< Zaburi 7 >

1 Ombolezo la Daudi kwa Bwana kwa sababu ya Kushi, Mbenyamini. Ee Bwana, Mungu wangu, ninakukimbilia wewe, uniokoe na kunikomboa na wote wanaonifuatia,
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 la sivyo watanirarua kama simba na kunichana vipande vipande, asiwepo wa kuniokoa.
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Ee Bwana, Mungu wangu, kama nimetenda haya na kuna hatia mikononi mwangu,
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 au ikiwa nimemtenda uovu aliye na amani nami, au nimemnyangʼanya adui yangu pasipo sababu,
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 basi adui anifuatie na kunipata, auponde uhai wangu ardhini na kunilaza mavumbini.
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
6 Amka kwa hasira yako, Ee Bwana, inuka dhidi ya ghadhabu ya adui zangu. Amka, Mungu wangu, uamue haki.
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Kusanyiko la watu na likuzunguke. Watawale kutoka juu.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
8 Bwana na awahukumu kabila za watu. Nihukumu Ee Bwana, kwa kadiri ya haki yangu, kwa kadiri ya uadilifu wangu, Ewe Uliye Juu Sana.
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Ee Mungu mwenye haki, uchunguzaye mawazo na mioyo, komesha ghasia za waovu na ufanye wenye haki waishi kwa amani.
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Ngao langu ni Mungu Aliye Juu Sana, awaokoaye wanyofu wa moyo.
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mungu ni mwamuzi mwenye haki, Mungu aghadhibikaye kila siku.
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Kama hakutuhurumia, atanoa upanga wake, ataupinda na kuufunga uzi upinde wake.
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Ameandaa silaha zake kali, ameweka tayari mishale yake ya moto.
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Yeye aliye na mimba ya uovu na achukuaye mimba ya ghasia huzaa uongo.
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Yeye achimbaye shimo na kulifukua hutumbukia katika shimo alilochimba mwenyewe.
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Ghasia azianzishazo humrudia mwenyewe, ukatili wake humrudia kichwani.
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Nitamshukuru Bwana kwa ajili ya haki yake, na nitaliimbia sifa jina la Bwana Aliye Juu Sana.
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

< Zaburi 7 >