< 1 Krönikeboken 19 >

1 Så begaf sig derefter, att Nahas, Ammons barnas Konung, blef död, och hans son vardt Konung i hans stad,
Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Då tänkte David: Jag vill göra barmhertighet på Hanun, Nahas son; ty hans fader hafver gjort barmhertighet med mig. Och han sände dit båd, till att hugsvala honom efter hans fader. Och då Davids tjenare kommo uti Ammons barnas land, till Hanun, att hugsvala honom,
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
3 Sade de Förstar för Ammons barn till Hanun: Menar du, att David ärar din fader för din ögon, att han sänder hugsvalare till dig? Ja, hans tjenare äro komne till dig, till att utfråga, bespana och bespeja landet.
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Då tog Hanun Davids tjenare, och rakade dem, och skar deras kläder half bort allt intill länderna, och lät gå dem.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
5 Och de gingo sin väg, och bådade det David med några män. Han sände emot dem; förty männerna voro svårliga beskämde, och Konungen sade: Blifver i Jericho, tilldess edart skägg växer, sedan kommer då igen.
Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Då Ammons barn sågo, att de illa luktade för David, sände de bort, både Hanun och Ammons barn, tusende centener silfver, till att besolda sig vagnar och resenärar utu Mesopotamien, utu Syrien Maacha, och utu Zoba;
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
7 Och besoldade tu och tretio tusend vagnar, och Konungen i Maacha med hans folk. De kommo och lägrade sig för Medba. Och Ammons barn församlade sig desslikes utu sina städer, och kommo till strids.
Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
8 Då David det hörde, sände han Joab dit, med hela de hjeltars här.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
9 Och Ammons barn voro utdragne, och skickade sig till strid för stadsporten; men Konungarna, som komne voro, höllo besynnerliga i markene.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
10 Då nu Joab såg, att både för honom och bak honom var strid emot honom, utvalde han af alla unga män i Israel, och skickade sig emot de Syrer.
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
11 Det andra folket fick han under Abisai sin broders hand, att de skulle draga emot Ammons barn;
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
12 Och sade: Om de Syrer varda mig för starke, så kom mig till hjelp; om Ammons barn varda dig för starke, så vill jag komma dig till hjelp.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
13 Var tröst, och låt oss trösteliga handla för vårt folk, och för vår Guds städer. Herren göre hvad honom täckes.
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
14 Och Joab drog fram med det folk, som med honom var, till att strida emot de Syrer; och de flydde för honom.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
15 Då nu Ammons barn sågo, att de Syrer flydde, flydde de ock för Abisai hans broder, och drogo in i staden; men Joab drog till Jerusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
16 Som de Syrer sågo, att de för Israel slagne voro, sände de ut båd, och läto utkomma de Syrer på hinsidon älfven; och Sophach, HadarEsers härhöfvitsman, drog för dem.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
17 Då det blef sagdt David, församlade han hela Israel, och drog öfver Jordan; och då han kom till dem, skickade han sig emot dem. Och David skickade sig emot de Syrer till strid, och de stridde med honom.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
18 Men de Syrer flydde för Israel; och David slog af de Syrer sjutusend vagnar, och fyratiotusend män till fot; dertill drap han Sophach härhöfvitsmannen.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
19 Då HadarEsers tjenare sågo, att de voro slagne för Israel, gjorde de frid med David och hans tjenare. Och de Syrer ville icke mer hjelpa Ammons barn.
Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< 1 Krönikeboken 19 >