< Нумерь 29 >

1 Ын луна а шаптя, ын чя динтый зи а луний, сэ авець о адунаре сфынтэ: атунч сэ ну фачець ничо лукраре де слугэ. Зиуа ачаста сэ фие веститэ ынтре вой ку сунет де трымбицэ.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Сэ адучець ка ардере-де-тот де ун мирос плэкут Домнулуй ун вицел, ун бербек ши шапте мей де ун ан фэрэ кусур.
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Сэ май адэугаць ши дарул лор де мынкаре дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн, трей зечимь пентру вицел, доуэ зечимь пентру бербек
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 ши о зечиме пентру фиекаре дин чей шапте мей.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, ка сэ факэ испэшире пентру вой.
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Сэ адучець ачесте жертфе, афарэ де ардеря-де-тот ши дарул ей де мынкаре дин фиекаре лунэ, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфеле де бэутурэ каре се адаугэ ла еле, дупэ рындуелиле ашезате. Ачестя сунт ниште жертфе мистуите де фок, де ун мирос плэкут Домнулуй.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Ын зиуа а зечя а ачестей лунь а шаптя, сэ авець о адунаре сфынтэ ши сэ вэ смериць суфлетеле; атунч сэ ну фачець ничо лукраре.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Сэ адучець ка ардере-де-тот де ун мирос плэкут Домнулуй: ун вицел, ун бербек ши шапте мей де ун ан фэрэ кусур.
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Сэ май адэугаць ши дарул лор де мынкаре дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн, трей зечимь пентру вицел, доуэ зечимь пентру бербек
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 ши о зечиме пентру фиекаре дин чей шапте мей.
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де жертфа де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ ку дарул ей де мынкаре ши жертфеле де бэутурэ обишнуите.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Ын зиуа а чинчспрезечя а луний а шаптя, сэ авець о адунаре сфынтэ; атунч сэ ну фачець ничо лукраре де слугэ. Сэ прэзнуиць о сэрбэтоаре ын чинстя Домнулуй тимп де шапте зиле.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Сэ адучець, ка ардере-де-тот, о жертфэ мистуитэ де фок, де ун мирос плэкут Домнулуй: трейспрезече вицей, дой бербечь ши пайспрезече мей де ун ан фэрэ кусур.
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Сэ май адэугаць ши дарул лор де мынкаре дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн, трей зечимь пентру фиекаре дин чей трейспрезече вицей, доуэ зечимь пентру фиекаре дин чей дой бербечь
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 ши о зечиме пентру фиекаре дин чей пайспрезече мей.
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфа са де бэутурэ.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 А доуа зи, сэ адучець дойспрезече вицей, дой бербечь ши пайспрезече мей де ун ан фэрэ кусур,
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 ымпреунэ ку дарул лор де мынкаре ши жертфеле лор де бэутурэ пентру вицей, бербечь ши мей, дупэ нумэрул лор, дупэ рындуелиле ашезате.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфеле де бэутурэ.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 А трея зи, сэ адучець унспрезече вицей, дой бербечь ши пайспрезече мей де ун ан фэрэ кусур,
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 ымпреунэ ку дарул лор де мынкаре ши жертфеле лор де бэутурэ пентру вицей, бербечь ши мей, дупэ нумэрул лор, дупэ рындуелиле ашезате.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфа де бэутурэ.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 А патра зи, сэ адучець зече вицей, дой бербечь ши пайспрезече мей де ун ан фэрэ кусур,
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 ымпреунэ ку дарул лор де мынкаре ши жертфеле лор де бэутурэ пентру вицей, бербечь ши мей, дупэ нумэрул лор, дупэ рындуелиле ашезате.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфа де бэутурэ.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Ын зиуа а чинчя, сэ адучець ноуэ вицей, дой бербечь ши пайспрезече мей де ун ан фэрэ кусур,
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 ымпреунэ ку дарул лор де мынкаре ши жертфеле лор де бэутурэ пентру вицей, бербечь ши мей, дупэ нумэрул лор, дупэ рындуелиле ашезате.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфа де бэутурэ.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Ын зиуа а шася, сэ адучець опт вицей, дой бербечь ши пайспрезече мей де ун ан фэрэ кусур,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 ымпреунэ ку дарул лор де мынкаре ши жертфеле лор де бэутурэ пентру вицей, бербечь ши мей, дупэ нумэрул лор, дупэ рындуелиле ашезате.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфеле де бэутурэ.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Ын зиуа а шаптя, сэ адучець шапте вицей, дой бербечь ши пайспрезече мей де ун ан фэрэ кусур,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 ымпреунэ ку дарул лор де мынкаре ши жертфеле лор де бэутурэ пентру вицей, бербечь ши мей, дупэ нумэрул лор, дупэ рындуелиле ашезате.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфа де бэутурэ.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Ын зиуа а опта, сэ авець о адунаре де сэрбэтоаре; атунч сэ ну фачець ничо лукраре де слугэ.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Сэ адучець ка ардере-де-тот о жертфэ мистуитэ де фок, де ун мирос плэкут Домнулуй: ун вицел, ун бербек ши шапте мей де ун ан, фэрэ кусур,
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 ымпреунэ ку дарул лор де мынкаре ши жертфеле лор де бэутурэ пентру вицел, бербек ши мей, дупэ нумэрул лор, дупэ рындуелиле ашезате.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Сэ адучець ши ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ, дарул ей де мынкаре ши жертфа де бэутурэ.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Ачестя сунт жертфеле пе каре сэ ле адучець Домнулуй ла сэрбэториле воастре, афарэ де ардериле воастре де тот, де даруриле воастре де мынкаре, де жертфеле воастре де бэутурэ ши де жертфеле воастре де мулцумире, ка ымплинире а уней журуинце сау ка дарурь де бунэвое.’”
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Мойсе а спус копиилор луй Исраел тот че-й порунчисе Домнул.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< Нумерь 29 >