< Salmos 120 >
1 En mi angustia, mi llanto subió al Señor, y él me dio una respuesta.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 Oh Señor, sé el salvador de mi alma de los labios mentirosos y de la lengua del engaño.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 ¿Qué castigo te dará? ¿Qué más te hará él, lengua falsa?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Flechas afiladas del fuerte y fuego ardiente.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 La aflicción es mía porque soy extraño en Mesec, y vivo en las tiendas de Cedar.
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 Mi alma ha estado viviendo por mucho tiempo con los que odian la paz.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Estoy a favor de la paz; pero cuando digo eso, están a favor de la guerra.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.