< Job 40 >
1 Dios siguió hablando a Job.
Yehova anati kwa Yobu:
2 “¿Todavía vas a pelear con el Todopoderoso y tratar de enderezarlo? Quien discute con Dios debe dar alguna respuesta”.
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Job respondió al Señor:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 “Yo no soy nada. No tengo respuestas. Pongo mi mano delante de mi boca.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Ya he dicho demasiado y no diré nada más”.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Entonces el Señor respondió a Job desde el torbellino:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 “Prepárate, sé fuerte, porque voy a interrogarte y debes responderme.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 “¿De verdad vas a decir que mis decisiones están equivocadas? ¿Vas a condenarme para tener razón?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 ¿Eres tan poderoso como yo? ¿Truena tu voz como la mía?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 ¿Por qué no te vistes de majestad y dignidad, y te revistes de gloria y esplendor?
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Da rienda suelta a tu feroz ira. Humilla a los soberbios con una mirada.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Derriba a los soberbios con tu mirada; pisotea a los malvados allí donde están.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Entiérralos en el polvo; enciérralos en la tumba.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Entonces también estaré de acuerdo en que tu propia fuerza puede salvarte.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 “Considera a Behemot, una criatura que hice igual que a ti. Come hierba como el ganado.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Mira sus poderosos lomos, los músculos de su vientre.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Dobla su cola como un cedro; los tendones de sus muslos son fuertes.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Sus huesos son como tubos de bronce, sus miembros como barras de hierro.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Es el ejemplo más importante de lo que Dios puede hacer; sólo el que lo hizo puede acercarse a él con una espada.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Las colinas producen alimento para él, y todos los animales salvajes juegan allí.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Se encuentra bajo el loto; se esconde en los juncos del pantano.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 El loto la cubre de sombra; los sauces del valle la rodean.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Aunque el río se desborde, no se preocupa; permanece en calma cuando el río Jordán se agita contra él.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Nadie puede atraparlo mientras mira, ni perforar su nariz con un lazo”.
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?