< Jeremija 1 >
1 Beseda Jeremija, Hilkijájevega sina, izmed duhovnikov, ki so bili v Anatótu v Benjaminovi deželi,
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 kateremu je prišla Gospodova beseda v dneh Jošíja, Amónovega sina, Judovega kralja, v trinajstem letu njegovega kraljevanja.
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 Ta je prišla tudi v dneh Jojakíma, Jošíjevega sina, Judovega kralja, do konca enajstega leta Sedekíja, Jošíjevega sina, Judovega kralja, do preselitve jeruzalemskega ujetništva v petem mesecu.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 Potem je prišla k meni Gospodova beseda, rekoč:
Yehova anayankhula nane kuti,
5 »Preden sem te oblikoval v trebuhu, sem te poznal. Preden si prišel iz maternice, sem te posvetil in te odredil [za] preroka narodom.«
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 Potem sem rekel: »Jaz, ah Gospod Bog! Glej, ne morem govoriti, kajti jaz sem otrok.«
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 Toda Gospod mi je rekel: »Ne govori: ›Jaz sem otrok, ‹ kajti šel boš k vsem, h katerim te bom poslal in karkoli ti zapovem, boš govoril.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Ne boj se njihovih obrazov, kajti jaz sem s teboj, da te rešujem, « govori Gospod.
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 Potem je Gospod iztegnil svojo roko in se dotaknil mojih ust. Gospod mi je rekel: »Glej, svoje besede sem položil v tvoja usta.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Glej, ta dan sem te postavil nad narode in nad kraljestva, da izkoreniniš, da podiraš, da uničiš, da zrušiš, da zgradiš in da sadiš.«
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 Poleg tega je prišla k meni Gospodova beseda, rekoč: »Jeremija, kaj vidiš?« Rekel sem: »Vidim palico mandljevca.«
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 Potem mi je Gospod rekel: »Dobro si videl, kajti pospešil bom svojo besedo, da jo izvršim.«
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 Gospodova beseda je drugič prišla k meni, rekoč: »Kaj vidiš?« Rekel sem: »Vidim lonec, v katerem vre in njegova stran je proti severu.«
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Potem mi je Gospod rekel: »Iz severa bo izbruhnilo zlo nad vse prebivalce dežele.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 Kajti, glej, poklical bom vse družine kraljestev iz severa, « govori Gospod »in prišli bodo in postavili bodo vsak svoj prestol ob vhodu velikih vrat [prestolnice] Jeruzalem in zoper vse njene zidove naokoli in zoper vsa Judova mesta.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Izrekel bom svoje sodbe zoper njih glede vseh njihovih zlobnosti, ki se dotikajo vseh svojih zlobnosti, ki so me zapustili in zažigali kadilo drugim bogovom ter oboževali dela svojih lastnih rok.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Opaši si torej svoja ledja in vstani ter jim spregovori vse, kar sem ti zapovedal. Ne bodi zaprepaden ob njihovih obrazih, da te ne bi zbegal pred njimi.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 Kajti glej, ta dan sem te naredil za obrambno mesto, železen steber in bronaste zidove zoper celotno deželo, zoper Judove kralje, zoper njegove prince in zoper njegove duhovnike in zoper ljudstvo dežele.
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 Borili se bodo zoper tebe, toda ne bodo prevladali zoper tebe, kajti jaz sem s teboj, « govori Gospod, »da te osvobodim.«
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.