< Psaltaren 18 >
1 En Psalm, till att föresjunga, Davids, Herrans tjenares; hvilken denna visos ord talade till Herran, på den tid Herren honom hulpit hade ifrå hans fiendars hand, och ifrå Sauls hand; Och sade: Hjerteliga, kär hafver jag dig, Herre, min starkhet;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
2 Herre, min klippa, min borg, min förlossare; min Gud, min tröst, den jag mig vid håller; min sköld, och min salighets horn, och mitt beskydd.
Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
3 Jag vill lofva och åkalla Herren; så blifver jag ifrå mina ovänner förlöst.
Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
4 Ty dödsens band hafva, omfattat mig, och Belials bäcker förskräckt mig.
Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
5 Helvetes band hafva omfattat mig, och dödsens snaror öfverfallit mig. (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
6 När jag är i ångest, så åkallar jag Herran, och ropar till min Gud; så hörer han mina röst af sitt tempel, och mitt rop kommer för honom till hans öron.
Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
7 Jorden bäfvade och gaf sig, och bergens grundvalar rördes och bäfvade, då han vred var.
Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
8 Damb gick upp af hans näso, och förtärande eld af hans mun; så att det ljungade deraf.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
9 Han böjde himmelen, och for neder, och mörker var under hans fötter.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
10 Och han för uppå Cherub, och flög; han sväfde på vädrens vingar.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
11 Hans tjäll omkring honom var mörker, och svart tjockt moln, der han inne fördold var.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
12 Af skenet för honom delte sig skyn, med hagel och ljungande.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
13 Och Herren dundrade i himmelen; och den Högste lät sitt dunder ut, med hagel och ljungande.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
14 Han sköt sina skott, och förströdde dem; han lät fast ljunga, och förskräckte dem.
Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
15 Der såg man vattuådrorna; och jordenes grund vardt blottad, Herre, af ditt straff, af dine näsos anda och blåst.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
16 Han sände utaf höjdene, och hemtade mig; och drog mig utu stor vatten.
Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
17 Han halp mig ifrå mina starka fiendar; ifrå mina hatare, som mig för mägtige voro;
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
18 De mig öfverföllo i mins motgångs tid; och Herren vardt min tröst.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
19 Och han förde mig ut på rymdena; han tog mig derut; ty han hade lust till mig.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
20 Herren gör väl emot mig, efter mina rättfärdighet; han vedergäller mig efter mina händers renhet.
Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
21 Ty jag håller Herrans vägar, och är icke ogudaktig emot min Gud.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
22 Ty alla hans rätter hafver jag för ögon, och hans bud kastar jag icke ifrå mig.
Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
23 Men jag; är utan vank för honom, och bevarar mig för min synd.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
24 Derföre vedergäller mig Herren, efter mina rättfärdighet; efter mina händers renhet för hans ögon.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
25 Med de heliga äst du helig; och med de fromma, äst du from;
Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
26 Och med de rena äst du ren; och vid de afvoga ställer du dig afvog.
kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
27 Ty du hjelper det elända folket, och de höga ögon förnedrar du.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
28 Ty du upplyser mina lykto; Herren, min Gud, gör mitt mörker ljust.
Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
29 Ty med dig kan jag nederlägga krigsfolk, och med minom Gud öfver muren springa.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
30 Guds vägar äro utan vank; Herrans tal äro genomluttrad; han är en sköld allom dem som trösta uppå honom.
Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
31 Ty ho är en Gud, utan Herren; eller en starker, utan vår Gud?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
32 Gud omgjordar mig med kraft, och gör mina vägar utan vank.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
33 Han gör mina fötter lika som hjortars, och sätter mig på mina höjder.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
34 Han lärer mina hand strida, och min arm spänna kopparbågan.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
35 Och du gifver mig dins salighets sköld, och din högra hand stärker mig; och när du förnedrar mig, gör du mig storan.
Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
36 Du gör under mig rum till att gå, att mina fötter icke skola slinta.
Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
37 Jag vill jaga efter mina fiendar, och gripa dem; och intet omvända, tilldess jag hafver nederlagt dem.
Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
38 Jag skall slå dem, och de skola icke kunna mig emotstå; de måste falla under mina fötter.
Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
39 Du kan rusta mig med starkhet till strid; du kan kasta dem under mig, som sig emot mig sätta.
Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
40 Du gifver mig mina fiendar på flyktena, att jag må förstöra mina hatare.
Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
41 De ropa, men der är ingen hjelpare: till Herran, men han svarar dem intet.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
42 Jag skall sönderstöta dem som stoft för vädret; jag skall bortkasta dem såsom träck på gatomen.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
43 Du hjelper mig ifrå det trätosamma folket, och gör mig till ett hufvud ibland Hedningarna; ett folk, som jag intet kände, tjenar mig.
Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
44 Det hörer mig med hörsam öron; men de främmande barn förneka mig.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
45 De främmande barn försmäkta, och brytas i sina bojor.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
46 Herren lefver, och lofvad vare min tröst; och mins salighets Gud varde upphöjd.
Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
47 Gud, som mig hämnd gifver, och tvingar folken under mig;
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
48 Den mig hjelper ifrå mina fiendar, och upphöjer mig ifrå dem, som sätta sig emot mig; du hjelper mig ifrå de vrånga.
amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
49 Derföre vill jag tacka dig, Herre, ibland Hedningarna, och lofsjunga dino Namne;
Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
50 Den sinom Konung stor salighet bevisar, och gör sinom smorda godt; David, och hans säd evinnerliga.
Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.