< Књига пророка Осије 3 >
1 Потом рече ми Господ: Иди опет, љуби жену коју љуби љубавник а она чини прељубу, као што Господ љуби синове Израиљеве а они гледају за туђим боговима и љубе жбанове винске
Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
2 И купих је за петнаест сикала сребра и гомор и по јечма.
Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
3 И рекох јој: Седи код мене дуго времена, и не курвај се, и не буди другог; тако ћу и ја бити твој.
Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
4 Јер ће дуго времена синови Израиљеви седети без цара и без кнеза и без жртве и без ступа и без оплећка и ликова.
Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
5 После ће се обратити и тражиће Господа Бога свог и Давида цара свог, и у страху ће приступити ка Господу и благости Његовој у последња времена.
Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.