< Nehemja 8 >

1 Då nu sjunde månaden kom, och Israels barn voro i sina städer, församlade sig allt folket, såsom en man, på breda gatone inför vattuporten, och sade till Esra den skriftlärda, att han skulle hemta fram Mose lagbok, som Herren Israel budit hade.
Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
2 Och Esra Presten hemtade fram lagen inför menighetena, både män och qvinnor, och för alla dem som det förstå kunde, på första dagen i sjunde månadenom;
Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
3 Och las deruti, på breda gatone, som för vattuporten är, allt ifrå morgonlysningen intill middag, för män och qvinnor, och för dem som det förstå kunde; och hela folkens öron voro vänd till lagbokena.
Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
4 Och Esra den Skriftlärde stod uppå en hög trästol, den de till predikan gjort hade; och när honom stodo Mattithia, Sema, Anaja, Uria, Hilkia och Maaseja, på hans högra sido; och på hans venstra Pedaja, Misael, Malchija, Hasum, Hasbadana, Zacharia och Mesullam.
Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
5 Och Esra lät upp bokena för hela folket; förty han stod högt öfver allt folket; och då han upplät henne, stod allt folket.
Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
6 Och Esra lofvade Herran den stora Guden; och allt folket svarade: Amen, Amen, med uppräckta händer; och bugade sig, och tillbådo Herran med ansigtet ned på jordena.
Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
7 Och Jesua, Bani, Serebia, Jamin, Akkub, Sabbethai, Hodija, Maaseja, Kelita, Asaria, Josabad, Hanan, Pelaja, och Leviterna, beställde att folket gaf akt uppå lagen; och folket stod uppå sitt rum.
Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
8 Och de läste uti Guds lagbok klarliga och förståndeliga, så att man förstod, då läset vardt.
Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
9 Och Nehemia, hvilken är Thirsatha, och Esra Presten, den Skriftlärde, och Leviterna, som folket höllo till att akta på, sade till allt folket: Denne dagen är helig Herranom edrom Gud; derföre sörjer intet, och gråter icke; ty allt folket gret, då de hörde lagsens ord.
Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
10 Derföre sade han till dem: Går bort, och äter det feta, och dricker det söta, och sänder dem ock delar, som intet för sig tillredt hafva; förty denne dagen är helig vårom Herra. Derföre bekymrer eder icke; ty fröjd i Herranom är edor starkhet.
Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
11 Och Leviterna stillade allt folket, och sade: Varer tyste, ty dagen är helig; bekymrens intet.
Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
12 Och allt folket gick bort till att äta, dricka och del sända, och gjorde sig en stor glädje; förty de hade förståndit orden, som man dem förkunnat hade.
Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
13 På annan dagen församlade sig öfversta fäderna ibland allt folket, och Presterna, och Leviterna, till Esra den Skriftlärda, att han skulle undervisa dem i lagsens ordom.
Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
14 Och de funno beskrifvet i lagen, att Herren genom Mose budit hade, att Israels barn skulle bo i löfhyddor, på den högtidene i sjunde månadenom.
Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
15 Och de läto det varda kunnigt, och utropadt i alla deras städer, och i Jerusalem, och sade: Går ut uppå berget, och hemter oljoqvistar, balsamqvistar, myrthenqvistar, palmqvistar och qvistar af tjockqvistadt trä, att man må göra löfhyddor, såsom skrifvet står.
Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
16 Och folket gick ut, och hemtade, och gjorde sig löfhyddor, hvar uppå sitt tak, och i sina gårdar, och i Guds hus gårdar; och uppå den breda gatone vid vattuporten, och uppå den breda gatone vid Ephraims port.
Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
17 Och hela menigheten af dem, som af fängelset igenkomne voro, gjorde löfhyddor, och bodde deruti; ty Israels barn hade ifrå Josua, Nuns sons, tid, allt intill denna dag, intet så gjort; och var en ganska stor glädje.
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
18 Och vardt hvar dag läset i Guds lagbok, ifrå första dagen allt intill den yttersta; och de höllo den högtiden i sju dagar; och på åttonde dagen församlingenes dag, såsom det borde sig.
Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.

< Nehemja 8 >