< Zekeriya 1 >
1 Darius'un krallığının ikinci yılının sekizinci ayında RAB İddo oğlu Berekya oğlu Peygamber Zekeriya aracılığıyla şöyle seslendi:
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 “RAB atalarınıza çok öfkelendi.
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 Bu nedenle halka de ki, Her Şeye Egemen RAB böyle diyor: ‘Her Şeye Egemen RAB, bana dönün’ diyor; ‘Ben de size dönerim diyor Her Şeye Egemen RAB.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Atalarınız gibi davranmayın! Önceki peygamberler, Her Şeye Egemen RAB kötü yollarınızdan ve kötü uygulamalarınızdan dönün diyor, diyerek onları uyardılar. Ne var ki, onlar dinlemediler, bana aldırış etmediler. Böyle diyor RAB.
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 Hani atalarınız nerede? Peygamberler de sonsuza kadar mı yaşar?
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 Peygamber kullarıma buyurduğum sözler ve kurallar atalarınıza ulaşmadı mı?’ “Onlar da dönüp, ‘Her Şeye Egemen RAB yollarımıza ve uygulamalarımıza bakarak bizim için ne düşündüyse aynen yaptı’ dediler.”
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 Darius'un krallığının ikinci yılında, on birinci ay olan Şevat ayının yirmi dördüncü günü RAB İddo oğlu Berekya oğlu Peygamber Zekeriya'ya görümlerle seslendi.
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 Gece vadideki mersin ağaçlarının arasında kızıl ata binmiş bir adam gördüm. Arkasında kızıl, kula ve beyaz atlar vardı.
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 “Efendim, bunlar ne?” diye sordum. Benimle konuşan melek, “Bunların ne olduğunu sana göstereceğim” diye yanıtladı.
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 Mersin ağaçları arasında duran adam da, “Bunlar dünyayı dolaşmak için RAB'bin gönderdikleridir” diye açıkladı.
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 Mersin ağaçları arasında duran RAB'bin meleğine, “Dünyayı dolaştık” dediler, “İşte bütün dünya esenlik ve güvenlik içinde!”
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 Bunun üzerine RAB'bin meleği, “Ey Her Şeye Egemen RAB, yetmiş yıldır öfkelendiğin Yeruşalim'den ve Yahuda kentlerinden sevecenliğini ne zamana dek esirgeyeceksin?” dedi.
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 RAB benimle konuşan meleği tatlı, avutucu sözlerle yanıtladı.
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 Bunun üzerine benimle konuşan melek, “Şunu duyur!” dedi, “Her Şeye Egemen RAB, ‘Yeruşalim ve Siyon için büyük kıskançlık duyuyorum’ diyor,
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 ‘Tasasız uluslara ise çok öfkeliyim; çünkü ben biraz öfkelenmiştim, onlarsa kötülüğe kötülük kattılar.’
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 “Onun için RAB, ‘Yeruşalim'e sevecenlikle döneceğim’ diyor, ‘Tapınağım orada yeniden kurulacak ve Yeruşalim üzerine ölçü ipi çekilecek!’ Böyle diyor Her Şeye Egemen RAB.
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 “Şunu da duyur: Her Şeye Egemen RAB, ‘Kentlerim yine bollukla dolup taşacak’ diyor, ‘Ben RAB, Siyon'u yine avutacağım, Yeruşalim'i yine seçeceğim.’”
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 Sonra gözlerimi kaldırıp baktım, dört boynuz vardı.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 Benimle konuşan meleğe, “Bunlar ne?” diye sordum. Melek, “Bunlar Yahuda, İsrail ve Yeruşalim halkını dağıtmış olan boynuzlardır” diye karşılık verdi.
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 Sonra RAB bana dört usta gösterdi.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 “Bunlar ne yapmaya geliyor?” diye sordum. Melek, “Şu boynuzlar Yahuda halkını öyle dağıttı ki, kimse başını kaldıramadı” dedi, “Bu ustalar da Yahuda halkını dağıtmak için boynuz kaldıran ulusları yıldırıp boynuzlarını yere çalmaya geldiler.”
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”