Ісуса Христа, любов Бога та спільність Святого Духа [будуть] з вами усіма!
Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mulungu, ndi chiyanjano cha Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.