< Mezmurlar 90 >
1 Tanrı adamı Musa'nın duası Ya Rab, barınak oldun bize Kuşaklar boyunca.
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Dağlar var olmadan, Daha evreni ve dünyayı yaratmadan, Öncesizlikten sonsuzluğa dek Tanrı sensin.
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 İnsanı toprağa döndürürsün, “Ey insanoğulları, toprağa dönün!” diyerek.
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 Çünkü senin gözünde bin yıl Geçmiş bir gün, dün gibi, Bir gece nöbeti gibidir.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 İnsanları bir düş gibi siler, süpürürsün, Sabah biten ot misali:
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 Sabah filizlenir, büyür, Akşam solar, kurur.
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 Eriyip bitiyoruz senin öfkenden, Kızgınlığından dehşete düşüyoruz.
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 Suçlarımızı önüne, Gizli günahlarımızı yüzünün ışığına çıkardın.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 Gazabından kısalıyor günlerimiz, Bir soluk gibi tükeniyor yıllarımız.
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 Ömrümüz yetmiş yıl sürüyor, Bilemedin seksen, o da sağlıklıysak; En güzel yıllar da zahmetle, kederle geçiyor, Çabucak bitiyor, uçup gidiyoruz.
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 Kim bilir gazabının gücünü? Çünkü öfken sana duyulan korku kadar güçlüdür.
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 Bu yüzden günlerimizi saymayı bize öğret ki, Bilgelik kazanalım.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Vazgeç, ya RAB! Öfken ne zamana dek sürecek? Acı kullarına!
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Sabah bizi sevginle doyur, Ömrümüz boyunca sevinçle haykıralım.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Kaç gün bizi sıkıntıya soktunsa, Kaç yıl çile çektirdinse, O kadar sevindir bizi.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Yaptıkların kullarına, Görkemin onların çocuklarına görünsün.
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 Tanrımız Rab bizden hoşnut kalsın. Ellerimizin emeğini boşa çıkarma. Evet, ellerimizin emeğini boşa çıkarma.
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.