< Job 39 >
1 “¿Sabes cuándo paren las cabras salvajes? ¿Has observado los dolores de parto de los ciervos?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 ¿Sabes cuántos meses llevan a sus crías? ¿Sabes en qué momento dan a luz?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Se agazapan en el parto para dar a luz a sus crías.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Sus crías se fortalecen en el campo, se van y no vuelven.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 “¿Quién le dio la libertad al asno salvaje? ¿Quién lo liberó de sus ataduras?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Yo le he dado el desierto como hogar, las llanuras saladas como lugar para vivir.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Desprecia el ruido de la ciudad; no necesita escuchar los gritos del conductor.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Caza en los montes los pastos, buscando toda clase de plantas verdes para comer.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 “¿Está dispuesto el buey salvaje a servirte? ¿Pasará la noche en tu pesebre?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 ¿Puedes atar un buey salvaje a un arado? ¿Puedes hacer que labre tus campos por ti?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Como es tan poderoso, ¿puedes confiar en él? ¿Puedes confiar en él para que te haga el trabajo pesado?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 ¿Estás seguro de que recogerá tu grano y lo llevará a tu era?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 “El avestruz bate con orgullo sus alas, pero no se parecen en nada a las plumas de vuelo de la cigüeña.
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 La avestruz abandona sus huevos en el suelo, dejándolos para que se calienten en el polvo.
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 No cree que puedan ser aplastados bajo sus pies, pisoteados por un animal salvaje.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Es dura con sus crías, actuando como si no le pertenecieran. No le importa que todo su trabajo haya sido en vano.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Porque yo, Dios, la hice olvidar la sabiduría; no tuvo su parte de inteligencia.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Pero cuando lo necesita, puede saltar y correr, burlando al caballo y a su jinete con su velocidad.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 “¿Le diste al caballo su fuerza? ¿Le pusiste crines en el cuello?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 ¿Le hiciste capaz de saltar como una langosta? Su fuerte resoplido es aterrador.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Da zarpazos en el suelo, se levanta con fuerza y se lanza a la batalla.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Se ríe del miedo; no se asusta en absoluto.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 El carcaj lleno de flechas resuena contra él; la lanza y la jabalina resplandecen a la luz del sol.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Temblando de rabia galopa por el suelo; no puede quedarse quieto cuando suena la trompeta.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Cuando suena la trompeta, está listo; siente el sonido de la batalla desde lejos, oye los gritos de los comandantes.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 “¿Es por tu sabiduría que el halcón se eleva, extendiendo sus alas hacia el sur?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 ¿Acaso ordenas al águila que vuele alto y haga su nido en las cumbres de los montes?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Vive entre los acantilados y se posa en un peñasco remoto.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Desde allí espía a su presa desde lejos, fijando su mirada en su víctima. Sus polluelos tragan sangre con avidez.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Donde están los cadáveres, allí se encuentran las aves de rapiña”.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”