< Jeremija 2 >

1 Poleg tega mi je prišla Gospodova beseda, rekoč:
Yehova anandiwuza kuti,
2 »Pojdi in jokaj v ušesa [prestolnice] Jeruzalem, rekoč: ›Tako govori Gospod: ›Spominjam se tebe, prijaznosti tvoje mladosti, ljubezni tvojih zaročencev, ko si šla za menoj v divjino, v deželo, ki ni bila posejana.‹
“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
3 Izrael je bil svetost Gospodu in prvi sadovi njegovega donosa. Vse, ki ga požirajo, bo jezil; zlo bo prišlo nadnje, ‹« govori Gospod.
Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
4 Poslušajte besedo od Gospoda, oh Jakobova hiša in vse družine Izraelove hiše:
Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
5 »Tako govori Gospod: ›Kakšno krivičnost so vaši očetje našli v meni, da so odšli daleč od mene in hodili za ničevostjo in postali ničevost?
Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
6 Niti niso rekli: ›Kje je Gospod, ki nas je privedel gor iz egiptovske dežele, ki nas je vodil skozi divjino, skozi deželo puščav in jam, skozi deželo suše in smrtne sence, skozi deželo, skozi katero noben človek ne gre in kjer noben človek ne prebiva?‹
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
7 Privedel sem vas v obilno deželo, da jeste njen sad in njeno dobroto, toda ko ste vstopili, ste omadeževali mojo deželo in mojo dediščino naredili ogabnost.
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
8 Duhovniki niso rekli: ›Kje je Gospod?‹ Tisti, ki so se ukvarjali s postavo, me niso poznali. Tudi pastirji so se pregrešili zoper mene in preroki so prerokovali pri Báalu in hodili za stvarmi, ki ne storijo koristi.
Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
9 Zato se bom še pravdal z vami, ‹ govori Gospod ›in z vašimi otrok otroki se bom pravdal.
“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 Kajti šel bom čez otoke Kitéjcev in videl in poslal v Kedár in marljivo preudaril in videl, če je tam takšna stvar.
Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Je narod spremenil svoje bogove, ki vendar niso bogovi? Toda moje ljudstvo je zamenjalo svojo slavo za to, kar ne koristi.
Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
12 Bodite osupla, oh ve nebesa, ob tem in bodite strašno prestrašena, bodite zelo zapuščena, ‹ govori Gospod.
Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
13 ›Kajti moje ljudstvo je zagrešilo dve hudobiji; zapustili so mene, studenec živih vodá in si izklesali vodne zbiralnike, razpokane vodne zbiralnike, ki ne morejo držati vode.
“Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
14 Ali je Izrael služabnik? Ali je doma rojeni suženj? Zakaj je oplenjen?
Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 Mladi levi so rjoveli nanj in vpili. Njegovo deželo so naredili opustošeno. Njegova mesta so požgana, brez prebivalcev.
Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Tudi otroci Nofa in Tahpanhésa so zlomili krono tvoje glave.
Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
17 Ali si nisi tega priskrbela k sebi v tem, da si zapustila Gospoda, svojega Boga, ko te je vodil po poti?
Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 In sedaj, kaj imaš opraviti na egiptovski poti, da piješ vode iz Sihorja? Ali kaj imaš opraviti na asirski poti, da piješ vode iz reke?
Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 Tvoja lastna zlobnost te bo grajala in tvoja zdrknjenja nazaj te bodo opominjala. Vedi torej in vidi, da je to huda stvar in grenka, da si zapustila Gospoda, svojega Boga in da mojega strahu ni v tebi, ‹ govori Gospod, Bog nad bojevniki.
Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
20 ›Kajti od starih časov sem prelomil tvoj jarem in raztrgal tvoje vezi; ti pa praviš: ›Jaz ne bom grešila; ‹ ko tavaš na vsakem visokem hribu in tavaš pod vsakim zelenim drevesom in igraš vlačugo.
“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 Vendar sem te zasadil [kot] plemenito trto, popolnoma pravo seme. Kako si se mi potem obrnila v degenerirano sadiko tuje trte?
Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
22 Kajti čeprav se umivaš s solitrom in si jemlješ precej mila, je vendar tvoja krivičnost zaznamovana pred menoj, ‹ govori Gospod Bog.
Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
23 Kako lahko rečeš: ›Nisem onesnažena, nisem odšla za Báali?‹ Poglej svojo pot v dolini, spoznaj, kaj si storila. Ti si hitri [enogrbi] velblod, ki prečka svoje poti,
“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
24 divja oslica, vajena divjine, ki voha veter po svojem zadovoljstvu; kdo jo ob njeni priložnosti lahko odvrne proč? Vsi tisti, ki jo iščejo, se ne bodo izmučili; v njenem mesecu jo bodo našli.
wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 Zadrži svoje stopalo pred bosostjo in svoje grlo pred žejo. Toda ti praviš: ›Tam ni upanja. Ne, kajti ljubila sem tujce in za njimi bom šla.‹
Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
26 Kakor je tat osramočen, ko je najden, tako je osramočena Izraelova hiša; oni, njihovi kralji, njihovi princi, njihovi duhovniki in njihovi preroki,
“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
27 rekoč lesu: ›Ti si moj oče; ‹ in skali: ›Ti si me rodila.‹ Kajti obrnili so mi svoj hrbet in ne svojega obraza. Toda v času njihove stiske bodo rekli: ›Vstani in nas reši.‹
Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 Toda kje so tvoji bogovi, ki si jih naredila? Naj vstanejo, če te lahko rešijo v času tvoje stiske, kajti glede na število tvojih mest so tvoji bogovi, oh Juda.
Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
29 Zakaj se hočete pravdati z menoj? Vsi vi ste se pregrešili zoper mene, ‹ govori Gospod.
“Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
30 ›V prazno sem udaril vaše otroke; nobenega grajanja niso prejeli. Vaš lastni meč je požrl vaše preroke kakor uničujoč lev.
“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
31 Oh rod, poglejte Gospodovo besedo. Ali sem bil Izraelu divjina? Dežela teme? Zakaj pravi moje ljudstvo: ›Mi smo gospodje, nič več ne bomo prišli k tebi?‹
“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
32 Mar lahko devica pozabi svoje ornamente ali nevesta svoj okras? Vendar me moje ljudstvo pozablja brez števila dni.
Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
33 Zakaj krajšaš svojo pot, da iščeš ljubezen? Zato si tudi zlobne učila svojih poti.
Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 Tudi v krajcih tvojega oblačila je najdena kri duš ubogih nedolžnih. Nisem je našel s skrivnim iskanjem, temveč na vseh teh.
Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35 Vendar praviš: ›Ker sem nedolžna, se bo njegova jeza zagotovo obrnila od mene.‹ Glej, jaz se bom pravdal s teboj, ker praviš: ›Nisem grešila.‹
inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Zakaj toliko hodiš sem ter tja, da bi spremenila svojo pot? Tudi ti boš osramočena od Egipta, kakor si bila osramočena od Asirije.
Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 Da, šla boš naprej od njega, s svojimi rokami na svoji glavi, kajti Gospod je zavrnil tvoje zaupnosti in ne boš uspela v njih.‹«
Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.

< Jeremija 2 >