< Süleyman'In Özdeyişleri 1 >

1 Davut oğlu İsrail Kralı Süleyman'ın özdeyişleri:
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Bu özdeyişler, bilgeliğe ve terbiyeye ulaşmak, Akıllıca sözleri anlamak,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 Başarıya götüren terbiyeyi edinip Doğru, haklı ve adil olanı yapmak,
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Saf kişiyi ihtiyatlı, Genç adamı bilgili ve sağgörülü kılmak içindir.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Özdeyişlerle benzetmeleri, Bilgelerin sözleriyle bilmecelerini anlamak için Bilge kişi dinlesin ve kavrayışını artırsın, Akıllı kişi yaşam hüneri kazansın.
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 RAB korkusudur bilginin temeli. Ahmaklarsa bilgeliği ve terbiyeyi küçümser.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Oğlum, babanın uyarılarına kulak ver, Annenin öğrettiklerinden ayrılma.
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Çünkü bunlar başın için sevimli bir çelenk, Boynun için gerdanlık olacaktır.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Oğlum, seni ayartmaya çalışan günahkârlara teslim olma.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Şöyle diyebilirler: “Bizimle gel, Adam öldürmek için pusuya yatalım, Zevk uğruna masum kişileri tuzağa düşürelim.
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Onları ölüler diyarı gibi diri diri, Ölüm çukuruna inenler gibi Bütünüyle yutalım. (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Bir sürü değerli mal ele geçirir, Evlerimizi ganimetle doldururuz.
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Gel, sen de bize katıl, Tek bir kesemiz olacak.”
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Oğlum, böyleleriyle gitme, Onların tuttuğu yoldan uzak dur.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Çünkü ayakları kötülüğe koşar, Çekinmeden kan dökerler.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Kuşların gözü önünde ağ sermek boşunadır.
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Başkasına pusu kuran kendi kurduğu pusuya düşer. Yalnız kendi canıdır tuzağa düşürdüğü.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Haksız kazanca düşkün olanların sonu böyledir. Bu düşkünlük onları canlarından eder.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Bilgelik dışarıda yüksek sesle haykırıyor, Meydanlarda sesleniyor.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Kalabalık sokak başlarında bağırıyor, Kentin giriş kapılarında sözlerini duyuruyor:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 “Ey budalalar, budalalığı ne zamana dek seveceksiniz? Alaycılar ne zamana dek alay etmekten zevk alacak? Akılsızlar ne zamana dek bilgiden nefret edecek?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Uyardığımda yola gelin, o zaman size yüreğimi açar, Sözlerimi anlamanıza yardım ederim.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Ama sizi çağırdığım zaman beni reddettiniz. Elimi uzattım, umursayan olmadı.
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Duymazlıktan geldiniz bütün öğütlerimi, Uyarılarımı duymak istemediniz.
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Bu yüzden ben de felaketinize sevineceğim. Belaya uğradığınızda, Bela üzerinize bir fırtına gibi geldiğinde, Bir kasırga gibi geldiğinde felaketiniz, Sıkıntıya, kaygıya düştüğünüzde, Sizinle alay edeceğim.
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 O zaman beni çağıracaksınız, Ama yanıtlamayacağım. Var gücünüzle arayacaksınız beni, Ama bulamayacaksınız.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Çünkü bilgiden nefret ettiniz. RAB'den korkmayı reddettiniz.
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Öğütlerimi istemediniz, Uyarılarımın tümünü küçümsediniz.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Bu nedenle tuttuğunuz yolun meyvesini yiyeceksiniz, Kendi düzenbazlığınıza doyacaksınız.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Bön adamlar dönekliklerinin kurbanı olacak. Akılsızlar kaygısızlıklarının içinde yok olup gidecek.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Ama beni dinleyen güvenlik içinde yaşayacak, Kötülükten korkmayacak, huzur bulacak.”
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Süleyman'In Özdeyişleri 1 >