< Књига пророка Исаије 49 >
1 Послушајте ме, острва, и пазите народи далеки. Господ ме позва од утробе; од утробе матере моје помену име моје.
Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
2 И учинио је уста моја да су као оштар мач, у сену руке своје сакри ме; учинио ме је сјајном стрелом, и тулу свом сакри ме.
Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
3 И рече ми: Ти си слуга мој, у Израиљу ћу се тобом прославити.
Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
4 А ја рекох: Узалуд се трудих, узалуд и напразно потроших силу своју; али опет суд је мој у Господа и посао мој у Бога мог.
Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
5 А сада говори Господ, који ме је саздао од утробе материне да сам Му слуга, да Му доведем натраг Јакова; ако се Израиљ и не сабере, опет ћу се прославити пред Господом, и Бог ће мој бити сила моја.
Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
6 И рече ми: Мало је да ми будеш слуга да се подигне племе Јаковљево и да се врати остатак Израиљев, него те учиних виделом народима да будеш моје спасење до крајева земаљских.
Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
7 Овако вели Господ, Избавитељ Израиљев, Светац његов, ономе кога презиру, на кога се гади народ, слузи оних који господаре: цареви ће видети и устати, и кнезови ће се поклонити ради Господа, који је веран, ради Свеца Израиљевог, који те је изабрао.
Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
8 Овако вели Господ: У време милосно услиших те, и у дан спасења помогох ти; и чуваћу те и даћу те да будеш завет народу да утврдиш земљу и наследиш опустело наследство;
Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
9 Да кажеш сужњима: Изађите; онима који су у мраку: Покажите се. Они ће покрај путева пасти, и паша ће им бити по свим високим местима.
Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
10 Неће бити гладни ни жедни, неће их бити врућина ни сунце; јер коме их је жао, он ће их водити, и покрај извора водених проводиће их.
Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
11 И све горе своје обратићу у путеве, и стазе ће моје бити повишене.
Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
12 Гле, ови ће из далека доћи, гле, и они од севера и од запада, и они из земље синске.
Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
13 Певајте, небеса, и весели се, земљо, подвикујте, горе, весело; јер Господ утеши свој народ, и на невољнике своје смилова се.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
14 Али Сион рече: Остави ме Господ, и заборави ме Господ.
Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
15 Може ли жена заборавити пород свој да се не смилује на чедо утробе своје? А да би га и заборавила, ја нећу заборавити тебе.
“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
16 Гле, на длановима сам те изрезао; зидови су твоји једнако преда мном.
Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
17 Похитаће синови твоји, а који те раскопаваше и пустошише, отићи ће од тебе.
Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
18 Подигни очи своје унаоколо, и види: сви се они скупљају и иду к теби. Тако био ја жив, вели Господ, свима њима као накитом заоденућеш се, и уресићеш се њима као невеста.
Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
19 Јер развалине твоје и пустолине и потрвена земља твоја биће тада тесна за становнике кад се удаље они који те прождираше.
“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
20 И деца коју ћеш имати, пошто си била без деце, рећи ће да чујеш: Тесно ми је ово место, помакни се да се могу настанити.
Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
21 А ти ћеш рећи у срцу свом: Ко ми их роди, јер бејах сирота и инокосна, заробљена и прогнана? И ко их отхрани? Ето, ја бејах остала сама, а где они беху?
Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
22 Овако вели Господ Господ: Ево, подигнућу руку своју к народима, и к племенима ћу подигнути заставу своју, и донеће синове твоје у наручју, и кћери твоје на раменима ће се носити.
Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
23 И цареви ће бити хранитељи твоји и царице њихове твоје дојкиње, и клањаће ти се лицем до земље, и прах с ногу твојих лизаће, и познаћеш да сам ја Господ, и да се неће осрамотити они који мене чекају.
Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
24 Хоће ли се јунаку узети плен и хоће ли се отети робље праведноме?
Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
25 Јер овако говори Господ: и робље јунаку узеће се и плен јакоме отеће се, јер ћу се ја прети с онима који се с тобом пру, и синове твоје ја ћу избавити;
Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
26 И који ти криво чине, нахранићу их њиховим месом и опиће се својом крвљу као новим вином; и познаће свако тело да сам ја Господ Спаситељ твој и Избавитељ твој, јаки Бог Јаковљев.
Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”