< Yeşaya 21 >

1 Deniz kıyısındaki çölle ilgili bildiri: Negev'den fırtınalar nasıl üst üste gelirse, Çölden, korkunç ülkeden bir istilacı öyle geliyor.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 Korkunç bir görüm gördüm: Hain hainlik etmede, Harap eden harap etmede. Ey Elam, saldır! Ey Meday, onu kuşat! Onun neden olduğu iniltileri sona erdireceğim.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 Gördüklerimden ötürü belime ağrı saplandı, Doğuran kadının ağrıları gibi ağrılar tuttu beni. Duyduklarımdan sarsıldım, Gördüklerimden dehşete düştüm.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 Şaşkınım, titremeler sardı beni. Özlediğim alaca karanlık bana korku veriyor artık.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 Gördüğüm görümde sofrayı hazırlıyor, Halıları seriyor, yiyip içiyorlar. Kalkın, ey önderler, kalkanları yağlayın!
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Rab bana dedi ki, “Git, bir gözcü dik, gördüğünü bildirsin.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Savaş arabalarının, Atlara, eşeklere, develere binmiş insanların Çifter çifter geldiğini görünce dikkat kesilsin.”
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Gözcü, “Ey efendim, Her gün aralıksız gözcü kulesinde duruyor, Her gece yerimde nöbet tutuyorum” diye bağırdı,
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 “Bak, savaş arabalarıyla atlılar Çifter çifter geliyor!” Sonra, “Yıkıldı, Babil yıkıldı!” diye haber verdi, “Taptıkları bütün putlar yere çalınıp parçalandı!”
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 Ey halkım, harman yerinde Buğday gibi dövülmüş olan halkım! Her Şeye Egemen RAB'den, İsrail'in Tanrısı'ndan duyduklarımı Size bildirdim.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 Duma ile ilgili bildiri: Biri Seir'den bana sesleniyor: “Ey gözcü, geceden geriye ne kaldı? Geceden geriye ne kaldı?”
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 Yanıtım şöyle: “Sabah olmak üzere, Ama yine gece olacak. Soracaksanız sorun, yine gelin.”
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 Arabistan'la ilgili bildiri: Arabistan çalılıklarında geceleyeceksiniz, Ey Dedan kervanları!
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 Ey Tema'da oturanlar, Su getirin, susamışları karşılayın, Kaçıp kurtulana ekmek verin.
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 Çünkü onlar kılıçtan, yalın kılıçtan, Gerilmiş yaydan, çetin çarpışmalardan kaçtılar.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Rab bana şöyle dedi: “Kedar'ın bütün övüncü tam bir yıl sonra sona erecek.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 Okçulardan, Kedar savaşçılarından pek az sağ kalan olacak.” Bunu söyleyen, İsrail'in Tanrısı RAB'dir.
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.

< Yeşaya 21 >