< 1 Tarihler 10 >
1 Filistliler İsrailliler'le savaşa tutuştu. İsrailliler Filistliler'in önünden kaçtı. Birçoğu Gilboa Dağı'nda ölüp yere serildi.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 Filistliler Saul'la oğullarının ardına düştüler. Saul'un oğulları Yonatan'ı, Avinadav'ı ve Malkişua'yı yakalayıp öldürdüler.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 Saul'un çevresinde savaş kızıştı. Derken Saul Filistli okçular tarafından vuruldu ve yaralandı.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 Saul silahını taşıyan adama, “Kılıcını çek de bana sapla” dedi, “Yoksa bu sünnetsizler gelip benimle alay edecekler.” Ama silah taşıyıcısı büyük bir korkuya kapılarak bunu yapmak istemedi. Bunun üzerine Saul kılıcını çekip kendini üzerine attı.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 Saul'un öldüğünü görünce, silah taşıyıcısı da kendini kılıcının üzerine atıp öldü.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa.
6 Böylece Saul, üç oğlu ve bütün ev halkı birlikte öldüler.
Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 Vadide oturan İsrailliler, İsrail ordusunun kaçtığını, Saul'la oğullarının öldüğünü anlayınca, kentlerini terk edip kaçmaya başladılar. Filistliler gelip bu kentlere yerleştiler.
Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 Ertesi gün Filistliler, öldürülenleri soymak için geldiklerinde, Saul'la oğullarının Gilboa Dağı'nda öldüğünü gördüler.
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa.
9 Saul'u soyduktan sonra başını kesip silahlarını aldılar. Sonra bu iyi haberi putlarına ve halka duyurmaları için Filist ülkesinin her yanına ulaklar gönderdiler.
Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 Saul'un silahlarını ilahlarının tapınağına koyup başını Dagon Tapınağı'na çaktılar.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 Yaveş-Gilat halkı Filistliler'in Saul'a yaptıklarını duydu.
Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 Bütün yiğitler gidip Saul'la oğullarının cesetlerini Yaveş'e getirdiler. Sonra kemiklerini Yaveş'teki yabanıl fıstık ağacının altına gömdüler ve yedi gün oruç tuttular.
anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 Saul RAB'be ihanet ettiği için öldü. RAB'bin sözünü yerine getirmedi. Yol göstermesi için RAB'be danışacağına bir cinciye danıştı. Bu yüzden RAB onu öldürdü. Krallığını da İşay oğlu Davut'a devretti.
Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.