< Псалтирь 3 >

1 Псалом Давида, когда он бежал от Авессалома, сына своего. Господи! как умножились враги мои! Многие восстают на меня
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 многие говорят душе моей: “нет ему спасения в Боге”.
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 Но Ты, Господи, щит предо мною, слава моя, и Ты возносишь голову мою.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 Гласом моим взываю к Господу, и Он слышит меня со святой горы Своей.
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 Ложусь я, сплю и встаю, ибо Господь защищает меня.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 Не убоюсь тем народа, которые со всех сторон ополчились на меня.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Восстань, Господи! спаси меня, Боже мой! ибо Ты поражаешь в ланиту всех врагов моих; сокрушаешь зубы нечестивых.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 От Господа спасение. Над народом Твоим благословение Твое.
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)

< Псалтирь 3 >