< Salmos 135 >
1 Deja que el Señor sea alabado. Oh siervos del Señor, alaben el nombre del Señor.
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 Tú que estás en la casa del Señor, y en los espacios abiertos de la casa de nuestro Dios,
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Alaben a Jah, porque él es bueno; hagan melodía a su nombre, porque es agradable.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Porque el Señor tomó consigo a Jacob, y a Israel por su propiedad.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Sé que el Señor es grande, y que nuestro Señor es más grande que todos los demás dioses.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 El Señor hizo todo lo que le agradaba, en el cielo, en la tierra, en los mares y en todas las aguas profundas.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Él hace que las nieblas suban desde los confines de la tierra; él hace llamas de trueno por la lluvia; Él envía los vientos desde sus almacenes.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 El mató las primicias de Egipto, de hombres y de bestias.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Envió señales y maravillas en medio de ti, oh Egipto, sobre Faraón y sobre todos sus siervos.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Él venció a las grandes naciones, y mató a los reyes fuertes;
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sehón, rey de los amorreos, y Og, rey de Basán, y todos los reinos de Canaán;
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 Y dieron su tierra por heredad, por heredad a Israel su pueblo.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Oh Señor, tu nombre es eterno; y el recuerdo de ti no tendrá fin.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Porque el Señor juzgará la causa de su pueblo; tiene compasión de sus sirvientes.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Las imágenes de las naciones son plata y oro, obra de manos de hombres.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Tienen bocas, pero ninguna voz; tienen ojos, pero no ven;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Tienen oídos, pero no oyen; y no hay aliento en sus bocas.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Los que los hacen son como ellos; y también lo es todo el que pone su esperanza en ellos.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Alaben a Jehová, oh hijos de Israel; alaben á Jehová, oh hijos de Aarón.
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Alaben al Señor, hijos de Leví, alaben todos los adoradores del Señor.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Bendito sea el Señor desde Sión, el Señor cuya casa está en Jerusalén, sea alabado Jehová.
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.