< Mezmurlar 75 >

1 Müzik şefi için - “Yok Etme” makamında - Asaf'ın mezmuru - İlahi Sana şükrederiz, ey Tanrı, Şükrederiz, çünkü sen yakınsın, Harikaların bunu gösterir.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 “Belirlediğim zaman gelince, Doğrulukla yargılayacağım” diyor Tanrı,
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 “Yeryüzü altüst olunca üzerindekilerle, Ben pekiştireceğim onun direklerini. (Sela)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 Övünenlere, ‘Övünmeyin artık!’ dedim; Kötülere, ‘Kaldırmayın başınızı!
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Kaldırmayın başınızı! Tepeden konuşmayın!’”
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 Çünkü ne doğudan, ne batıdan, Ne de çöldeki dağlardan doğar yargı.
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 Yargıç ancak Tanrı'dır, Birini alçaltır, birini yükseltir.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 RAB elinde dolu bir kâse tutuyor, Köpüklü, baharat karıştırılmış şarap döküyor; Yeryüzünün bütün kötüleri Tortusuna dek yalayıp onu içiyor.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Bense sürekli duyuracağım bunu, Yakup'un Tanrısı'nı ilahilerle öveceğim:
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 “Kıracağım kötülerin bütün gücünü, Doğruların gücüyse yükseltilecek.”
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

< Mezmurlar 75 >