< 1 Tarihler 11 >

1 İsrailliler'in tümü Hevron'da bulunan Davut'a gelip şöyle dediler: “Biz senin etin, kemiğiniz.
Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Davide ku Hebroni ndipo anati, “Ife ndife abale anu.
2 Geçmişte Saul kralımızken, savaşta İsrail'e komuta eden sendin. Tanrın RAB sana, ‘Halkım İsrail'i sen güdecek, onlara sen önder olacaksın’ diye söz verdi.”
Kale lija, ngakhale pamene Sauli anali mfumu, inu ndinu amene munkatsogolera Aisraeli pa nkhondo zawo. Ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwuzani kuti, ‘Iwe udzaweta anthu anga Aisraeli, ndipo udzakhala mfumu yawo.’”
3 İsrail'in bütün ileri gelenleri Hevron'a, Kral Davut'un yanına gelince, Davut RAB'bin önünde orada onlarla bir antlaşma yaptı. Onlar da RAB'bin Samuel aracılığıyla söylediği söz uyarınca, Davut'u İsrail Kralı olarak meshettiler.
Akuluakulu onse a Israeli atafika kwa Mfumu Davide ku Hebroni, iye anachita nawo pangano pamaso pa Yehova, ndipo anamudzoza Davide kukhala mfumu ya Israeli, monga momwe Yehova analonjezera kudzera mwa Samueli.
4 Kral Davut'la İsrailliler Yevus diye bilinen Yeruşalim'e saldırmak için yola çıktılar. Orada yaşayan Yevuslular
Davide ndi Aisraeli onse anapita ku Yerusalemu (ku Yebusi). Ayebusi amene ankakhala kumeneko
5 Davut'a, “Sen buraya giremezsin” dediler. Ne var ki, Davut Siyon Kalesi'ni, Davut Kenti'ni ele geçirdi.
anamuwuza Davide kuti, “Simulowa muno.” Komabe Davide analanda linga la Ziyoni, limene ndi mzinda wa Davide.
6 Davut, “Yevuslular'a ilk saldıran kişi komutan ve önder olacak” demişti. İlk saldırıyı Seruya oğlu Yoav yaptı, böylece ordu komutanı oldu.
Davide anali atanena kuti “Aliyense amene adzatsogolere kukathira nkhondo Ayebusi adzakhala mkulu wa asilikali.” Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anayamba kupita, motero anakhala mkulu wa asilikali.
7 Bundan sonra Davut kalede oturmaya başladı. Bunun için oraya “Davut Kenti” adı verildi.
Tsono Davide anakhazikika mu lingamo, ndipo mzindawu anawutcha Mzinda wa Davide.
8 Çevredeki bölgeyi, Millo'dan çevre surlara kadar uzanan kesimi inşa etti. Yoav da kentin geri kalan bölümünü onardı.
Iye anamanga malo onse ozungulira, kuyambira ku matsitso ozungulira khoma. Ndipo Yowabu anakonzanso mbali ina ya mzindawu.
9 Davut giderek güçleniyordu. Çünkü Her Şeye Egemen RAB onunlaydı.
Ndipo mphamvu za Davide zinkakulirakulira chifukwa anali ndi Yehova Wamphamvuzonse.
10 RAB'bin İsrail'e verdiği söz uyarınca Davut'un yiğit askerlerinin komutanları İsrail halkıyla birlikte Davut'u kral yaptılar ve krallığının güçlenmesi için onu desteklediler.
Awa ndiye anali atsogoleri amphamvu a Davide. Iwo pamodzi ndi Aisraeli onse, anathandiza kulimbikitsa ufumu wake kuti ukwanire madera onse, monga momwe Yehova analonjezera.
11 Bunların adları şöyledir: Üçler'in önderi Hakmonlu Yaşovam, mızrağını üç yüz kişiye karşı kaldırıp bir saldırıda hepsini öldürdü.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yasobeamu Mhakimoni anali mkulu wa atsogoleri. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300 nthawi imodzi.
12 İkincisi, üç yiğitlerden biri olan Ahohlu Dodo oğlu Elazar.
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi, mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu.
13 Filistliler savaş için Pas-Dammim'de toplandıklarında Elazar Davut'un yanındaydı. Orada bir arpa tarlası vardı. İsrailliler Filistliler'in önünden kaçmıştı.
Iye anali ndi Davide ku Pasi-Damimu pamene Afilisti anasonkhana kudzachita nkhondo. Ankhondo anathawa Afilistiwo pamalo pamene panali munda wodzaza ndi barele.
14 Ama Elazar'la Davut tarlanın ortasında durup orayı savunmuş, Filistliler'i öldürmüşlerdi. RAB onlara büyük bir zafer sağlamıştı.
Koma awiriwo anayima pakati pa mundawo. Iwo anawuteteza, nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
15 Otuzlar'dan üçü Davut'un yanına, Adullam Mağarası'ndaki kayaya gittiler. Bir Filist birliği Refaim Vadisi'nde ordugah kurmuştu.
Atatu mwa atsogoleri makumi atatu aja anabwera kwa Davide ku thanthwe ku phanga la Adulamu pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
16 Bu sırada Davut hisarda, başka bir Filist birliğiyse Beytlehem'deydi.
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
17 Davut özlemle, “Keşke biri Beytlehem'de kapının yanındaki kuyudan bana su getirse!” dedi.
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
18 Bu Üçler Filist ordugahının ortasından geçerek Beytlehem'de kapının yanındaki kuyudan su çekip Davut'a getirdiler. Ama Davut içmek istemedi; suyu yere dökerek RAB'be sundu.
Choncho anthu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
19 “Ey Tanrım, bunu yapmak benden uzak olsun!” dedi, “Canlarını tehlikeye atıp giden bu üç kişinin kanını mı içeyim?” Canlarını tehlikeye atarak suyu getirdikleri için Davut içmek istemedi. Bu üç kişinin yiğitliği işte böyleydi.
Iye anati, “Inu Mulungu, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi ndimwe magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Chifukwa iwo anayika miyoyo yawo pachiswe kuti abweretse madziwo, Davide sanamwe. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
20 Yoav'ın kardeşi Avişay Üçler'in önderiydi. Mızrağını kaldırıp üç yüz kişiyi öldürdü. Bu yüzden Üçler kadar ünlendi.
Abisai mʼbale wa Yowabu ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300. Choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
21 Üçler'in en saygın kişisiydi ve onların önderi oldu. Ama Üçler'den sayılmadı.
Iye analandira ulemu woposa atatuwo. Kotero anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti iyeyo sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
22 Yehoyada oğlu Kavseelli Benaya yürekli bir savaşçıydı. Büyük işler başardı. Aslan yürekli iki Moavlı'yı öldürdü. Ayrıca karlı bir gün çukura inip bir aslan öldürdü.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
23 Beş arşın boyunda iri yarı bir Mısırlı'yı da öldürdü. Mısırlı'nın elinde dokumacı sırığı gibi bir mızrak vardı. Benaya sopayla onun üzerine yürüdü. Mızrağı elinden kaptığı gibi onu kendi mızrağıyla öldürdü.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto amene anali wotalika mamita awiri ndi theka. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo wofanana ndi ndodo yowombera nsalu mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
24 Yehoyada oğlu Benaya'nın yaptıkları bunlardır. Bu sayede o da üç yiğitler kadar ünlendi.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
25 Benaya Otuzlar arasında saygın bir yer edindiyse de, Üçler'den sayılmadı. Davut onu muhafız birliği komutanlığına atadı.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
26 Öteki yiğitler şunlardır: Yoav'ın kardeşi Asahel, Beytlehemli Dodo oğlu Elhanan,
Ankhondo amphamvuwa anali: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
27 Harorlu Şammot, Pelonlu Heles,
Samoti Mharori, Helezi Mpeloni.
28 Tekoalı İkkeş oğlu İra, Anatotlu Aviezer,
Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa, Abiezeri wa ku Anatoti,
29 Huşalı Sibbekay, Ahohlu İlay,
Sibekai Mhusati, Ilai Mwahohi,
30 Netofalı Mahray ve Baana oğlu Helet,
Maharai Mnetofa, Heledi mwana wa Baana Mnetofa,
31 Benyaminoğulları'ndan Givalı Rivay oğlu İttay, Piratonlu Benaya,
Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini, Benaya Mpiratoni,
32 Gaaş vadilerinden Huray, Arvalı Aviel,
Hurai wa ku zigwa za Gaasi, Abieli Mwaribati,
33 Baharumlu Azmavet, Şaalbonlu Elyahba,
Azimaveti Mbaharumi, Eliyahiba Msaaliboni,
34 Gizonlu Haşem'in oğulları, Hararlı Şage oğlu Yonatan,
ana a Hasemu Mgizoni, Yonatani mwana wa Sage Mharari,
35 Hararlı Sakâr oğlu Ahiam, Ur oğlu Elifal,
Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,
36 Mekeralı Hefer, Pelonlu Ahiya,
Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,
37 Karmelli Hesro, Ezbay oğlu Naaray,
Heziro wa ku Karimeli Naara mwana wa Ezibai,
38 Natan'ın kardeşi Yoel, Hacer oğlu Mivhar,
Yoweli mʼbale wa Natani, Mibihari mwana wa Hagiri,
39 Ammonlu Selek, Seruya oğlu Yoav'ın silah taşıyıcısı Berotlu Nahray,
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya.
40 Yattirli İra ve Garev,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
41 Hititli Uriya, Ahlay oğlu Zavat,
Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Ahilai,
42 Rubenliler'in önderi Rubenli Şiza oğlu Adina ve ona eşlik eden otuz kişi,
Adina mwana wa Siza Mrubeni, amene anali mtsogoleri wa Arubeni ndi anthu makumi atatu pamodzi naye,
43 Maaka oğlu Hanan, Mitanlı Yoşafat,
Hanani mwana wa Maaka, Yehosafati Mmitini,
44 Aşteralı Uzziya, Aroerli Hotam'ın oğulları Şama ve Yeiel,
Uziya Mwasiterati, Sama ndi Yeiyeli ana a Hotamu Mwaroeri,
45 Şimri oğlu Yediael ve kardeşi Tisli Yoha,
Yediaeli mwana wa Simiri, ndi Yoha Mtizi mʼbale wake,
46 Mahavlı Eliel, Elnaam'ın oğulları Yerivay ve Yoşavya, Moavlı Yitma,
Elieli Mhavati, Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, Itima Mmowabu,
47 Eliel, Ovet, Mesovalı Yaasiel.
Elieli, Obedi ndi Yaasieli Mmeobai.

< 1 Tarihler 11 >