< Нумерь 28 >

1 Домнул а ворбит луй Мойсе ши а зис:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 „Порунчеште копиилор луй Исраел ши спуне-ле: ‘Сэ авець грижэ сэ-Мь адучець, ла время хотэрытэ, дарул Меу де мынкаре, храна жертфелор Меле мистуите де фок, каре Ымь сунт де ун плэкут мирос.’
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 Сэ ле спуй: ‘Ятэ жертфа мистуитэ де фок пе каре о вець адуче Домнулуй: ын фиекаре зи, кыте дой мей де ун ан фэрэ кусур, ка ардере-де-тот некурматэ.
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 Сэ адучь ун мел диминяца ши челэлалт мел сяра,
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 яр, ка дар де мынкаре, сэ адучь а зечя парте динтр-о ефэ де флоаря фэиний фрэмынтатэ ынтр-ун сферт де хин де унтделемн де мэслине сфэрымате.
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 Ачаста есте ардеря-де-тот некурматэ каре а фост адусэ ла мунтеле Синай; о жертфэ мистуитэ де фок де ун мирос плэкут Домнулуй.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 Жертфа де бэутурэ сэ фие де ун сферт де хин пентру фиекаре мел; жертфа де бэутурэ де вин с-о фачь Домнулуй ын Локул Сфынт.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 Ал дойля мел сэ-л адучь сяра, ку ун дар де мынкаре ши о жертфэ де бэутурэ ка челе де диминяцэ; ачаста есте о жертфэ мистуитэ прин фок, де ун мирос плэкут Домнулуй.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 Ын зиуа Сабатулуй, сэ адучець дой мей де ун ан фэрэ кусур ши, ка дар де мынкаре, доуэ зечимь де ефэ дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн, ымпреунэ ку жертфа де бэутурэ.
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 Ачаста есте ардеря-де-тот пентру фиекаре зи де Сабат, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ ши жертфа ей де бэутурэ.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 Ла ынчепутул лунилор воастре, сэ адучець, ка ардере-де-тот Домнулуй, дой вицей, ун бербек ши шапте мей де ун ан фэрэ кусур
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 ши, ка дар де мынкаре пентру фиекаре вицел, трей зечимь де ефэ дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн; ка дар де мынкаре пентру бербек, сэ адучець доуэ зечимь де ефэ дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 ка дар де мынкаре пентру фиекаре мел, сэ адучець о зечиме де ефэ дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн. Ачаста есте о ардере-де-тот, о жертфэ мистуитэ де фок де ун мирос плэкут Домнулуй.
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 Жертфеле де бэутурэ сэ фие де о жумэтате де хин де вин пентру ун вицел, а трея парте динтр-ун хин пентру ун бербек ши ун сферт де хин пентру ун мел. Ачаста есте ардеря-де-тот пентру ынчепутул луний, ын фиекаре лунэ, ын тоате луниле анулуй.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 Сэ се адукэ Домнулуй ун цап ка жертфэ де испэшире, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ ши жертфа ей де бэутурэ.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 Ын луна ынтый, ын зиуа а пайспрезечя а луний, вор фи Паштеле Домнулуй.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 Зиуа а чинчспрезечя а ачестей лунь сэ фие о зи де сэрбэтоаре. Тимп де шапте зиле сэ се мэнынче азиме.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 Ын зиуа динтый, сэ фие о адунаре сфынтэ: сэ ну фачець ничо лукраре де слугэ ын еа.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 Сэ адучець ка ардере-де-тот Домнулуй о жертфэ мистуитэ де фок: дой вицей, ун бербек ши шапте мей де ун ан фэрэ кусур.
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 Сэ май адэугаць ши дарул лор де мынкаре дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн, трей зечимь де ефэ пентру ун вицел, доуэ зечимь пентру ун бербек
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 ши о зечиме пентру фиекаре дин чей шапте мей.
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 Сэ адучець ун цап ка жертфэ де испэшире, ка сэ факэ испэшире пентру вой.
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 Сэ адучець ачесте жертфе, афарэ де ардеря-де-тот де диминяцэ, каре есте о ардере-де-тот некурматэ.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 Сэ ле адучець ын фиекаре зи, тимп де шапте зиле, ка храна уней жертфе мистуите де фок, де ун мирос плэкут Домнулуй. Сэ фие адусе афарэ де ардеря-де-тот некурматэ ши жертфа ей де бэутурэ.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 Ын зиуа а шаптя сэ авець о адунаре сфынтэ: сэ ну фачець ничо лукраре де слугэ ын еа.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 Ын зиуа челор динтый роаде, кынд вець адуче Домнулуй ун дар де мынкаре, ла сэрбэтоаря ынкеерий сэптэмынилор, сэ авець о адунаре сфынтэ; сэ ну фачець ничо лукраре де слугэ ын еа.
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 Сэ адучець ка ардере-де-тот де ун мирос плэкут Домнулуй: дой вицей, ун бербек ши шапте мей де ун ан.
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 Сэ май адэугаць дарул лор де мынкаре дин флоаря фэиний фрэмынтатэ ку унтделемн, кыте трей зечимь де фиекаре вицел, доуэ зечимь пентру бербек
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 ши о зечиме пентру фиекаре дин чей шапте мей.
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 Сэ адучець ши ун цап, ка сэ факэ испэшире пентру вой.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 Сэ адучець ачесте жертфе, афарэ де ардеря-де-тот некурматэ ши дарул ей де мынкаре. Меий сэ фие фэрэ кусур ши сэ адэугаць ши жертфеле лор де бэутурэ.
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

< Нумерь 28 >