< Höga Visan 1 >

1 Salomos Höga Visa.
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 Han kysse mig med sins muns kyssande; ty din bröst äro ljufligare än vin;
Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Att man må lukta din goda salvo; ditt Namn är en utgjuten salva; derföre hafva pigorna dig kär.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Drag mig efter dig, så löpe vi; Konungen förde mig in uti sin kammar: Vi fröjde oss, och äre glade öfver dig; vi tänke uppå din bröst mer än uppå vin; de fromme älska dig.
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 Jag är svart, men ganska täck, I Jerusalems döttrar, såsom Kedars hyddor, såsom Salomos tapeter.
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 Ser icke derefter, att jag så svart är; ty solen hafver bränt mig; mins moders barn vredgas emot mig. Man hafver satt mig till vingårdsvaktersko; men min vingård, den jag hade, bevarade jag icke.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Säg mig du, den min själ älskar, hvar du beter, hvar du hvilar om middagen; att jag icke skall gå hit och dit, till dina stallbröders hjordar.
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
8 Känner du dig icke, du dägeligasta ibland qvinnor, så gack uppå fårens fotspår, och bet din kid vid herdahusen.
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
9 Jag liknar dig, min kära, vid mitt resigtyg, vid Pharaos vagnar.
Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Dina kinder stå ljufliga i spann, och din hals i kedjo.
Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Vi vilje göra dig gyldene spann med silfdoppor.
Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
12 Då Konungen vände sig hit, gaf min nardus sina lukt.
Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Min vän är mig ett knippe af myrrham, det emellan min bröst hänger.
Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Min vän är mig en drufva Copher, uti de vingårdar i EnGedi.
Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
15 Si, min kära, du äst dägelig; dägelig äst du, din ögon äro såsom dufvoögon.
Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
16 Si, min vän, du äst dägelig och ljuflig; vår säng grönskas.
Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
17 Vår hus bjelkar äro cedreträ; våre sparrar äro cypress.
Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.

< Höga Visan 1 >