< 2 Krönikeboken 5 >

1 Alltså vardt allt arbetet fullkomnadt, som Salomo gjorde på Herrans hus. Och Salomo lät komma derin allt det hans fader David helgat hade, nämliga silfver och guld, och allahanda tyg; och lade det in uti fataburen i Guds hus.
Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
2 Då församlade Salomo alla äldsta i Israel, alla höfdingar i slägterna, Förstar för fäderna i Israels barn, till Jerusalem, att de skulle låta uppkomma Herrans förbunds ark utu Davids stad, det är Zion.
Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
3 Och församlade sig till Konungen alle Israels män på högtidene, det är i sjunde månadenom;
Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
4 Och kommo alle äldste i Israel; och de Leviter togo arken;
Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
5 Och båro honom upp, samt med vittnesbördsens tabernakel, och all helig tyg, som i tabernaklet voro; och Presterna Leviterna båro det allt med upp.
ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
6 Men Konung Salomo och hela Israels menighet med honom, församlad inför arken, offrade får och fä, så mycket, att det ingen tälja eller räkna kunde.
ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
7 Alltså båro Presterna Herrans förbunds ark uti sitt rum, i husets chor, uti det aldrahelgasta, under Cherubims vingar;
Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
8 Så att Cherubim utsträckte sina vingar öfver arkens rum; och Cherubim öfvertäckte arken och hans stänger, ofvantill.
Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
9 Men stängerna voro så långa, att man såg ändarna på dem för choren ifrån arkenom; men utantill såg man dem icke; och blef han der allt intill denna dag.
Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
10 Och i arken var intet utan de två taflor, som Mose hade lagt deruti i Horeb, då Herren ett förbund gjorde med Israels barn, den tid de utur Egypten drogo.
Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
11 Och då Presterna gingo utu det helga; ty alle de Prester, som för handene voro, helgade sig, så att ock skiften icke hållne vordo,
Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
12 Och de Leviter, med alla dem som under Assaph, Heman, Jeduthun, och deras barn och bröder, voro, klädde med linnen kläder, sjöngo med cymbaler, psaltare och harpor, och stodo österut ifrån altaret, och när dem tjugu och hundrade Prester, som blåste med trummeter;
Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
13 Och det var, såsom det hade varit allt en som trummetade, och sjöng, såsom man hörde ena röst, till att lofva och tacka Herranom; och då rösten upphof sig af trummeterna, cymbaler och annor strängaspel, och af Herrans lof, att han mild är, och hans barmhertighet varar till evig tid; då vardt Herrans hus uppfyldt med ett moln;
Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
14 Så att Presterna icke stå kunde, till att tjena, för molnets skull; ty Herrans härlighet uppfyllde Guds hus.
choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

< 2 Krönikeboken 5 >