< Псалтирь 2 >
1 Псалом Давида. Зачем мятутся народы, и племена замышляют тщетное?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Восстают цари земли, и князья совещаются вместе против Господа и против Помазанника Его.
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 “Расторгнем узы их, и свергнем с себя оковы их”.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Живущий на небесах посмеется, Господь поругается им.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Тогда скажет им во гневе Своем и яростью Своею приведет их в смятение:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 “Я помазал Царя Моего над Сионом, святою горою Моею;
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 возвещу определение: Господь сказал Мне: Ты Сын Мой; Я ныне родил Тебя;
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 проси у Меня, и дам народы в наследие Тебе и пределы земли во владение Тебе;
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Ты поразишь их жезлом железным; сокрушишь их, как сосуд горшечника”.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Итак вразумитесь, цари; научитесь, судьи земли!
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Служите Господу со страхом и радуйтесь с трепетом.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Почтите Сына, чтобы Он не прогневался, и чтобы вам не погибнуть в пути вашем, ибо гнев Его возгорится вскоре. Блаженны все, уповающие на Него.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.