< Дії 21 >
1 Коли ми розлучилися з ними, то попливли прямо до [острова] Кос, наступного дня на Родос, а звідти в Патару.
Titalawirana nawo, tinachoka kumeneko mʼsitima ya pamadzi, ndipo tinayenda molunjika mpaka kufika ku Kosi. Mmawa mwake tinapita ku Rode, kuchokera kumeneko tinapita ku Patara.
2 Знайшовши корабель, що прямував у Фінікію, ми сіли й попливли.
Kumeneko tinapeza sitima yapamadzi yopita ku Foinike. Choncho tinalowamo nʼkunyamuka.
3 Коли показався Кіпр, ми залишили його ліворуч, попливли до Сирії та причалили в Тирі, тому що там наш корабель мав вивантажити товар.
Tinaona chilumba cha Kupro ndipo tinadutsa kummwera kwake nʼkupita ku Siriya. Tinakayima ku Turo chifukwa sitima yathuyo imayenera kusiya katundu kumeneko.
4 Знайшовши учнів, ми пробули з ними сім днів. Вони, [довідавшись] через Духа [про майбутнє], застерігали Павла не йти до Єрусалима.
Tinafunafuna ophunzira kumeneko, ndipo titawapeza tinakhala nawo masiku asanu ndi awiri. Iwowa, mwa Mzimu Woyera anakakamiza Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
5 Але коли дні [перебування разом] закінчилися, ми пішли далі. Усі вони разом із дружинами та дітьми проводжали нас аж за місто, і на березі, схиливши коліна, ми помолилися.
Koma nthawi yathu itatha, tinachokako ndi kupitiriza ulendo wathu. Ophunzira onse pamodzi ndi akazi awo ndi ana anatiperekeza mpaka kunja kwa mzinda. Ndipo kumeneko tinagwada mʼmbali mwa nyanja ndi kupemphera.
6 Попрощавшись з усіма, ми піднялися на корабель, а вони повернулися до своїх домівок.
Titatsanzikana, tinalowa mʼsitima ija, iwowo anabwerera ku nyumba zawo.
7 Ми продовжили свою морську подорож і з Тира прибули в Птолеміаду, де, привітавши братів, пробули з ними один день.
Ife tinapitiriza ulendo wathu wochokera ku Turo mpaka tinafika ku Ptolemayi. Kumeneko tinalonjera abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi.
8 Наступного дня ми вирушили в дорогу, прийшли до Кесарії, зайшли в дім євангеліста Филипа, одного з сімох, і залишилися в нього.
Tinachoka mmawa mwake, mpaka tinakafika ku Kaisareya. Tinapita kukakhala mʼnyumba ya mlaliki Filipo, amene anali mmodzi mwa atumiki a mpingo asanu ndi awiri aja.
9 Він мав чотири незаймані доньки, які пророкували.
Iye anali ndi ana aakazi anayi osakwatiwa amene anali ndi mphatso ya uneneri.
10 Після того, як ми пробули там чимало днів, з Юдеї прийшов пророк, на ім’я Агав.
Titakhala kumeneko masiku ambiri, kunabwera mneneri wina wochokera ku Yudeya dzina lake Agabu.
11 Він підійшов до нас, узяв пояс Павла й, зв’язавши собі руки та ноги, сказав: «Святий Дух каже: „Так юдеї в Єрусалимі зв’яжуть та віддадуть у руки язичників чоловіка, якому належить цей пояс“».
Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’”
12 Почувши це, ми й місцеві стали благати Павла, щоб він не йшов до Єрусалима.
Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu kumeneko tinamudandaulira Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
13 Але Павло відповів: «Чому ви плачете й розриваєте моє серце? Я готовий не лише бути зв’язаним, але й померти в Єрусалимі за ім’я Господа Ісуса».
Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
14 Коли ми зрозуміли, що його не переконати, то заспокоїлись, сказавши: «Нехай станеться воля Господня».
Titalephera kumuletsa tinamuleka ndipo tinati, “Chifuniro cha Ambuye chichitike.”
15 Після тих днів ми зібралися й вирушили до Єрусалима.
Pambuyo pake, ife tinakonzeka ndi kunyamuka kumapita ku Yerusalemu.
16 Разом із нами [пішли] й учні з Кесарії, які провели нас до Мнасона з Кіпру, давнього учня, у якого ми залишилися.
Ena mwa ophunzira a ku Kaisareya anatiperekeza mpaka kukatifikitsa ku nyumba ya Mnasoni, kumene tinakonza kuti tizikhalako. Iye anali wa ku Kupro ndiponso mmodzi wa ophunzira oyambirira.
17 Коли ми прийшли до Єрусалима, брати з радістю прийняли нас.
Titafika ku Yerusalemu, abale anatilandira mwachimwemwe.
18 Наступного ж дня Павло разом із нами пішов до Якова. Туди прийшли й всі старійшини.
Mmawa mwake Paulo pamodzi ndi ife tonse tinapita kwa Yakobo, ndipo akulu onse a mpingo anali komweko.
19 Привітавши їх, [Павло] докладно розповів, що зробив Бог серед язичників через його служіння.
Paulo anawalonjera ndi kuwafotokozera mwatsatanetsatane zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.
20 Вони послухали його та прославили Бога. Потім сказали Павлові: «Брате, ти бачиш, як багато тисяч юдеїв увірувало, і всі вони ревно ставляться до Закону.
Atamva zimenezi, iwo anayamika Mulungu. Kenaka anawuza Paulo kuti, “Mʼbale, ukuona kuti pali Ayuda ambirimbiri amene anakhulupirira, ndipo ndi okhulupirika potsatira Malamulo a Mose.
21 Вони чули про тебе, що ти навчаєш юдеїв, які живуть між язичниками, відступити від [Закону] Мойсея, кажучи, щоб вони не обрізали своїх дітей і не дотримувалися звичаїв.
Iwo anawuzidwa kuti iwe umaphunzitsa Ayuda onse amene akukhala pakati pa anthu a mitundu ina kuti asiye kutsatira Mose, kuti asamachite mdulidwe kapena kutsatira miyambo.
22 Що ж тепер [робити]? Вони, безумовно, почують, що ти прийшов.
Nanga pamenepa ife titani? Iwo adzamva ndithu kuti iwe wabwera,
23 Тому зроби, що ми тобі кажемо: серед нас є четверо чоловіків, які пов’язані обітницею.
tsono iwe chita zimene ife tikuwuze. Tili nawo amuna anayi pano amene anachita lumbiro kwa Mulungu.
24 Візьми їх, очисться разом із ними й заплати за них, щоб вони поголили собі голови. Тоді всі дізнаються: те, що сказано про тебе, – неправда, а, навпаки, ти дотримуєшся Закону.
Muwatenge anthu amenewa, ndipo muchite nawo mwambo wowayeretsa ndipo muwalipirire zoti apereke kuti amete tsitsi lawo. Kotero aliyense adzadziwa kuti palibe choonadi pa zimene anamva za inu, koma kuti inu mwini mumakhala moyo womvera Malamulo.
25 А щодо язичників, які увірували, то ми написали їм про наше рішення: вони повинні утримуватися від їжі, яка приносилась ідолам, від крові, від задушених тварин та від статевої розпусти».
Koma kunena za anthu a mitundu ina amene asandulika okhulupirira, ife tinawalembera zimene tinavomerezana zakuti asadye chakudya choperekedwa ku mafano, asadye magazi, asadye nyama yopotola ndiponso asachite zadama.”
26 Наступного дня Павло взяв тих людей і разом із ними виконав вимоги очищення. Потім увійшов у Храм і оголосив, що після закінчення днів очищення за кожного з них буде принесено жертву.
Mmawa mwake Paulo anatenga amuna aja ndipo anachita mwambo wodziyeretsa. Kenaka anapita ku Nyumba ya Mulungu nakadziwitsa ansembe za tsiku limene adzatsiriza nthawi ya kudziyeretsa ndi kuperekera nsembe aliyense wa iwo.
27 Коли ж закінчувалися сім днів, декілька юдеїв з Азії побачили Павла в Храмі та, підбуривши весь народ, схопили його.
Ali pafupi kutsiriza masiku asanu ndi awiriwo, Ayuda ena ochokera ku Asiya anaona Paulo mʼNyumba ya Mulungu. Iwo anawutsa gulu lonse la anthu ndipo anamugwira Paulo,
28 Вони кричали: «Ізраїльтяни, допоможіть! Це чоловік, який повсюди навчає проти [нашого] народу, проти Закону й проти цього місця. До того ж він привів греків у Храм і цим осквернив це святе місце».
akufuwula kuti, “Inu Aisraeli, tithandizeni! Ndi uyu munthu uja amaphunzitsa anthu onse ponseponse kuti azinyoza mtundu wathu ndiponso Malamulo athu ndi malo ano. Kuwonjezera pamenepo, walowetsa Agriki mʼbwalo la Nyumba ino ndipo wadetsa malo opatulika.”
29 Перед тим вони бачили в місті Павла разом із Трохимом з Ефеса й припустили, що Павло ввів його в Храм.
Iwo ananena izi chifukwa anali ataona Trofimo wa ku Efeso ali ndi Paulo mu mzindamo ndipo iwo ankaganiza kuti Paulo anamulowetsa mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
30 Усе місто заворушилося, і зібрався народ. Схопивши Павла, витягнули його з Храму та негайно зачинили двері.
Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata.
31 Вони вже хотіли вбити Павла, але звістка, що весь Єрусалим охоплено заворушенням, дійшла до римського Трибуна.
Pamene anthuwo ankafuna kupha Paulo, nkhaniyi inamveka kwa mkulu wa magulu a asilikali a Aroma kuti mzinda wonse wa Yerusalemu wasokonezeka.
32 Він, узявши воїнів та сотників, відразу побіг до них. Побачивши Трибуна та воїнів, юдеї перестали бити Павла.
Nthawi yomweyo iye anatenga asilikali ndi atsogoleri a magulu a asilikali ndi kuthamangira kumene kunali anthuwo. Anthuwo ataona mkuluyo ndi asilikali ake analeka kumenya Paulo.
33 Трибун, підійшовши, узяв, заарештував Павла й наказав зв’язати його двома ланцюгами. Він спитав народ, хто це такий і що він зробив.
Mkulu wa asilikaliyo anabwera nagwira Paulo, ndipo analamula kuti amangidwe ndi maunyolo awiri. Kenaka iye anafunsa kuti ndi ndani ndipo wachita chiyani.
34 Однак у натовпі одні кричали одне, а інші – інше. Оскільки він через метушню не міг зрозуміти нічого достеменно, то наказав відвести Павла до фортеці.
Ena mʼgulumo anafuwula chinthu china ndi enanso chinanso. Tsono popeza mkulu wa asilikaliyo sanathe kudziwa choonadi chenicheni chifukwa cha phokoso, analamula kuti Paulo atengedwe kupita ku malo a asilikali.
35 Коли він був уже на сходах, воїни були вимушені нести його через тиск натовпу.
Paulo atafika pa makwerero olowera ku malo a asilikaliwo, ananyamulidwa ndi asilikali chifukwa cha ukali wa anthuwo.
36 Багато народу йшло за ним, вигукуючи: «Смерть йому!»
Gulu la anthu limene linamutsatira linapitiriza kufuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi!”
37 Перед тим, як Павла мали ввести до фортеці, він спитав Трибуна: ―Чи можна мені щось тобі сказати? Той відповів: ―Ти знаєш грецьку?
Asilikali ali pafupi kulowa naye ku malo awo, iye anapempha mkulu wa asilikaliyo kuti, “Kodi mungandilole ndiyankhulepo?” Mkulu wa asilikaliyo anafunsa kuti, “Kodi umayankhula Chigriki?
38 Чи ти не той єгиптянин, який нещодавно підняв бунт і повів за собою в пустелю чотири тисячі розбійників?
Kodi sindiwe Mwigupto uja amene masiku apitawo unayambitsa kuwukira ndi kutsogolera anthu 4,000 owukira aja nʼkupita nawo ku chipululu?”
39 Павло відповів: ―Я юдей з Тарса в Килікії, громадянин відомого міста. Прошу тебе, дозволь мені звернутися до народу.
Paulo anayankha kuti, “Ine ndine Myuda, wa ku Tarisisi ku Kilikiya. Sindine nzika ya mzinda wamba. Chonde loleni ndiyankhule nawo anthuwa.”
40 Коли той дозволив, Павло, стоячи на сходах, дав народові знак рукою. Коли настала тиша, він заговорив єврейською мовою, кажучи:
Ataloledwa ndi mkulu wa asilikaliyo, Paulo anayimirira pa makwereropo nakweza dzanja lake kwa gulu la anthuwo. Onse atakhala chete, iye anayankhula nawo mʼChihebri.