< Provérbios 10 >

1 Proverbios de Salomão. O filho sabio alegra a seu pae, mas o filho louco é a tristeza de sua mãe.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Os thesouros da impiedade de nada aproveitam; porém a justiça livra da morte.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 O Senhor não deixa ter fome a alma do justo, mas a fazenda dos impios rechaça.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 O que trabalha com mão enganosa empobrece, mas a mão dos diligentes enriquece.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 O que ajunta no verão é filho entendido, mas o que dorme na sega é filho que faz envergonhar.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Bençãos ha sobre a cabeça do justo, mas a violencia cobre a bocca dos impios.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 A memoria do justo é abençoada, mas o nome dos impios apodrecerá.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 O sabio de coração acceita os mandamentos, mas o louco de labios será transtornado.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Quem anda em sinceridade, anda seguro; mas o que perverte os seus caminhos será conhecido.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 O que acena com os olhos dá dôres, e o tolo de labios será transtornado.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 A bocca do justo é fonte de vida, mas a bocca dos impios cobre a violencia.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 O odio excita contendas, mas o amor cobre todas as transgressões.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 Nos labios do entendido se acha a sabedoria, mas a vara é para as costas do falto de entendimento.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 Os sabios escondem a sabedoria; mas a bocca do tolo está perto da ruina.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 A fazenda do rico é a cidade da sua fortaleza: a pobreza dos pobres é a sua ruina.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 A obra do justo conduz á vida, as novidades do impio ao peccado.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 O caminho para a vida é d'aquelle que guarda a correcção, mas o que deixa a reprehensão faz errar.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 O que encobre o odio tem labios falsos, e o que produz má fama é um insensato.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 Na multidão de palavras não ha falta de transgressão, mas o que modera os seus labios é prudente.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Prata escolhida é a lingua do justo: o coração dos impios é de nenhum preço.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Os labios do justo apascentam a muitos, mas os tolos, por falta de entendimento, morrem.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 A benção do Senhor é a que enriquece; e não lhe accrescenta dôres.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 Como brincadeira é para o tolo fazer abominação, mas sabedoria para o homem entendido.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 O temor do impio virá sobre elle, mas o desejo dos justos Deus lhe cumprirá.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Como passa a tempestade, assim o impio mais não é; mas o justo tem perpetuo fundamento.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Como vinagre para os dentes, como o fumo para os olhos, assim é o preguiçoso para aquelles que o mandam.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 O temor do Senhor augmenta os dias, mas os annos dos impios serão abreviados.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 A esperança dos justos é alegria, mas a expectação dos impios perecerá.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 O caminho do Senhor é fortaleza para os rectos, mas ruina será para os que obram iniquidade.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 O justo nunca jámais será abalado, mas os impios não habitarão a terra.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 A bocca do justo em abundancia produz sabedoria, mas a lingua da perversidade será desarreigada.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Os beiços do justo sabem o que agrada, mas a bocca dos impios anda cheia de perversidades.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Provérbios 10 >