< Jesaja 45 >
1 Så säger Herren till Cores, sin smorda, den jag vid hans högra hand fattar, att jag skall underkufva Hedningarna för honom, och lösa Konungenom svärdet ifrå; på det att portarna skola öppnade varda för honom, och dörrarna icke igenlästa blifva;
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 Jag vill gå för dig, och göra backarna till jemna mark; jag vill sönderslå de koppardörrar, och sönderbryta de jernbommar;
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 Och skall gifva dig de fördolda rikedomar, och de bortgömda klenodier, på det att du skall förnimma att jag, Herren Israels Gud, dig vid ditt namn nämnt hafver;
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 För Jacob min tjenares skull, och för Israel mins utkorades skull; ja, jag kallade dig vid ditt namn, och nämnde dig, då du ännu intet kände mig.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 Jag är Herren, och eljest ingen mer; ingen Gud är utan jag. Jag tillrustade dig, då du ännu intet kände mig;
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 På det man skall förnimma, både ifrån östan och vestan, att utan mig är intet; jag är Herren, och ingen mer.
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Jag, som gör ljuset, och skapar mörkret; jag, som frid gifver, och skapar det onda; jag är Herren, som allt detta gör.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Dryper, I himlar, ofvanefter, och skyn regne rättfärdighet; jorden öppne sig, och bäre salighet, och rättfärdighet växe till med, jag Herren skapar honom.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Ve honom, som träter med sinom skapare, nämliga krukan med krukomakaren. Månn leret säga till krukomakaren: Hvad gör du? Du bevisar icke dina händer på ditt verk.
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Ve honom, som till fadren säger: Hvi hafver du aflat mig? och till qvinnona: Hvi födde du?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Så säger Herren, den Helige i Israel, och hans mästare: Äsker tecken af mig, viser min barn och mina händers verk till mig.
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 Jag hafver gjort jordena, och skapat menniskona deruppå; jag är den, hvilkens händer himmelen utsträckt hafva, och budit allom hans här.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 Jag hafver uppväckt honom uti rättfärdighet, och jag skall göra alla hans vägar släta; han skall bygga min stad, och låta mina fångar lösa, icke för penningar eller gåfvor, säger Herren Zebaoth.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Så säger Herren: De Egyptiers handel, och de Ethiopers förvärfning, och det stora folket i Seba, skola gifva sig under dig, och vara dine egne; de skola följa dig, uti fjettrar skola de gå, och skola nederfalla för dig, och bedja dig; ty när dig är Gud, och är eljest ingen gud mer.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Sannerliga äst du en fördold Gud, du Israels Gud, Frälsaren.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Men de afgudamakare måste allesammans med skam och hån bestå, och med hvarannan med blygd afgå.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Men Israel varder förlossad genom Herran evinnerliga; och skall icke till skam och spott varda någon tid i evighet.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 Ty så säger Herren, som himmelen skapat hafver, Gud, som jordena beredt hafver, och hafver gjort henne och tillredt, och icke så gjort henne, att hon skulle tom vara; utan hafver tillredt henne, att man skall bo deruppå. Jag är Herren, och ingen mer.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Jag hafver icke hemliga talat uti något mörkt rum på jordene; jag hafver icke fåfängt sagt till Jacobs säd: Söker mig; ty jag är Herren, som om rättfärdighet talar, och förkunnar det rätt är.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Låt församla sig och tillhopa framkomma Hedningarnas hjeltar, de der intet veta, och bära deras afgudars stockar, och bedja den gud, som dem intet hjelpa kan.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Förkunner och kommer hit, rådslår tillsamman. Ho hafver detta låtit säga af ålder, och på den tiden förkunnat det? Hafver icke jag Herren gjort det? Och är eljest ingen Gud utan jag; en rätt Gud och Frälsare, och ingen är utan jag.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Vänder eder till mig, så varden I salige, alle verldenes ändar; ty jag är Gud, och ingen mer.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 Jag svär vid mig sjelf, och ett rättfärdighets ord går utaf min mun, der skall det blifva vid; nämliga, mig skola, all knä böjas, och alla tungor svärja;
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 ( Och säga: ) Uti Herranom hafver jag rättfärdighet och starkhet. Desse skola ock komma till honom; men alle de, som honom emotstå, måste till skam varda.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 Ty uti Herranom varder all Israels säd rättfärdigad, och skall berömma sig af honom.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.