< Habakkuk 3 >

1 Peygamber Habakkuk'un Duası - Şigyonot Makamında
Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
2 Ya RAB, ününü duydum ve yaptıklarının karşısında ürperdim. Günümüzde de aynı şeyleri yap, ya RAB, Şimdi herkes bilsin neler yapabildiğini. Öfkeliyken merhametini anımsa!
Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
3 Tanrı Teman'dan, Kutsal Tanrı Paran Dağı'ndan geldi. (Sela) Görkemi kapladı gökleri, O'na sunulan övgüler dünyayı doldurdu.
Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
4 Güneş gibi parıldıyor, Elleri ışık saçıyor. Gücünün gizi ellerinde.
Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
5 Yayılıyor salgın hastalıklar önüsıra, Ardısıra da ölümcül hastalıklar.
Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
6 Duruşuyla dünyayı sarstı, Titretti ulusları bakışıyla, Yaşlı dağlar darmadağın oldu, Dünya kurulalı beri var olan tepeler O'na baş eğdi. Tanrı'nın yolları değişmezdir.
Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
7 Kuşan çadırlarını çaresizlik içinde gördüm, Midyan konutları korkudan titriyordu.
Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
8 Ya RAB, nehirlere mi öfkelendin? Gazabın ırmaklara mı? Yoksa denize mi kızdın da, Atlarına, yenilmez savaş arabalarına bindin?
Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
9 Gerdin yayını, Okların içtiğin antlardır. (Sela) Yeryüzünü akarsularla yardın.
Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
10 Sarsıldı dağlar seni görünce, Seller her yanı süpürüp geçti. Engin denizler gürledi, dalgalar yükseldi.
mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
11 Uçuşan oklarının pırıltısından, Parlayan mızrağının ışıltısından, Yerlerinde durakaldı güneş ve ay.
Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
12 Gazap içinde ilerledin yeryüzünde, Ulusları öfkeyle çiğneyip ezdin.
Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
13 Kendi halkını, seçtiğin ulusu kurtarmaya geldin. Kötü soyun başını ezdin, Soydun onu tepeden tırnağa. (Sela)
Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
14 Başını kendi mızrağıyla deldin. Askerleri fırtına gibi gelmişti bizi dağıtmaya, Saklanan düşkünleri yok etmiş gibi seviniyorlardı.
Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
15 Sense atlarınla çiğneyip geçtin büyük denizleri, Sularını köpürterek...
Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
16 Sesini duyunca yüreğim hopladı, Seğirdi dudaklarım, Kemiklerim eridi sanki, Çözüldü dizlerimin bağı. Ama bize saldıran halkın felakete uğrayacağı günü Sabırla bekleyeceğim.
Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
17 Tomurcuklanmasa incir ağaçları, Asmalar üzüm vermese, Boşa gitse de zeytine verilen emek, Tarlalar ürün vermese de, Boşalsa da davar ağılları, Sığır kalmasa da ahırlarda,
Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
18 Ben yine RAB sayesinde sevineceğim, Kurtuluşumun Tanrısı sayesinde sevinçten coşacağım.
komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
19 Egemen RAB gücümdür benim. Ayaklarıma geyik ayağının çevikliğini verir. Aşırtır beni yükseklerden. Müzik şefi için: Telli sazlar eşliğinde söylenecek.
Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

< Habakkuk 3 >