< Nehemja 5 >

1 Och sig upphof ett stort rop af folket, och deras hustrur, emot sina bröder Judarna.
Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
2 Och voro somlige, som sade: Våre söner och döttrar äro allt för månge; låt oss taga säd, och äta, att vi måge lefva.
Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
3 Och somlige sade: Låt oss utsätta våra åkrar, vingårdar och hus, och taga säd i denna hårda tiden.
Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
4 Somlige sade: Låt oss låna penningar på ränto till Konungen, på våra åkrar och vingårdar.
Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
5 Ty våra bröders kropp är såsom vår kropp, och deras barn såsom vår barn; eljest gifve vi våra söner och döttrar i träldom, och äre allaredo våra döttrar somliga undergifna, och ingen magt är i våra händer; komma också våra åkrar och vingårdar androm tillhanda.
Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
6 Då jag nu deras rop och dessa orden hörde, vardt jag ganska vred.
Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
7 Och mitt hjerta fick till råds, att jag straffade rådherrarna och öfverstarna, och sade till dem: Viljen I drifva ocker, den ene på den andra? Och jag hade tillhopa emot dem en stor församling;
Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
8 Och sade till dem: Vi hafve igenköpt våra bröder Judarna, som Hedningomen sålde voro, efter våra förmågo; och I viljen också sälja edra bröder, de vi till oss köpt hafve? Då tego de, och funno intet till att svara.
ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
9 Och jag sade: Det är icke godt, som I gören. Skullen I icke vandra i Gudsfruktan, för Hedningarnas försmädelses skull, våra fiendars?
Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
10 Jag och mine bröder, och mine tjenare, hafvom ock fått dem penningar och säd; men ockret vilje vi låta blifva tillbaka.
Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
11 Så får dem nu i denna dag igen sina åkrar, vingårdar, oljogårdar och hus, och hundradedelen af penningomen för säd, vin och oljo, som I på dem ockrat hafven.
Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
12 Då sade de: Vi vilje få dem det igen, och vilje intet äska af dem; och vilje göra såsom du sagt hafver. Och jag kallade Presterna, och tog en ed af dem, att de så göra skulle.
Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
13 Och jag skuddade mitt sköte ut, och sade: Så skudde Gud hvar och en af sitt hus, och ifrå hans arbete, den icke blifver vid detta ord, så att han blifve utskuddad och blottad. Och hela församlingen sade Amen; och lofvade Herran. Och folket gjorde så.
Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
14 Desslikes, ifrå den tiden, då mig vardt befaldt att vara landshöfding i Juda land, nämliga ifrå tjugonde årena, allt intill annat och tretionde året Konungs Arthahsasta, det är i tolf år, höll jag mig och mina bröder intet af höfdingakoste.
Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
15 Förty de förre landshöfdingar, som för mig varit hade, hade besvärat folket, och hade tagit af dem bröd och vin, och dertill fyratio siklar silfver, och deras tjenare hade haft sig väldeliga med folket; men jag gjorde icke så, för Gudsfruktans skull.
Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
16 Arbetade jag ock på murarbetet, och köpte ingen åker; och alle mine tjenare måste der komma samman till arbetes.
Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
17 Dertill voro ock af Judarna och Förstarna hundrade och femtio vid mitt bord, som till mig komne voro ifrå Hedningarna, som kringom oss äro.
Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
18 Och man måste beställa mig om dagen en oxa, och sex utvald får, och foglar, och ju i tio dagar allahanda vin tillfyllest. Likväl äskade jag intet höfdingakosten; förty tungen var svår på folkena.
Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
19 Min Gud, betänk mig till godo allt det jag desso folkena gjorde.
Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.

< Nehemja 5 >